< 2 Atesalonika 2 >
1 Pa za kubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu ndiponso za kusonkhana kwathu kuti tikumane naye, abale, tikukupemphani
Men vi bede eder, Brødre! angående vor Herres Jesu Kristi Tilkommelse og vor Samling til ham,
2 kuti musagwedezeke msanga mʼmaganizo kapena kuopsezedwa ndi uneneri, mbiri kapena kalata yokhala ngati yachokera kwa ife, yonena kuti tsiku lija la Ambuye linafika kale.
at I ikke i en Hast må lade eder bringe fra Besindelse eller forskrække hverken ved nogen Ånd eller ved nogen Tale eller Brev, der skulde være fra os, som om Herrens Dag var lige for Hånden.
3 Musalole kuti wina aliyense akunamizeni mwa njira ina iliyonse. Pakuti tsikulo lisanafike, kudzakhala mpatuko waukulu kwambiri, ndipo kudzaoneka munthu woyipitsitsa uja, munthu woyenera kuwonongedwayo.
Lad ingen bedrage eder i nogen Måde; thi først må jo Frafaldet komme og Syndens Menneske åbenbares, Fortabelsens Søn,
4 Iyeyo adzatsutsa ndi kudziyika pamwamba pa chilichonse chimene anthu amachitcha mulungu kapena amachipembedza. Iyeyo adzadzikhazika mʼNyumba ya Mulungu ndi kudzitcha Mulungu.
han, som sætter sig imod og ophøjer sig over alt. hvad der kaldes Gud eller Helligdom, så at han sætter sig i Guds Tempel og udgiver sig selv for at være Gud.
5 Kodi simukukumbukira kuti pamene ndinali nanu pamodzi ndinkakuwuzani zimenezi?
Komme I ikke i Hu, at jeg sagde eder dette, da jeg endnu var hos eder?
6 Ndipo tsopano mukudziwa chimene chikumuletsa kuonekera, koma adzawululika pa nthawi yake yoyenera.
Og nu vide I, hvad der holder ham tilbage, indtil han åbenbares i sin Tid.
7 Pakuti mphamvu yobisika yoyipitsitsa ikugwira ntchito ngakhale tsopano; koma amene akutchinga mphamvuyo adzapitiriza kutero mpaka pamene wotchingayo adzachotsedwe.
Thi Lovløshedens Hemmelighed virker allerede, kun at den, som nu holder tilbage, først må komme af Vejen
8 Ndipo kenaka woyipitsitsayo adzaonekera, amene Ambuye Yesu adzamugonjetsa ndi mpweya otuluka mʼkamwa mwake ndi kumuwononga ndi ulemerero wa kubwera kwake.
og da skal den lovløse åbenbares, hvem den Herre Jesus skal dræbe med sin Munds Ånde og tilintetgøre ved sin Tilkommelses Åbenbarelse,
9 Woyipitsitsayo adzabwera ndi mphamvu za Satana. Adzaonetsa mphamvu zake pochita zizindikiro ndi zodabwitsa zachinyengo.
han, hvis Komme sker ifølge Satans Kraft, med al Løgnens Magt og Tegn og Undere
10 Iye adzagwiritsa ntchito mtundu uliwonse wachinyengo kupusitsa amene akuwonongeka. Iwo akuwonongeka chifukwa akukana kukonda choonadi ndi kuti apulumutsidwe.
og med alt Uretfærdigheds Bedrag for dem, som fortabes, fordi de ikke toge imod Kærligheden til Sandheden, så de kunde blive frelste.
11 Chifukwa cha chimenechi, Mulungu akuwatumizira chinyengo chachikulu kuti akhulupirire bodza.
Og derfor sender Gud dem kraftig Vildfarelse, så at de tro Løgnen,
12 Choncho adzalangidwa onse amene sanakhulupirire choonadi, koma anakondwera mu zoyipa.
for at de skulle dømmes, alle de, som ikke troede Sandheden, men fandt Behag i Uretfærdigheden.
13 Koma tiyenera kuyamika Mulungu chifukwa cha inu abale okondedwa mwa Ambuye, pakuti Mulungu anakusankhani pachiyambi pomwe kuti mupulumuke chifukwa cha ntchito yoyeretsa ya Mzimu ndi chikhulupiriro chanu mʼchoonadi.
Men vi ere skyldige at takke Gud altid for eder, I af Herren elskede Brødre! fordi Gud har udvalgt eder fra Begyndelsen til Frelse ved Åndens Helligelse og Tro på Sandheden,
14 Iye anakuyitanirani zimenezi kudzera mwa uthenga wathu wabwino, kuti mulandire nawo ulemerero wa Ambuye athu Yesu Khristu.
hvortil han kaldte eder ved vort Evangelium, for at I skulde vinde vor Herres Jesu Kristi Herlighed.
15 Kotero tsono, abale, imani mwamphamvu ndi kugwiritsa ziphunzitso zimene tinakupatsani kudzera mʼmawu apakamwa kapena kudzera mʼkalata.
Så står da fast, Brødre! og holder fast ved de Overleveringer, hvori I bleve oplærte, være sig ved vor Tale eller vort Brev.
16 Ambuye athu Yesu Khristu mwini ndi Mulungu Atate wathu, amene anatikonda ife ndipo mwachisomo chake anatipatsa kulimba mtima kwamuyaya ndi chiyembekezo chabwino, (aiōnios )
Men han selv, vor Herre Jesus Kristus og Gud vor Fader, som har elsket og givet os en evig Trøst og et godt Håb i Nåde, (aiōnios )
17 akulimbikitseni ndi kukupatsani mphamvu yogwirira ntchito ndi kuyankhula zabwino zilizonse.
han trøste eders Hjerter og styrke eder i al god Gerning og Tale!