< 2 Atesalonika 3 >
1 Potsiriza, abale, mutipempherere kuti uthenga wa Ambuye ufalikire msanga ndi kulemekezedwa monga momwe munachitira inu.
S'uwatsno ti eshwotso! itokere wottsok'o doonzo aap'tso káári jamok borr b́ mangitwok'o noosh Ik'o k'onuwere.
2 Ndipo pempherani kuti tilanditsidwe mʼmanja mwa anthu ovuta ndi oyipa, pakuti si onse amene ali nacho chikhulupiriro.
Mank'owere jam asho amankaaliye, mansh weri gondetswotsnat gond ashuwotsatse no faritwok'o noosh Ik'o k'onuwere.
3 Koma Ambuye ndi wokhulupirika, ndipo adzakulimbikitsani ndi kukutetezani kwa woyipayo.
Doonzonmó amaneke, bí itn kup'shitwe, gondatsnowere itn kotetwe.
4 Tili ndi chikhulupiriro mwa Ambuye kuti mukuchita zonse ndipo mudzapitirira kuchita zimene tinakulamulirani.
Itn no azazitwo and wotowa shino maants it k'alitwok'o it jangosh doonzo ats amanatniye.
5 Ambuye atsogolere mitima yanu kuti mudziwe chikondi cha Mulungu ndiponso kupirira kumene Khristu amapereka.
Doonzonú it nibo Ik' shúnonat Krstos k'amo maants jishwe.
6 Abale, tikukulamulani mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu, kuti mupewe mʼbale aliyense amene ndi waulesi ndi wachisokonezo, wosafuna kutsata zimene tinakuphunzitsani.
Tí eshúwotso! fin bitstsk wottsonat nookere itsh beeshiyets danok'on beeraw krstiyani jamatse it galetwok'o doonzo Iyesus Krstos shútson itn azazerone.
7 Pakuti inu mukudziwa zimene muyenera kuchita pofuna kutitsatira. Ife sitinali alesi pamene tinali nanu
Noon aro itsh b́k'anitwok'o it it tookonor danfte, noo itnton noteshor fino biitstswotsi teyatsone,
8 ndipo sitinadye chakudya cha aliyense osalipira. Komatu tinkagwira ntchito mwamphamvu usiku ndi usana kuti tisakhale cholemetsa kwa aliyense.
Kon mishonor datsmec'ron mááratsone, dabnwor ititse konatsor kuro nowoterawok'owa etaat t'uwe aawo no maawfetsosha nofinefoni.
9 Sitinachite zimenezi chifukwa choti tinalibe mphamvu zolamula kuti mutithandize koma kuti tikhale chitsanzo choti mutsatire.
Mank'o nok'alwere it noon araar no jafrats it sha'iitwok'owa etaatni bako itkooke tep'o dek'o noosh b́ faletwok'o daratniyaliye.
10 Pakuti ngakhale pamene tinali nanu, tinakupatsani lamulo lakuti, “Munthu wosafuna kugwira ntchito, asadye.”
Itnton noteshor «Fin finosh geerawo maak'aye» etts niwo itsh imrone b́ teshi.
11 Ife tikumva kuti pakati panu pali ena amene ndi alesi. Iwo safuna kugwira ntchito, koma amangolowerera pa za eni.
Han noo etwere ititsere ik ik fin biitstswots bo fa'ok'o t shishtsotsne, ashaanots boon geraw keewots kinda bako botookon eegor fineratsne.
12 Mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu, tikuwalamula ndi kuwakakamiza kuti azigwira ntchito mwabata ndi kumadya chakudya chodzigwirira ntchito okha.
Hank'o ashuwots s'ker beyar bo finitwok'o bín bo beetwo bodaatsitwok'o doonzo Iyesus Krstos shútson hanotsk'o ashuwotsi azazerone, izitwone.
13 Koma inu abale, musatope nʼkuchita zabwino.
Itmó ti eshúwotso! shaatsrone err sheeng fin finosh nefk'ayere.
14 Ngati wina aliyense akana kumvera malangizo athu a mʼkalatayi, mumuonetsetse ameneyo ndipo musayanjane naye kuti achite manyazi.
Woshanitse itsh nobeshits izo de'aw asho b́ beyal hank'o ashaan t'iwintswere, b́ jitsitwok'owere bínton gonkek'ayere.
15 Komatu musamutenge kukhala mdani, koma muchenjezeni ngati mʼbale.
B́ wotefere eshúwok'o izwere bako t'alatok'o taawk'ayere.
16 Tsopano Ambuye mwini mtendere akupatseni mtendere nthawi zonse mwa njira iliyonse. Ambuye akhale ndi inu nonse.
Jeeni doonzo b́ tookon jam aawo jam keewon jeeno itsh ime, doonzo it únetsnton wotowe.
17 Ine Paulo, ndikulemba malonje awa ndi dzanja langa, chimene ndi chizindikiro chodziwika mʼmakalata anga onse. Umo ndi mmene ndimalembera.
Jamán t kishon itsh guut'tso taane P'awlosiye, t wosh jamotse daatset wosho tik b́wti milikito haniye. T guut'etwere hank'owe.
18 Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale ndi inu nonse.
No doonz Iyesus Krstos s'aato it únetsnton wotowe.