< 2 Timoteyo 2 >

1 Tsono iwe, mwana wanga, limbika mʼchisomo chimene chili mwa Khristu Yesu.
You then, my child, must be strong in the grace that is in Christ Jesus.
2 Ndipo zinthu zimene unamva ine ndikuziyankhula pamaso pa mboni zambiri, uziphunzitse kwa anthu odalirika amene akaphunzitsenso ena.
All that you have been taught by me in the hearing of many witnesses, you must hand on to trusty men who shall themselves, in turn, be competent to instruct others also.
3 Umve nane zowawa, monga msilikali wa Khristu Yesu.
As a good soldier of Christ Jesus accept your share of suffering.
4 Palibe msilikali amene ali pa ntchito amagwiranso ntchito za anthu wamba, iye amafuna kukondweretsa bwana wolamulira.
Every one who serves as a soldier keeps himself from becoming entangled in the world's business--so that he may satisfy the officer who enlisted him.
5 Chimodzimodzinso, munthu amene ali pa mpikisano waliwiro, salandira mphotho ya wopambana pokhapokha atatsiriza monga mwa malamulo a mpikisanowo.
And if any one takes part in an athletic contest, he gets no prize unless he obeys the rules.
6 Mlimi wolimbika ndi amene amayembekezereka kukhala woyambirira kulandira gawo la zokolola.
The harvestman who labours in the field must be the first to get a share of the crop.
7 Lingalira zimene ndikunenazi, pakuti Ambuye adzakuzindikiritsa zonsezi.
Mark well what I am saying: the Lord will give you discernment in everything.
8 Kumbukira Yesu Khristu wochokera ku mtundu wa Davide kuti anauka kwa akufa. Uwu ndiye uthenga wanga wabwino
Never forget that Jesus Christ has risen from among the dead and is a descendant of David, as is declared in the Good News which I preach.
9 umene ndikuwuvutikira choterewu mpaka kumangidwa ndi maunyolo ngati wakuba. Koma mawu a Mulungu sanamangidwe ndi maunyolo.
For preaching the Good News I suffer, and am even put in chains, as if I were a criminal: yet the word of God is not imprisoned.
10 Choncho ndikupirira chilichonse chifukwa cha osankhidwa, kuti nawonso apulumutsidwe ndi Khristu Yesu ndi kulandira ulemerero wosatha. (aiōnios g166)
For this reason I endure all things for the sake of God's own people; so that they also may obtain salvation--even the salvation which is in Christ Jesus--and with it eternal glory. (aiōnios g166)
11 Mawu oyenera kuwadalira ndi awa: Ngati ife tinafa naye pamodzi, tidzakhalanso moyo pamodzi naye.
Faithful is the saying: "If we died with Him, we shall also live with Him;
12 Ngati tinapirira, tidzalamuliranso naye pamodzi. Ngati ife timukana, Iye adzatikananso.
"If we patiently endure pain, we shall also share His Kingship; "If we disown Him, He will also disown us;
13 Ngati ndife osakhulupirika, Iye adzakhalabe wokhulupirika popeza sangathe kudzikana.
"And even if our faith fails, He remains true--He cannot prove false to Himself."
14 Uziwakumbutsa anthu a Mulungu zinthu izi. Uwachenjeze pamaso pa Mulungu kuti asamakangane pa za mawu. Zimenezi nʼzopanda phindu ndipo zimangowononga amene akumvawo.
Bring all this to men's remembrances, solemnly charging them in the presence of God not to waste time in wrangling about mere words, a course which is altogether unprofitable and tends only to the ruin of the hearers.
15 Uyesetse kukhala wovomerezeka pamaso pa Mulungu monga wantchito wopanda chifukwa chochitira manyazi amene amalalikira mawu achoonadi molondola.
Earnestly seek to commend yourself to God as a servant who, because of his straightforward dealing with the word of truth, has no reason to feel any shame.
16 Upewe nkhani zopanda pake, zosalemekeza Mulungu, chifukwa anthu oyankhula zotere amanka napotokerapotokera.
But from irreligious and frivolous talk hold aloof, for those who indulge in it will proceed from bad to worse in impiety,
17 Chiphunzitso chawo chidzafalikira ngati chilonda. Mwa anthuwa muli Humenayo ndi Fileto.
and their teaching will spread like a running sore. Hymenaeus and Philetus are men of that stamp.
18 Iwowa apatuka pa choonadi. Iwo amaphunzitsa kuti kuuka kwa akufa kunachitika kale, motero amawononga chikhulupiriro cha anthu ena.
In the matter of the truth they have gone astray, saying that the Resurrection is already past, and so they are overthrowing the faith of some.
19 Komabe maziko olimba, amene Mulungu anawayika ngokhazikika, ndipo mawu olembedwapo ndi awa: “Yehova amadziwa amene ndi ake,” ndiponso, “Aliyense amene amavomereza dzina la Ambuye ayenera kusiya zoyipa.”
Yet God's solid foundation stands unmoved, bearing this inscription, "The Lord knows those who really belong to Him." And this also, "Let every one who names the Name of the Lord renounce all wickedness."
20 Mʼnyumba yayikulu simukhala ziwiya zagolide ndi zasiliva zokha, koma mumakhalanso zamtengo ndi zadothi. Zina zimakhala za ntchito yapamwamba, zina za ntchito wamba.
Now in a great house there are not only articles of gold and silver, but also others of wood and of earthenware; and some are for specially honourable, and others for common use.
21 Munthu akadziyeretsa nʼkusiya ntchito za wambazi, adzakhala chiwiya cha ntchito yapamwamba, woyeretsedwa, ndi waphindu kwa Ambuye wake, wokonzeka kugwira ntchito iliyonse yabwino.
If therefore a man keeps himself clear of these latter, he himself will be for specially honourable use, consecrated, fit for the Master's service, and fully equipped for every good work.
22 Thawa zilakolako zoyipa zachinyamata. Funafuna chilungamo, chikhulupiriro, chikondi ndi mtendere pamodzi ndi amene akuyitanira pa dzina la Ambuye ndi mtima osadetsedwa.
Keep a strong curb, however, on your youthful cravings; and strive for integrity, good faith, love, peace, in company with all who pray to the Lord with pure hearts.
23 Ukane matsutsano oyipa ndi opusa, chifukwa amayambitsa mikangano.
But avoid foolish discussions with ignorant men, knowing--as you do--that these lead to quarrels;
24 Ndiponso mtumiki wa Ambuye asamakangane ndi anthu, koma azikhala wachifundo kwa aliyense, wodziwa kuphunzitsa, osati wokalipakalipa.
and a bondservant of the Lord must not quarrel, but must be inoffensive towards all men, a skilful teacher, and patient under wrongs.
25 Otsutsana naye awalangize mofatsa, mwina Mulungu adzawapatsa mwayi woti asinthike ndi kuzindikira choonadi.
He must speak in a gentle tone when correcting the errors of opponents, in the hope that God will at last give them repentance, for them to come to a full knowledge of the truth
26 Motero nzeru zawo zidzabweramo, ndipo adzathawa msampha wa mdierekezi, amene anawagwira ukapolo kuti azichita zofuna zake.
and recover sober-mindedness and freedom from the Devil's snare, though they are now entrapped by him to do his will.

< 2 Timoteyo 2 >