< 2 Samueli 1 >
1 Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
I stało się po śmierci Saulowej, gdy się Dawid wrócił od porażki Amalekitów, że zamieszkał Dawid w Sycelegu przez dwa dni.
2 Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
Tedy dnia trzeciego przybieżał mąż z obozu Saulowego, a szaty jego rozdarte były, i proch na głowie jego; który przyszedłszy do Dawida, upadł na ziemię, i pokłonił się.
3 Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
I rzekł do niego Dawid: Skąd idziesz? I odpowiedział mu: Z obozum Izraelskiego uszedł.
4 Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
Rzekł mu znowu Dawid: Cóż się stało? proszę powiedz mi. I odpowiedział: To, że uciekł lud z bitwy, a do tego wiele poległo z ludu i pomarło, także i Saul, i Jonatan, syn jego, polegli.
5 Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
Zatem rzekł Dawid do młodzieńca, który mu to powiedział: Jakoż wiesz, iż umarł Saul i Jonatan, syn jego?
6 Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
Odpowiedział mu młodzieniec, który mu to oznajmił: Przyszedłem z trafunku na górę Gilboe, a oto, Saul tkwiał na włóczni swojej, a wozy i jezdni doganiali go.
7 Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
Tedy obejrzawszy się, obaczył mię, i zawołał na mię, i rzekłem: Owom ja.
8 Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
I rzekł mi: Coś ty zacz? A jam mu odpowiedział: Jestem Amalekita.
9 “Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
I rzekł mi: Stań, proszę, nademną, a zabij mię: bo mię zdjęły ciężkości, gdyż jeszcze wszystka dusza moja we mnie jest.
10 “Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
Przetoż stanąwszy nad nim, zabiłem go: bom wiedzieł, że nie będzie żyw po upadku swoim, i wziąłem koronę, która była na głowie jego, i zawieszenie, które było na ramieniu jego, a przyniosłem je tu do pana mego.
11 Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
Tedy Dawid pochwyciwszy szaty swoje, rozdarł je, także i wszyscy mężowie, którzy z nim byli.
12 Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
A żałując płakali, i pościli aż do wieczora dla Saula, i dla Jonatana, syna jego, i dla ludu Pańskiego, i dla domu Izraelskiego, że polegli od miecza.
13 Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
I rzekł Dawid do młodzieńca, który mu to oznajmił: Skądeś ty? I odpowiedział: Jestem synem męża przychodnia Amalekity.
14 Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
Zatem rzekł do niego Dawid: Jakożeś się nie bał ściągnąć ręki twej, abyś zabił pomazańca Pańskiego?
15 Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
Zawołał tedy Dawid jednego z sług, i rzekł: Przystąp, a zabij go, a on go uderzył, że umarł.
16 Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
I rzekł do niego Dawid: Krew twoja na głowę tweję: bo usta twoje świadczyły przeciw tobie, mówiąc: Jam zabił pomazańca Pańskiego.
17 Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
Lamentował tedy Dawid lamentem takowym nad Saulem, i nad Jonatanem, synem jego;
18 Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
(Rozkazawszy jednak, aby uczono synów Judzkich z łuku strzelać, jako napisano w księgach Jasar.)
19 “Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
O ozdobo Izraelska! na górach twoich zranionyś jest; jakoż polegli mocarze twoi!
20 “Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
Nie powiadajcież w Get, a nie rozgłaszajcie po ulicach w Aszkalonie, aby się snać nie weseliły córki Filistyńskie, by się snać nie radowały córki nieobrzezańców.
21 “Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
O góry Gielboe! ani rosa, ani deszcz niech nie upada na was, i niech tam nie będą pola urodzajne; albowiem tam porzucona jest tarcz mocarzów, tarcz Saulowa, jakoby nie był pomazany olejem.
22 “Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
Od krwi zabitych, i od sadła mocarzów strzała łuku Jonatanowego nie wracała się na wstecz, a miecz Saulowy nie wracał się próżno.
23 “Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
Saul i Jonatan miłośni i przyjemni za żywota swego, i w śmierci swojej nie są rozłączeni, nad orły lekciejsi, nad lwy mocniejsi byli.
24 “Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
Córki Izraelskie płaczcie nad Saulem, który was przyodziewał szarłatem rozkosznym, a który was ubierał w klejnoty złote na szaty wasze.
25 “Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
Jakoż polegli mocarze pośród bitwy! Jonatan na górach twoich zabity jest.
26 Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
Bardzo mi cię żal, bracie mój Jonatanie, byłeś mi bardzo wdzięcznym; większa u mnie była miłość twoja, niż miłość niewieścia.
27 “Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”
Jakoż polegli mocarze, a poginęła broń wojenna!