< 2 Samueli 1 >
1 Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
Da Saul var død, og David var vendt tilbake efterat han hadde slått amalekittene, blev David ennu to dager i Siklag.
2 Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
Da hendte det den tredje dag at det kom en mann fra Sauls leir med sønderrevne klær og jord på sitt hode; og da han kom til David, kastet han sig ned på jorden for ham.
3 Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
David spurte ham: Hvor kommer du fra? Han svarte: Jeg har flyktet fra Israels leir.
4 Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
Da sa David til ham: Hvorledes er det gått? Fortell mig det! Han svarte: Folket flyktet fra striden; mange av folket falt og døde, og Saul og hans sønn Jonatan er også død.
5 Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
Da sa David til den gutt som kom med denne tidende til ham: Hvorledes vet du at Saul og hans sønn Jonatan er død?
6 Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
Gutten, han som var kommet med tidenden til ham, svarte: Ved en hendelse kom jeg op på Gilboafjellet, og der fikk jeg se Saul som stod og støttet sig på sitt spyd, mens vognene og hestfolket satte hårdt inn på ham.
7 Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
Han vendte sig om, og da han så mig, ropte han på mig. Jeg svarte: Her er jeg.
8 Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
Så spurte han: Hvem er du? Jeg svarte: Jeg er en amalekitt.
9 “Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
Da sa han til mig: Kom hit til mig og drep mig! For krampen har grepet mig, men jeg har ennu min fulle livskraft.
10 “Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
Så gikk jeg bort til ham og drepte ham, for jeg visste at han ikke vilde overleve sitt fall; og jeg tok kongesmykket som han hadde på hodet, og ringen han bar på armen, og tok dem med hit til min herre.
11 Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
Da tok David og sønderrev sine klær, og det samme gjorde alle de menn som var hos ham.
12 Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
Og de klaget og gråt og fastet helt til aftenen over Saul og hans sønn Jonatan og over Herrens folk og over Israels hus, fordi de var falt for sverdet.
13 Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
Så spurte David gutten som var kommet med tidenden til ham: Hvor er du fra? Han svarte: Jeg er sønn av en amalekitt som er flyttet inn her.
14 Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
Da sa David til ham: Hvorledes kunde du driste dig til å utrekke din hånd og ta livet av Herrens salvede?
15 Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
Og David kalte på en av sine menn og sa: Kom hit og hugg ham ned! Og han slo ham ihjel.
16 Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
Men David sa til ham: Ditt blod komme over ditt hode; for din egen munn vidnet mot dig da du sa: Jeg har drept Herrens salvede.
17 Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
Og David kvad denne klagesang over Saul og hans sønn Jonatan,
18 Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
og han bød at Judas barn skulde lære den; "buen" heter den, og den er opskrevet i Den rettskafnes bok:
19 “Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
Din pryd, Israel, ligger ihjelslått på dine hauger; o, at heltene skulde falle!
20 “Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
Forkynn det ikke i Gat, meld det ikke på gatene i Askalon, at ikke filistrenes døtre skal glede sig, de uomskårnes døtre juble!
21 “Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
I Gilboa-fjell! Ikke falle det dugg eller regn på eder, ei heller være der marker som bærer offergaver! For der blev heltes skjold plettet med blod, Sauls skjold, ei salvet med olje.
22 “Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
Fra falnes blod, fra heltes kjøtt vek Jonatans bue aldri tilbake, aldri kom Sauls sverd umettet hjem.
23 “Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
Saul og Jonatan, elskelige og milde i livet, blev heller ikke skilt i døden; hurtigere var de enn ørner, sterkere enn løver.
24 “Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
I Israels døtre! Gråt over Saul som klædde eder yndig i purpur, som satte smykker av gull på eders klædebon!
25 “Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
O, at heltene skulde falle i striden! Jonatan ligger ihjelslått på dine hauger!
26 Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
Hjertelig bedrøvet er jeg over dig, min bror Jonatan! Du var mig inderlig kjær; din kjærlighet var mig dyrebarere enn kvinners kjærlighet.
27 “Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”
O, at heltene skulde falle, og krigens redskaper omkomme!