< 2 Timoteyo 1 >

1 Paulo mtumwi wa Khristu Yesu mwa chifuniro cha Mulungu. Anandituma kuti ndilalike za lonjezo la moyo umene uli mwa Khristu Yesu.
Pavel, po Božji volji apostol Jezusa Kristusa, glede na obljubo življenja, ki je v Kristusu Jezusu,
2 Kwa Timoteyo, mwana wanga wokondedwa: Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye athu Yesu Khristu.
Timóteju, mojemu srčno ljubljenemu sinu: ›Milost, usmiljenje in mir od Boga Očeta in Kristusa Jezusa, našega Gospoda.‹
3 Ndikuyamika Mulungu amene ndimamutumikira ndi chikumbumtima chosatsutsika, monga momwe ankachitira makolo anga. Usiku ndi usana ndimakukumbukira mosalekeza mʼmapemphero anga.
Zahvaljujem se Bogu, ki mu služim s čisto vestjo od svojih pradedov, da se te brez prenehanja, noč in dan, spominjam v svojih molitvah
4 Ndikamakumbukira misozi yako, ndimalakalaka nditakuona kuti ndidzazidwe ndi chimwemwe.
in silno si želim, da te vidim, zavedajoč se tvojih solz, da bom lahko izpolnjen z radostjo;
5 Ndakumbukira za chikhulupiriro chako choona chimene chinayamba mwa agogo ako a Loisi ndi mwa amayi ako Yunike ndipo ndikutsimikiza mtima kuti chilinso mwa iwe.
ko se spominjam nehlinjene vere, ki je v tebi, ki je najprej prebivala v tvoji stari materi Loídi in tvoji materi Evníki; in prepričan sem, da tudi v tebi.
6 Nʼchifukwa chake ndikukukumbutsa kuti upemerere monga amachitira moto, mphatso imene Mulungu anakupatsa nditakusanjika manja.
Zatorej te spominjam, da razvnameš Božji dar, ki je v tebi po polaganju mojih rok.
7 Pakuti Mzimu amene Mulungu anatipatsa, si Mzimu wotipatsa manyazi, koma Mzimu wotipatsa mphamvu, chikondi ndi kudzisunga.
Kajti Bog nam ni dal duha strahu, temveč moči, ljubezni in zdravega razuma.
8 Choncho usachite manyazi kuchitira umboni Ambuye athu, kapena kuchita manyazi chifukwa cha ine wamʼndende. Koma umve nane zowawa chifukwa cha Uthenga Wabwino, mothandizidwa ndi mphamvu za Mulungu.
Ti se torej ne sramuj pričevanja o našem Gospodu niti o meni, njegovem jetniku, temveč bodi soudeleženec trpljenj evangelija glede na Božjo moč;
9 Iye anatipulumutsa ndipo anatiyitanira ku moyo oyera mtima, osati chifukwa cha chilichonse chimene tinachita, koma chifukwa cha chikonzero ndi chisomo chake. Chisomo chimenechi anatipatsa ife mwa Khristu Yesu nthawi isanayambe. (aiōnios g166)
ki nas je rešil in nas poklical s sveto poklicanostjo, ne glede na naša dela, temveč glede na svoj lastni namen in milost, ki nam je bila dana v Kristusu Jezusu pred začetkom sveta, (aiōnios g166)
10 Koma tsopano Mulungu watiwululira kudzera mʼkuoneka kwa Mpulumutsi wathu, Khristu Yesu, amene anathetsa mphamvu za imfa ndipo mwa Uthenga Wabwino anaonetsa poyera moyo umene sungafe.
toda sedaj je prikazana s pojavitvijo našega Odrešenika Jezusa Kristusa, ki je odpravil smrt in po evangeliju prinesel življenje in nesmrtnost na svetlobo.
11 Ine ndinasankhidwa kukhala wamthenga, ndi mtumwi ndi mphunzitsi wa Uthenga Wabwinowu.
Kateremu sem bil jaz določen za pridigarja in apostola in učitelja poganov.
12 Nʼchifukwa chake ndikuvutika monga ndililimu. Komabe zimenezi sizikundichititsa manyazi, popeza ndikumudziwa amene ndamukhulupirira ndipo ndikutsimikiza mtima kuti akhoza kusamalira chimene ndinamusungitsa mpaka tsiku lijalo.
Zaradi tega razloga tudi trpim te stvari. Pa vendar nisem osramočen, ker vem, komu sem veroval in prepričan sem, da je on zmožen obdržati to, kar sem mu izročil, za tisti dan.
13 Zimene unamva kwa ine, uzisunge kuti zikhale chitsanzo cha chiphunzitso choona, mwa chikhulupiriro ndi chikondi mwa Khristu Yesu.
Trdno drži vzorec zdravih besed, ki si jih slišal od mene, v veri in ljubezni, ki je v Kristusu Jezusu.
14 Samalira bwino zokoma zimene anakusungitsa. Uzisamalire mothandizidwa ndi Mzimu Woyera amene amakhala mwa ife.
To dobro stvar, ki ti je bila zaupana, varuj s Svetim Duhom, ki prebiva v nas.
15 Iwe udziwa kuti onse a mʼchigawo cha Asiya anandithawa, kuphatikizapo Fugelo ndi Herimogene omwe.
To veš, da so se vsi, ki so v Aziji, obrnili proč od mene; izmed katerih sta Figel in Hermógen.
16 Mulungu achitire chifundo banja lonse la Onesiforo chifukwa ankandisangalatsa kawirikawiri ndipo sankachita nane manyazi ngakhale ndinali womangidwa ndi maunyolo.
Gospod naj da usmiljenje Onezíforjevi hiši, kajti pogosto me je poživil in ni bil osramočen zaradi mojih verig.
17 Mʼmalo mwake, atangofika ku Roma, anandifunafuna ndipo anandipeza.
Toda ko je bil v Rimu, me je zelo marljivo iskal in me našel.
18 Ambuye amulole kuti adzalandire chifundo kwa Ambuye pa tsiku lijalo! Ukudziwa bwino momwe iye anandithandizira mʼnjira zosiyanasiyana ku Efeso.
Gospod naj mu zagotovi, da bo na tisti dan lahko našel usmiljenje od Gospoda. In ti zelo dobro veš, v kako mnogih stvareh mi je služil v Efezu.

< 2 Timoteyo 1 >