< 2 Timoteyo 1 >
1 Paulo mtumwi wa Khristu Yesu mwa chifuniro cha Mulungu. Anandituma kuti ndilalike za lonjezo la moyo umene uli mwa Khristu Yesu.
Mina Phawuli, umpostoli kaKhristu uJesu ngentando kaNkulunkulu, mayelana lesithembiso sokuphila okukuKhristu uJesu,
2 Kwa Timoteyo, mwana wanga wokondedwa: Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye athu Yesu Khristu.
KuThimothi, indodana yami ethandekayo ngithi: Umusa lesihawu kanye lokuthula okuvela kuNkulunkulu uBaba lakuKhristu uJesu iNkosi yethu.
3 Ndikuyamika Mulungu amene ndimamutumikira ndi chikumbumtima chosatsutsika, monga momwe ankachitira makolo anga. Usiku ndi usana ndimakukumbukira mosalekeza mʼmapemphero anga.
Ngiyambonga uNkulunkulu engimkhonzayo njengokwenziwa ngokhokho bami ngesazela esimsulwa lapho ngikukhumbula kokuphela emikhulekweni yami ebusuku lemini.
4 Ndikamakumbukira misozi yako, ndimalakalaka nditakuona kuti ndidzazidwe ndi chimwemwe.
Lapho ngikhumbula inyembezi zakho, ngifisa ukukubona ukuze ngibe lokuthokoza okukhulu.
5 Ndakumbukira za chikhulupiriro chako choona chimene chinayamba mwa agogo ako a Loisi ndi mwa amayi ako Yunike ndipo ndikutsimikiza mtima kuti chilinso mwa iwe.
Ngikhunjuzwe ngokukholwa kwakho okuqotho okwaqala kugogo wakho uLoyisi lakunyoko uYunisi njalo ngiyathemba ukuba khathesi kukhona lakuwe futhi.
6 Nʼchifukwa chake ndikukukumbutsa kuti upemerere monga amachitira moto, mphatso imene Mulungu anakupatsa nditakusanjika manja.
Ngenxa yalokhu ngiyakukhumbuza ukuba sihlale sivutha isipho sikaNkulunkulu owasamukela ngokubekwa kwezandla zami phezu kwakho.
7 Pakuti Mzimu amene Mulungu anatipatsa, si Mzimu wotipatsa manyazi, koma Mzimu wotipatsa mphamvu, chikondi ndi kudzisunga.
Ngoba uNkulunkulu kasiphanga umoya wobugwala kodwa umoya wamandla, lowothando kanye lowokuzithiba.
8 Choncho usachite manyazi kuchitira umboni Ambuye athu, kapena kuchita manyazi chifukwa cha ine wamʼndende. Koma umve nane zowawa chifukwa cha Uthenga Wabwino, mothandizidwa ndi mphamvu za Mulungu.
Ngakho-ke, ungabi lenhloni ukufakaza ngeNkosi yethu loba ube lenhloni ngami isibotshwa sayo. Kodwa hlanganyela lami ekuhluphekeleni ivangeli ngamandla kaNkulunkulu
9 Iye anatipulumutsa ndipo anatiyitanira ku moyo oyera mtima, osati chifukwa cha chilichonse chimene tinachita, koma chifukwa cha chikonzero ndi chisomo chake. Chisomo chimenechi anatipatsa ife mwa Khristu Yesu nthawi isanayambe. (aiōnios )
owasisindisayo, wasibizela ekuphileni okungcwele kungayisikho kuthi kukhona esakwenzayo kodwa ngenxa yenjongo yakhe langomusa wakhe. Umusa lo sawunikwa ngoKhristu uJesu ngaphambi kokuqala kwesikhathi (aiōnios )
10 Koma tsopano Mulungu watiwululira kudzera mʼkuoneka kwa Mpulumutsi wathu, Khristu Yesu, amene anathetsa mphamvu za imfa ndipo mwa Uthenga Wabwino anaonetsa poyera moyo umene sungafe.
kodwa khathesi usubonakaliswe ngokubonakala koMsindisi wethu uKhristu Jesu, osechithe ukufa waletha ekukhanyeni ukuphila lokungafi ngevangeli.
11 Ine ndinasankhidwa kukhala wamthenga, ndi mtumwi ndi mphunzitsi wa Uthenga Wabwinowu.
Njalo ivangeli leli mina ngabekwa ukuba yisithunywa lompostoli kanye lomfundisi walo.
12 Nʼchifukwa chake ndikuvutika monga ndililimu. Komabe zimenezi sizikundichititsa manyazi, popeza ndikumudziwa amene ndamukhulupirira ndipo ndikutsimikiza mtima kuti akhoza kusamalira chimene ndinamusungitsa mpaka tsiku lijalo.
Yikho-nje ngihlupheka njengoba nginje. Kodwa kangilanhloni ngoba ngiyamazi engikholwa kuye njalo ngiyakholwa ukuthi ulamandla okulondoloza lokho engikubeke kuye ngalolosuku.
13 Zimene unamva kwa ine, uzisunge kuti zikhale chitsanzo cha chiphunzitso choona, mwa chikhulupiriro ndi chikondi mwa Khristu Yesu.
Lokho owakuzwa ngami kugcine njengesibonelo semfundiso epheleleyo, ngokukholwa langothando kuKhristu uJesu.
14 Samalira bwino zokoma zimene anakusungitsa. Uzisamalire mothandizidwa ndi Mzimu Woyera amene amakhala mwa ife.
Londoloza isibambiso osiphathisiweyo usilondoloze ngosizo lukaMoya oNgcwele ohlala phakathi kwethu.
15 Iwe udziwa kuti onse a mʼchigawo cha Asiya anandithawa, kuphatikizapo Fugelo ndi Herimogene omwe.
Uyakwazi ukuthi abantu bonke esabelweni sase-Ezhiya sebangidela, kubalwa loFigelusi kanye loHemogenesi.
16 Mulungu achitire chifundo banja lonse la Onesiforo chifukwa ankandisangalatsa kawirikawiri ndipo sankachita nane manyazi ngakhale ndinali womangidwa ndi maunyolo.
Sengathi iNkosi ingaba lomusa kwabendlu ka-Onesiforosi ngoba wayehlala engivuselela njalo wayengelanhloni ngezibopho zami.
17 Mʼmalo mwake, atangofika ku Roma, anandifunafuna ndipo anandipeza.
Kodwa kwathi eseRoma wangidinga kakhulu waze wangithola.
18 Ambuye amulole kuti adzalandire chifundo kwa Ambuye pa tsiku lijalo! Ukudziwa bwino momwe iye anandithandizira mʼnjira zosiyanasiyana ku Efeso.
Sengathi iNkosi ingenza ukuba athole umusa eNkosini ngalolosuku! Uyakwazi kakuhle ukuba wangisiza ngezindlela ezinengi kangakanani e-Efesu.