< 2 Timoteyo 2 >
1 Tsono iwe, mwana wanga, limbika mʼchisomo chimene chili mwa Khristu Yesu.
Отож, сину мій, зміцняйся в благода́ті, що в Христі Ісусі вона!
2 Ndipo zinthu zimene unamva ine ndikuziyankhula pamaso pa mboni zambiri, uziphunzitse kwa anthu odalirika amene akaphunzitsenso ena.
А що чув ти від мене при багатьо́х свідках, те передай вірним лю́дям, що будуть спроможні й інших навчити.
3 Umve nane zowawa, monga msilikali wa Khristu Yesu.
А ти терпи лихо, як добрий воя́к Христа Ісуса!
4 Palibe msilikali amene ali pa ntchito amagwiranso ntchito za anthu wamba, iye amafuna kukondweretsa bwana wolamulira.
Бо жоден воя́к не в'яжеться в справи життя, аби догодити тому, хто ві́йсько збирає.
5 Chimodzimodzinso, munthu amene ali pa mpikisano waliwiro, salandira mphotho ya wopambana pokhapokha atatsiriza monga mwa malamulo a mpikisanowo.
А як хто йде на зма́ги, то вінка́ не одержує, якщо незако́нно змага́ється.
6 Mlimi wolimbika ndi amene amayembekezereka kukhala woyambirira kulandira gawo la zokolola.
Трудящому хліборо́бові нале́житься першому покуштувати з плоду.
7 Lingalira zimene ndikunenazi, pakuti Ambuye adzakuzindikiritsa zonsezi.
Розумій, що́ я говорю́. А Госпо́дь нехай дасть тобі розум у всьому.
8 Kumbukira Yesu Khristu wochokera ku mtundu wa Davide kuti anauka kwa akufa. Uwu ndiye uthenga wanga wabwino
Пам'ятай про Ісуса Христа з насіння Дави́дового, що воскрес із мертвих, за моєю Єва́нгелією,
9 umene ndikuwuvutikira choterewu mpaka kumangidwa ndi maunyolo ngati wakuba. Koma mawu a Mulungu sanamangidwe ndi maunyolo.
за яку я терплю́ муки аж до ув'я́знення, як той злочи́нець. Але Сло́ва Божого не ув'язни́ти!
10 Choncho ndikupirira chilichonse chifukwa cha osankhidwa, kuti nawonso apulumutsidwe ndi Khristu Yesu ndi kulandira ulemerero wosatha. (aiōnios )
Через це перено́шу я все ради ви́браних, щоб і вони доступили спасі́ння, що в Христі Ісусі, зо славою вічною. (aiōnios )
11 Mawu oyenera kuwadalira ndi awa: Ngati ife tinafa naye pamodzi, tidzakhalanso moyo pamodzi naye.
Вірне слово: коли ра́зом із Ним ми померли, то й жи́тимемо ра́зом із Ним!
12 Ngati tinapirira, tidzalamuliranso naye pamodzi. Ngati ife timukana, Iye adzatikananso.
А коли терпимо́, то будемо ра́зом тако́ж царюва́ти. А коли відцураємось, то й Він відцурається нас!
13 Ngati ndife osakhulupirika, Iye adzakhalabe wokhulupirika popeza sangathe kudzikana.
А коли ми невірні, зостається Він вірним, бо не може зректися Само́го Себе!
14 Uziwakumbutsa anthu a Mulungu zinthu izi. Uwachenjeze pamaso pa Mulungu kuti asamakangane pa za mawu. Zimenezi nʼzopanda phindu ndipo zimangowononga amene akumvawo.
Нагадуй про це й заклинай перед Богом, щоб не спереча́лись словами, бо ніна́що воно, хіба слухача́м на руїну.
15 Uyesetse kukhala wovomerezeka pamaso pa Mulungu monga wantchito wopanda chifukwa chochitira manyazi amene amalalikira mawu achoonadi molondola.
Силку́йся поставити себе перед Богом гідним, працівнико́м бездоганним, що вірно навчає науки правди.
16 Upewe nkhani zopanda pake, zosalemekeza Mulungu, chifukwa anthu oyankhula zotere amanka napotokerapotokera.
Стережися ж базі́кань марни́х, бо вони ще більше провадять до безбожности,
17 Chiphunzitso chawo chidzafalikira ngati chilonda. Mwa anthuwa muli Humenayo ndi Fileto.
а їхнє слово, як рак, буде ши́ритися. Від таких Гімене́й і Філі́т,
18 Iwowa apatuka pa choonadi. Iwo amaphunzitsa kuti kuuka kwa akufa kunachitika kale, motero amawononga chikhulupiriro cha anthu ena.
що вони погрішилися в правді, казавши, що воскресі́ння було вже, і віру деяких руйнують.
19 Komabe maziko olimba, amene Mulungu anawayika ngokhazikika, ndipo mawu olembedwapo ndi awa: “Yehova amadziwa amene ndi ake,” ndiponso, “Aliyense amene amavomereza dzina la Ambuye ayenera kusiya zoyipa.”
Та однако стоїть міцна́ Божа основа та має печатку оцю: „Господь знає тих, хто Його“, та: „Нехай від неправди відсту́питься всякий, хто Господнє Ім'я́ називає!“
20 Mʼnyumba yayikulu simukhala ziwiya zagolide ndi zasiliva zokha, koma mumakhalanso zamtengo ndi zadothi. Zina zimakhala za ntchito yapamwamba, zina za ntchito wamba.
А в великому домі знахо́диться по́суд не тільки золотий та срібний, але й дерев'яний та гли́няний, і одні посу́дини на честь, а другі на не́честь.
21 Munthu akadziyeretsa nʼkusiya ntchito za wambazi, adzakhala chiwiya cha ntchito yapamwamba, woyeretsedwa, ndi waphindu kwa Ambuye wake, wokonzeka kugwira ntchito iliyonse yabwino.
Отож, хто від цього очистить себе, буде по́суд на честь, освя́чений, потрібний Володареві, приготова́ний на всяке добре ді́ло.
22 Thawa zilakolako zoyipa zachinyamata. Funafuna chilungamo, chikhulupiriro, chikondi ndi mtendere pamodzi ndi amene akuyitanira pa dzina la Ambuye ndi mtima osadetsedwa.
Стережися молодечих пожадли́востей, трима́йся праведности, віри, любови, миру з тими, хто Господа кличе від чистого серця.
23 Ukane matsutsano oyipa ndi opusa, chifukwa amayambitsa mikangano.
А від нерозумних та від невче́них змага́нь ухиляйся, знавши, що вони родять сварки́.
24 Ndiponso mtumiki wa Ambuye asamakangane ndi anthu, koma azikhala wachifundo kwa aliyense, wodziwa kuphunzitsa, osati wokalipakalipa.
А раб Господній не повинен свари́тись, але бути привітним до всіх, навча́льним, до ли́ха терпля́чим,
25 Otsutsana naye awalangize mofatsa, mwina Mulungu adzawapatsa mwayi woti asinthike ndi kuzindikira choonadi.
що навчав би противників із ла́гідністю, чи Бог їм не дасть покая́ння, щоб правду пізнати,
26 Motero nzeru zawo zidzabweramo, ndipo adzathawa msampha wa mdierekezi, amene anawagwira ukapolo kuti azichita zofuna zake.
щоб визволитися від сітки диявола, що він уловив їх для ро́блення волі своєї.