< 2 Timoteyo 2 >

1 Tsono iwe, mwana wanga, limbika mʼchisomo chimene chili mwa Khristu Yesu.
Thou therefore, my sonne, be strong in the grace that is in Christ Iesus.
2 Ndipo zinthu zimene unamva ine ndikuziyankhula pamaso pa mboni zambiri, uziphunzitse kwa anthu odalirika amene akaphunzitsenso ena.
And what things thou hast heard of me, by many witnesses, ye same deliuer to faithfull men, which shalbe able to teache other also.
3 Umve nane zowawa, monga msilikali wa Khristu Yesu.
Thou therefore suffer affliction as a good souldier of Iesus Christ.
4 Palibe msilikali amene ali pa ntchito amagwiranso ntchito za anthu wamba, iye amafuna kukondweretsa bwana wolamulira.
No man that warreth, entangleth himselfe with the affaires of this life, because he woulde please him that hath chosen him to be a souldier.
5 Chimodzimodzinso, munthu amene ali pa mpikisano waliwiro, salandira mphotho ya wopambana pokhapokha atatsiriza monga mwa malamulo a mpikisanowo.
And if any man also striue for a Masterie, he is not crowned, except he striue as he ought to doe.
6 Mlimi wolimbika ndi amene amayembekezereka kukhala woyambirira kulandira gawo la zokolola.
The husbandman must labour before he receiue the fruites.
7 Lingalira zimene ndikunenazi, pakuti Ambuye adzakuzindikiritsa zonsezi.
Consider what I say: and the Lord giue thee vnderstanding in all things:
8 Kumbukira Yesu Khristu wochokera ku mtundu wa Davide kuti anauka kwa akufa. Uwu ndiye uthenga wanga wabwino
Remember that Iesus Christ, made of the seede of Dauid, was raysed againe from the dead according to my Gospel,
9 umene ndikuwuvutikira choterewu mpaka kumangidwa ndi maunyolo ngati wakuba. Koma mawu a Mulungu sanamangidwe ndi maunyolo.
Wherein I suffer trouble as an euill doer, euen vnto bondes: but the worde of God is not bounde.
10 Choncho ndikupirira chilichonse chifukwa cha osankhidwa, kuti nawonso apulumutsidwe ndi Khristu Yesu ndi kulandira ulemerero wosatha. (aiōnios g166)
Therefore I suffer all things, for the elects sake, that they might also obtaine the saluation which is in Christ Iesus, with eternall glorie. (aiōnios g166)
11 Mawu oyenera kuwadalira ndi awa: Ngati ife tinafa naye pamodzi, tidzakhalanso moyo pamodzi naye.
It is a true saying, For if we be dead together with him, we also shall liue together with him.
12 Ngati tinapirira, tidzalamuliranso naye pamodzi. Ngati ife timukana, Iye adzatikananso.
If we suffer, we shall also reigne together with him: if we denie him, he also will denie vs.
13 Ngati ndife osakhulupirika, Iye adzakhalabe wokhulupirika popeza sangathe kudzikana.
If we beleeue not, yet abideth he faithfull: he cannot denie himselfe.
14 Uziwakumbutsa anthu a Mulungu zinthu izi. Uwachenjeze pamaso pa Mulungu kuti asamakangane pa za mawu. Zimenezi nʼzopanda phindu ndipo zimangowononga amene akumvawo.
Of these things put them in remembrance, and protest before the Lord, that they striue not about wordes, which is to no profit, but to the peruerting of the hearers.
15 Uyesetse kukhala wovomerezeka pamaso pa Mulungu monga wantchito wopanda chifukwa chochitira manyazi amene amalalikira mawu achoonadi molondola.
Studie to shewe thy selfe approued vnto God, a workeman that needeth not to be ashamed, diuiding the worde of trueth aright.
16 Upewe nkhani zopanda pake, zosalemekeza Mulungu, chifukwa anthu oyankhula zotere amanka napotokerapotokera.
Stay prophane, and vaine babblings: for they shall encrease vnto more vngodlinesse.
17 Chiphunzitso chawo chidzafalikira ngati chilonda. Mwa anthuwa muli Humenayo ndi Fileto.
And their worde shall fret as a canker: of which sort is Hymeneus and Philetus,
18 Iwowa apatuka pa choonadi. Iwo amaphunzitsa kuti kuuka kwa akufa kunachitika kale, motero amawononga chikhulupiriro cha anthu ena.
Which as concerning ye trueth haue erred from the marke, saying that the resurrection is past alreadie, and do destroy the faith of certaine.
19 Komabe maziko olimba, amene Mulungu anawayika ngokhazikika, ndipo mawu olembedwapo ndi awa: “Yehova amadziwa amene ndi ake,” ndiponso, “Aliyense amene amavomereza dzina la Ambuye ayenera kusiya zoyipa.”
But the foundation of God remaineth sure, and hath this seale, The Lord knoweth who are his: and, Let euery one that calleth on the Name of Christ, depart from iniquitie.
20 Mʼnyumba yayikulu simukhala ziwiya zagolide ndi zasiliva zokha, koma mumakhalanso zamtengo ndi zadothi. Zina zimakhala za ntchito yapamwamba, zina za ntchito wamba.
Notwithstanding in a great house are not onely vessels of gold and of siluer, but also of wood and of earth, and some for honour, and some vnto dishonour.
21 Munthu akadziyeretsa nʼkusiya ntchito za wambazi, adzakhala chiwiya cha ntchito yapamwamba, woyeretsedwa, ndi waphindu kwa Ambuye wake, wokonzeka kugwira ntchito iliyonse yabwino.
If any man therefore purge him selfe from these, he shalbe a vessell vnto honour, sanctified, and meete for the Lord, and prepared vnto euery good worke.
22 Thawa zilakolako zoyipa zachinyamata. Funafuna chilungamo, chikhulupiriro, chikondi ndi mtendere pamodzi ndi amene akuyitanira pa dzina la Ambuye ndi mtima osadetsedwa.
Flee also from the lustes of youth, and follow after righteousnes, faith, loue, and peace, with them that call on the Lord with pure heart,
23 Ukane matsutsano oyipa ndi opusa, chifukwa amayambitsa mikangano.
And put away foolish and vnlearned questions, knowing that they ingender strife.
24 Ndiponso mtumiki wa Ambuye asamakangane ndi anthu, koma azikhala wachifundo kwa aliyense, wodziwa kuphunzitsa, osati wokalipakalipa.
But the seruant of ye Lord must not striue, but must be gentle toward all men, apt to teache, suffering the euill,
25 Otsutsana naye awalangize mofatsa, mwina Mulungu adzawapatsa mwayi woti asinthike ndi kuzindikira choonadi.
Instructing them with meekenesse that are contrary minded, prouing if God at any time will giue them repentance, that they may acknowledge the trueth,
26 Motero nzeru zawo zidzabweramo, ndipo adzathawa msampha wa mdierekezi, amene anawagwira ukapolo kuti azichita zofuna zake.
And come to amendment out of that snare of the deuil, of whom they are taken prisoners, to doe his will.

< 2 Timoteyo 2 >