< 2 Timoteyo 2 >

1 Tsono iwe, mwana wanga, limbika mʼchisomo chimene chili mwa Khristu Yesu.
Ti se dakle, dijete moje, jačaj milošću u Kristu Isusu
2 Ndipo zinthu zimene unamva ine ndikuziyankhula pamaso pa mboni zambiri, uziphunzitse kwa anthu odalirika amene akaphunzitsenso ena.
i što si od mene po mnogim svjedocima čuo, to predaj vjernim ljudima koji će biti podobni i druge poučiti.
3 Umve nane zowawa, monga msilikali wa Khristu Yesu.
S njima se zlopati kao dobar vojnik Krista Isusa.
4 Palibe msilikali amene ali pa ntchito amagwiranso ntchito za anthu wamba, iye amafuna kukondweretsa bwana wolamulira.
Tko vojuje, ne zapleće se u svagdanje poslove kako bi se vojskovođi svidio.
5 Chimodzimodzinso, munthu amene ali pa mpikisano waliwiro, salandira mphotho ya wopambana pokhapokha atatsiriza monga mwa malamulo a mpikisanowo.
I natječe li se tko, ne ovjenčava se ako se zakonito ne natječe.
6 Mlimi wolimbika ndi amene amayembekezereka kukhala woyambirira kulandira gawo la zokolola.
Ratar koji se trudi treba da prvi primi od uroda.
7 Lingalira zimene ndikunenazi, pakuti Ambuye adzakuzindikiritsa zonsezi.
Shvati što govorim! Ta dat će ti Gospodin razum u svemu.
8 Kumbukira Yesu Khristu wochokera ku mtundu wa Davide kuti anauka kwa akufa. Uwu ndiye uthenga wanga wabwino
Spominji se Isusa Krista, uskrsla od mrtvih, od potomstva Davidova - po mojem evanđelju.
9 umene ndikuwuvutikira choterewu mpaka kumangidwa ndi maunyolo ngati wakuba. Koma mawu a Mulungu sanamangidwe ndi maunyolo.
Za nj se ja zlopatim sve do okova, kao zločinac. Ali riječ Božja nije okovana!
10 Choncho ndikupirira chilichonse chifukwa cha osankhidwa, kuti nawonso apulumutsidwe ndi Khristu Yesu ndi kulandira ulemerero wosatha. (aiōnios g166)
Stoga sve podnosim radi izabranih, da i oni postignu spasenje, spasenje u Kristu Isusu, zajedno s vječnom slavom. (aiōnios g166)
11 Mawu oyenera kuwadalira ndi awa: Ngati ife tinafa naye pamodzi, tidzakhalanso moyo pamodzi naye.
Vjerodostojna je riječ: Ako s njime umrijesmo, s njime ćemo i živjeti.
12 Ngati tinapirira, tidzalamuliranso naye pamodzi. Ngati ife timukana, Iye adzatikananso.
Ako ustrajemo, s njime ćemo i kraljevati. Ako ga zaniječemo, i on će zanijekati nas.
13 Ngati ndife osakhulupirika, Iye adzakhalabe wokhulupirika popeza sangathe kudzikana.
Ako ne budemo vjerni, on vjeran ostaje. Ta ne može sebe zanijekati!
14 Uziwakumbutsa anthu a Mulungu zinthu izi. Uwachenjeze pamaso pa Mulungu kuti asamakangane pa za mawu. Zimenezi nʼzopanda phindu ndipo zimangowononga amene akumvawo.
Na to podsjećaj zaklinjući pred Bogom neka ne bude rječoborstva: ničemu ne koristi, a na propast je onima koji slušaju.
15 Uyesetse kukhala wovomerezeka pamaso pa Mulungu monga wantchito wopanda chifukwa chochitira manyazi amene amalalikira mawu achoonadi molondola.
Uznastoj da kao prokušan staneš pred Boga kao radnik koji se nema čega stidjeti, koji ispravno reže riječ istine.
16 Upewe nkhani zopanda pake, zosalemekeza Mulungu, chifukwa anthu oyankhula zotere amanka napotokerapotokera.
Svjetovnih se pak praznorječja kloni: sve će više provaljivati prema bezbožnosti
17 Chiphunzitso chawo chidzafalikira ngati chilonda. Mwa anthuwa muli Humenayo ndi Fileto.
i riječ će njihova kao rak-rana izgrizati. Od njih su Himenej i Filet,
18 Iwowa apatuka pa choonadi. Iwo amaphunzitsa kuti kuuka kwa akufa kunachitika kale, motero amawononga chikhulupiriro cha anthu ena.
koji zastraniše od istine tvrdeći da je uskrsnuće već bilo te nekima prevraćaju vjeru.
19 Komabe maziko olimba, amene Mulungu anawayika ngokhazikika, ndipo mawu olembedwapo ndi awa: “Yehova amadziwa amene ndi ake,” ndiponso, “Aliyense amene amavomereza dzina la Ambuye ayenera kusiya zoyipa.”
Ipak čvrsti temelj Božji stoji - pod ovim je pečatom: Poznaje Gospodin one koji su njegovi i neka se kloni zloće tko god imenuje ime Gospodnje.
20 Mʼnyumba yayikulu simukhala ziwiya zagolide ndi zasiliva zokha, koma mumakhalanso zamtengo ndi zadothi. Zina zimakhala za ntchito yapamwamba, zina za ntchito wamba.
Pa u velikoj kući ima posuda ne samo zlatnih i srebrnih, nego i drvenih i glinenih; i jedne su časne, druge pak nečasne.
21 Munthu akadziyeretsa nʼkusiya ntchito za wambazi, adzakhala chiwiya cha ntchito yapamwamba, woyeretsedwa, ndi waphindu kwa Ambuye wake, wokonzeka kugwira ntchito iliyonse yabwino.
Očisti li se dakle tko od toga, bit će posuda časna, posvećena, korisna Gospodaru, za svako dobro djelo prikladna.
22 Thawa zilakolako zoyipa zachinyamata. Funafuna chilungamo, chikhulupiriro, chikondi ndi mtendere pamodzi ndi amene akuyitanira pa dzina la Ambuye ndi mtima osadetsedwa.
A mladenačkih se strastvenosti kloni! Teži za pravednošću, vjerom, ljubavlju, mirom sa svima koji iz čista srca prizivlju Gospodina.
23 Ukane matsutsano oyipa ndi opusa, chifukwa amayambitsa mikangano.
Lude pak i neobuzdane raspre odbijaj znajući da rađaju svađama.
24 Ndiponso mtumiki wa Ambuye asamakangane ndi anthu, koma azikhala wachifundo kwa aliyense, wodziwa kuphunzitsa, osati wokalipakalipa.
A sluga Gospodnji treba da se ne svađa, nego da bude nježan prema svima, sposoban poučavati, zlo podnositi,
25 Otsutsana naye awalangize mofatsa, mwina Mulungu adzawapatsa mwayi woti asinthike ndi kuzindikira choonadi.
da s blagošću preodgaja protivnike, ne bi li ih Bog podario obraćenjem te spoznaju istinu
26 Motero nzeru zawo zidzabweramo, ndipo adzathawa msampha wa mdierekezi, amene anawagwira ukapolo kuti azichita zofuna zake.
i ponovno budu trijezni izvan zamke đavla koji ih drži robljem svoje volje.

< 2 Timoteyo 2 >