< 2 Timoteyo 2 >

1 Tsono iwe, mwana wanga, limbika mʼchisomo chimene chili mwa Khristu Yesu.
Toi donc, mon enfant, sois fortifié dans la grâce qui est en Jésus-Christ.
2 Ndipo zinthu zimene unamva ine ndikuziyankhula pamaso pa mboni zambiri, uziphunzitse kwa anthu odalirika amene akaphunzitsenso ena.
Ce que tu as entendu de moi en présence de nombreux témoins, confie-le à des hommes fidèles, capables d'instruire aussi les autres.
3 Umve nane zowawa, monga msilikali wa Khristu Yesu.
Il faut donc que tu supportes les épreuves comme un bon soldat de Jésus-Christ.
4 Palibe msilikali amene ali pa ntchito amagwiranso ntchito za anthu wamba, iye amafuna kukondweretsa bwana wolamulira.
Aucun soldat en service ne se mêle des affaires de la vie, afin de plaire à celui qui l'a enrôlé comme soldat.
5 Chimodzimodzinso, munthu amene ali pa mpikisano waliwiro, salandira mphotho ya wopambana pokhapokha atatsiriza monga mwa malamulo a mpikisanowo.
De même, si quelqu'un participe à un concours d'athlétisme, il n'est pas couronné s'il n'a pas concouru selon les règles.
6 Mlimi wolimbika ndi amene amayembekezereka kukhala woyambirira kulandira gawo la zokolola.
Le cultivateur qui travaille doit être le premier à recevoir une part des récoltes.
7 Lingalira zimene ndikunenazi, pakuti Ambuye adzakuzindikiritsa zonsezi.
Considérez ce que je dis, et que le Seigneur vous donne de l'intelligence en toutes choses.
8 Kumbukira Yesu Khristu wochokera ku mtundu wa Davide kuti anauka kwa akufa. Uwu ndiye uthenga wanga wabwino
Souviens-toi de Jésus-Christ, ressuscité des morts, de la descendance de David, selon ma Bonne Nouvelle,
9 umene ndikuwuvutikira choterewu mpaka kumangidwa ndi maunyolo ngati wakuba. Koma mawu a Mulungu sanamangidwe ndi maunyolo.
dans laquelle je souffre des privations jusqu'à être enchaîné comme un criminel. Mais la parole de Dieu n'est pas enchaînée.
10 Choncho ndikupirira chilichonse chifukwa cha osankhidwa, kuti nawonso apulumutsidwe ndi Khristu Yesu ndi kulandira ulemerero wosatha. (aiōnios g166)
C'est pourquoi je supporte tout à cause des élus, afin qu'eux aussi obtiennent le salut qui est en Jésus-Christ, avec la gloire éternelle. (aiōnios g166)
11 Mawu oyenera kuwadalira ndi awa: Ngati ife tinafa naye pamodzi, tidzakhalanso moyo pamodzi naye.
Cette parole est digne de foi: « Car si nous sommes morts avec lui, nous vivrons aussi avec lui.
12 Ngati tinapirira, tidzalamuliranso naye pamodzi. Ngati ife timukana, Iye adzatikananso.
Si nous endurons, nous régnerons aussi avec lui. Si nous le renions, il nous reniera aussi.
13 Ngati ndife osakhulupirika, Iye adzakhalabe wokhulupirika popeza sangathe kudzikana.
Si nous sommes infidèles, il reste fidèle; car il ne peut pas se renier. »
14 Uziwakumbutsa anthu a Mulungu zinthu izi. Uwachenjeze pamaso pa Mulungu kuti asamakangane pa za mawu. Zimenezi nʼzopanda phindu ndipo zimangowononga amene akumvawo.
Rappelle-leur ces choses, en leur recommandant, devant le Seigneur, de ne pas discuter inutilement des paroles, au détriment de ceux qui écoutent.
