< 2 Samueli 1 >

1 Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
Pripetilo se je torej, po Savlovi smrti, ko se je David vrnil iz pokola Amalečanov in je David dva dni prebival v Ciklágu
2 Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
in tretji dan se je zgodilo celo, da je, glej, mož prišel iz tabora od Savla s svojimi pretrganimi oblačili in zemlja je bila na njegovi glavi. In bilo je tako, ko je prišel k Davidu, da je padel k tlom in se globoko priklonil.
3 Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
David mu je rekel: »Od kod prihajaš?« Rekel mu je: »Pobegnil sem iz tabora Izraelcev.«
4 Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
David mu je rekel: »Kako je šla zadeva? Prosim te, povej mi.« Odgovoril je: »Da je ljudstvo pobegnilo iz bitke in tudi številni izmed ljudstva so padli in so mrtvi in tudi Savel in njegov sin Jonatan sta mrtva.«
5 Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
David je rekel mladeniču, ki mu je povedal: »Kako veš, da sta Savel in njegov sin Jonatan mrtva?«
6 Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
Mladenič, ki mu je povedal, je rekel: »Kakor sem se naključno znašel na gori Gilbói, glej, Savel se je naslanjal na svojo sulico in glej, bojni vozovi in konjeniki so tesno sledili za njim.«
7 Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
Ko je pogledal za seboj, me je videl in me poklical k sebi. Odgovoril sem: »Tukaj sem.«
8 Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
Rekel mi je: »Kdo si?« Odgovoril sem mu: »Amálečan sem.«
9 “Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
Ponovno mi je rekel: »Stoj, prosim te, nad menoj in me ubij, kajti tesnoba je prišla nadme, ker je moje življenje še celo v meni.«
10 “Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
Tako sem stopil k njemu in ga usmrtil, ker sem bil prepričan, da potem, ko je padel, ne bi mogel živeti in vzel sem krono, ki je bila na njegovi glavi ter zapestnico, ki je bila na njegovem laktu ter ju prinesel sèm k svojemu gospodu.
11 Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
Potem je David prijel svoja oblačila in jih raztrgal in prav tako vsi možje, ki so bili z njim
12 Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
in žalovali so, jokali in se do večera postili za Savlom in za njegovim sinom Jonatanom in za Gospodovim ljudstvom in za Izraelovo hišo, ker so padli pod mečem.
13 Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
David je rekel mladeniču, ki mu je povedal: »Od kod si?« Odgovoril je: »Jaz sem sin tujca, Amálečana.«
14 Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
David mu je rekel: »Kako se nisi bal iztegniti svoje roke, da uničiš Gospodovega maziljenca?«
15 Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
David je poklical enega izmed mladeničev ter rekel: »Približaj se in padi nanj.« In ta ga je udaril, da je umrl.
16 Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
David mu je rekel: »Tvoja kri bodi na tvoji glavi, kajti tvoja usta so pričala zoper tebe, rekoč: ›Umoril sem Gospodovega maziljenca.‹«
17 Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
David je s tem žalovanjem žaloval nad Savlom in nad njegovim sinom Jonatanom.
18 Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
(Prav tako je zaukazal, naj Judove otroke učijo uporabo loka. Glej, to je napisano v Jasherjevi knjigi.)
19 “Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
»Izraelova lepota je umorjena na tvojih visokih krajih. Kako so padli mogočni!
20 “Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
Ne povejte tega v Gatu, ne razglašajte tega na Aškelónskih ulicah, da se ne bi filistejske hčere veselile, da ne bi hčere neobrezancev slavile.
21 “Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
Ve gore Gilbóe, naj tam ne bo nobene rose niti naj tam ne bo dežja nad vami niti nobenih polj za darovanja, kajti ščit mogočnega je podlo odvržen, Savlov ščit, kakor če ne bi bil maziljen z oljem.
22 “Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
Od krvi pobitih, od maščobe mogočnih, se Jonatanov lok ni obrnil nazaj in Savlov meč se ni vrnil prazen.
23 “Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
Savel in Jonatan sta bila očarljiva in prijetna v svojih življenjih in v svoji smrti nista bila ločena. Hitrejša sta bila kakor orli, močnejša sta bila kakor levi.
24 “Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
Ve hčere izraelske, jokajte nad Savlom, ki vas je oblekel v škrlat, z drugimi nasladami, ki je na vaše obleke nadel ornamente iz zlata.
25 “Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
Kako so mogočni padli v sredi bitke! Oh Jonatan, umorjen si bil na svojih visokih krajih.
26 Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
Žalosten sem zaradi tebe, moj brat Jonatan. Zelo prijeten si mi bil. Tvoja ljubezen do mene je bila čudovita, presegajoča ljubezen žensk.
27 “Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”
Kako so mogočni padli in so uničena bojna orožja.«

< 2 Samueli 1 >