< 2 Timoteyo 4 >

1 Pamaso pa Mulungu ndi pamaso pa Khristu Yesu, amene adzaweruza amoyo ndi akufa omwe pamene adzaonekera ndi ufumu wake, ndikukulamula kuti:
Rotim torej jaz pred Bogom in Gospodom Jezusom Kristusom, kateri bode kdaj sodil žive in mrtve po prihodu svojem in po kraljestvu svojem,
2 Lalikira Mawu; khala wokonzeka pa nthawi yake, ngakhale pamene si pa nthawi yake. Konza zolakwa zawo, dzudzula ndipo limbikitsa moleza mtima kwambiri ndi malangizo osamalitsa.
Razglašaj besedo, ne odjenjaj o priliki, nepriliki; svári, kaznuj, opominjaj v vsej potrpežljivosti in uku.
3 Pakuti idzafika nthawi imene anthu adzakana chiphunzitso choona. Mʼmalo mwake, chifukwa chokhumba kumva zowakomera zokha, adzasonkhanitsa aphunzitsi ambiri omawawuza zimene iwo akufuna kumva.
Kajti bode čas, ko ne bodo prenašali zdravega uka, nego po lastnem poželenji kopičili si učitelje, ker jih ušesa srbé.
4 Sadzafuna kumva choona koma adzafuna kumva nthano chabe.
In od resnice bodo odvračali ušesa in obračali se k basnim.
5 Koma iwe, khala tcheru nthawi zonse, pirira mʼzovuta, gwira ntchito ya mlaliki, gwira ntchito zonse za utumiki wako.
Ti pa bodi trezen v vsem, trpi, delo opravljaj evangelista, izpolnjuj službo svojo.
6 Pakuti moyo wanga wayamba kale kuthiridwa ngati nsembe, ndipo nthawi yakwana yoti ndinyamuke ulendo wanga.
Kajti jaz bodem skoraj žrtvovan, in ločitve moje čas je blizu.
7 Ndamenya nkhondo yabwino, ndatsiriza bwino mpikisano wa liwiro ndipo ndasunga chikhulupiriro.
Bojeval sem lepi boj, dopolnil ték, ohranil vero;
8 Tsopano mphotho yanga ikundidikira imene ndi chipewa cha chilungamo, imene Ambuye, woweruza wolungama, adzandipatsa pa tsiku lijalo, osati ine ndekha komanso onse amene akufunitsitsa kubwera kwake.
Že mi je pripravljen venec pravice, katerega mi podelí Gospod tisti dan, pravični sodnik; ne pa meni samo, nego tudi vsem, kateri so ljubili prihod njegov.
9 Uyesetse kubwera kuno msanga.
Prizadeni si, da prideš skoraj k meni.
10 Paja Dema anandisiya chifukwa chokonda dziko lapansi lino, ndipo anapita ku Tesalonika. Kresike anapita ku Galatiya ndipo Tito anapita ku Dalimatiya. (aiōn g165)
Kajti Dema me je zapustil iz ljubezni do tega sveta, in potoval je v Tesaloniko; Krescent v Galacijo, Tit v Dalmacijo; (aiōn g165)
11 Ndatsala ndi Luka yekha basi. Mutenge Marko ndipo ubwere naye kuno, chifukwa amandithandiza mu utumiki wanga.
Luka je sam pri meni. Marka vzemi in pripelji sè seboj, kajti koristen mi je za pomočnika.
12 Ndatumiza Tukiko ku Efeso.
Tihika pa sem poslal v Efez.
13 Pobwera, unditengere chofunda pamwamba chimene ndinachisiya kwa Kupro ku Trowa. Unditengerenso mabuku anga, makamaka aja azikopawa.
Plašč, ki sem ga pustil v Troadi pri Karpu, prinesi gredé, in knjige, zlasti pergamene.
14 Alekisandro, mmisiri wa zitsulo anandichitira zoyipa kwambiri. Ambuye adzamubwezera pa zimene anachita.
Aleksander kovač mi je storil mnogo hudega; povrni mu Gospod po delih njegovih!
15 Iwenso ukhale naye tcheru chifukwa anatsutsa kwambiri uthenga wathu.
Njega se tudi tí pazi, ker silno nasprotuje besedam našim.
16 Podziteteza koyamba pa mlandu wanga, panalibe ndi mmodzi yemwe amene anandithandiza, koma aliyense anandithawa. Mulungu awakhululukire.
O prvem zagovarjanji mojem ni mi bilo nikogar na strani, nego vsi so me bili zapustili; naj se jim ne všteva!
17 Koma Ambuye anayima nane limodzi, ndipo anandipatsa mphamvu, kuti kudzera mwa ine, uthenga ulalikidwe kwambiri, ndikuti anthu a mitundu ina amve. Ndipo ndinalanditsidwa mʼkamwa mwa mkango.
Gospod pa mi je bil na pómoč in ojačil me, da se po meni zvrši oznanilo, in ga čujejo vsi pogani; in otét sem bil levu iz žrela.
18 Ambuye adzandilanditsa ku chilichonse chofuna kundichita choyipa ndipo adzandisamalira bwino mpaka kundilowetsa chonse mu ufumu wake wakumwamba. Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya. (aiōn g165)
In otél me bode Gospod vsakega hudega dela in rešil v kraljestvo svoje nebeško; njemu slava na vekov veke! Amen. (aiōn g165)
19 Pereka moni kwa Prisila ndi Akura pamodzi ndi banja lonse la Onesiforo.
Pozdravi Prisko in Akvilo, in Onezifora hišo.
20 Erasto anatsalira ku Korinto. Trofimo ndinamusiya akudwala ku Mileto.
Erast je ostal v Korintu; Trofima pa sem pustil bolnega v Miletu.
21 Uyesetse kubwera kuno nthawi yozizira isanafike. Eubulo akupereka moni, ndiponso Pude, Lino, Klaudiya ndi abale onse nawonso akupereka moni.
Prizadeni si, da prideš pred zimo. Pozdravlja te Evbúl in Pudent in Lin in Klavdija in bratje vsi.
22 Ambuye akhale ndi mzimu wako. Chisomo chikhale ndi inu nonse.
Gospod Jezus Kristus z duhom tvojim! Milost z vami! Amen. Timoteju list drugi, prvemu glavarju izvoljenemu občine Efežanske, pisan iz Rima, ko je bil Pavel v drugič pred cesarjem Neronom.

< 2 Timoteyo 4 >