15 Uyesetse kukhala wovomerezeka pamaso pa Mulungu monga wantchito wopanda chifukwa chochitira manyazi amene amalalikira mawu achoonadi molondola.
Efforce-toi de te présenter devant Dieu, comme un ouvrier qui n'a pas à rougir, maniant avec soin la Parole de Vérité.
16 Upewe nkhani zopanda pake, zosalemekeza Mulungu, chifukwa anthu oyankhula zotere amanka napotokerapotokera.
Mais fuis les discours creux, car ils vont plus loin dans l'impiété,
17 Chiphunzitso chawo chidzafalikira ngati chilonda. Mwa anthuwa muli Humenayo ndi Fileto.
et ces discours-là se consument comme la gangrène. Parmi eux se trouvent Hyménée et Philète,
18 Iwowa apatuka pa choonadi. Iwo amaphunzitsa kuti kuuka kwa akufa kunachitika kale, motero amawononga chikhulupiriro cha anthu ena.
des hommes qui se sont égarés dans la vérité, en disant que la résurrection est déjà passée, et en renversant la foi de quelques-uns.
19 Komabe maziko olimba, amene Mulungu anawayika ngokhazikika, ndipo mawu olembedwapo ndi awa: “Yehova amadziwa amene ndi ake,” ndiponso, “Aliyense amene amavomereza dzina la Ambuye ayenera kusiya zoyipa.”
Cependant, le solide fondement de Dieu subsiste, ayant ce sceau: « Le Seigneur connaît ceux qui sont à lui » et « Que quiconque invoque le nom du Seigneur s'éloigne de l'iniquité ».
20 Mʼnyumba yayikulu simukhala ziwiya zagolide ndi zasiliva zokha, koma mumakhalanso zamtengo ndi zadothi. Zina zimakhala za ntchito yapamwamba, zina za ntchito wamba.
Dans une grande maison, il y a non seulement des vases d'or et d'argent, mais aussi des vases de bois et d'argile. Les uns sont pour l'honneur, les autres pour le déshonneur.
21 Munthu akadziyeretsa nʼkusiya ntchito za wambazi, adzakhala chiwiya cha ntchito yapamwamba, woyeretsedwa, ndi waphindu kwa Ambuye wake, wokonzeka kugwira ntchito iliyonse yabwino.
Si donc quelqu'un se purifie de ces derniers, il sera un vase d'honneur, sanctifié, propre à l'usage du maître, préparé pour toute bonne œuvre.
22 Thawa zilakolako zoyipa zachinyamata. Funafuna chilungamo, chikhulupiriro, chikondi ndi mtendere pamodzi ndi amene akuyitanira pa dzina la Ambuye ndi mtima osadetsedwa.
Fuyez les convoitises de la jeunesse, mais recherchez la justice, la foi, l'amour et la paix avec ceux qui invoquent le Seigneur d'un cœur pur.
23 Ukane matsutsano oyipa ndi opusa, chifukwa amayambitsa mikangano.
Mais refusez les interrogations insensées et ignorantes, sachant qu'elles engendrent des querelles.
24 Ndiponso mtumiki wa Ambuye asamakangane ndi anthu, koma azikhala wachifundo kwa aliyense, wodziwa kuphunzitsa, osati wokalipakalipa.
Le serviteur du Seigneur ne doit pas se disputer, mais être doux envers tous, capable d'enseigner, patient,
25 Otsutsana naye awalangize mofatsa, mwina Mulungu adzawapatsa mwayi woti asinthike ndi kuzindikira choonadi.
corrigeant avec douceur ceux qui s'opposent à lui. Peut-être Dieu leur donnera-t-il une repentance qui les amènera à la pleine connaissance de la vérité,
26 Motero nzeru zawo zidzabweramo, ndipo adzathawa msampha wa mdierekezi, amene anawagwira ukapolo kuti azichita zofuna zake.
et ils se ressaisiront du piège du diable, après avoir été emmenés par lui pour faire sa volonté.

< 2 Timoteyo 2 >