< 2 Samueli 1 >
1 Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
Or, il arriva, après que Saül fut mort, que David revint de la défaite d’Amalec, et qu’il demeura à Siceleg pendant deux jours.
2 Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
Mais au troisième jour, il parut un homme, venant du camp de Saül, le vêtement déchiré et la tête couverte de poussière; et dès qu’il arriva auprès de David, il tomba sur sa face, et se prosterna.
3 Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
Et David lui demanda: D’où viens-tu? Celui-ci lui répondit: Je me suis échappé du camp d’Israël.
4 Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
David lui demanda encore: Qu’est-ce qui a été fait? Apprends-le moi. Il répondit: Le peuple s’est enfui de la bataille, et beaucoup d’entre le peuple, ayant succombé, sont morts; et Saül même et Jonathas son fils ont péri.
5 Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
Et David dit au jeune homme qui lui apportait la nouvelle: D’où sais-tu que Saül est mort, et Jonathas son fils?
6 Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
Et le jeune homme qui lui apportait la nouvelle lui répondit: Je suis venu par hasard sur la montagne de Gelboé, et Saül était appuyé sur sa lance; or, les chariots et les cavaliers s’avançaient vers lui,
7 Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
Et s’étant retourné, et me voyant, il m’a appelé. Et quand je lui eus répondu: Me voici,
8 Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
Il me demanda: Qui es-tu? Et je lui répondis: Je suis Amalécite.
9 “Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
Alors il me dit: Jette-toi sur moi, et tue-moi, parce que je suis en proie aux angoisses, et que toute mon âme est encore en moi.
10 “Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
Me jetant donc sur lui, je le tuai; car je savais qu’il ne pouvait pas vivre après son désastre; alors je pris le diadème qui était sur sa tête, et le bracelet de son bras, et je les apportai ici à vous, mon seigneur.
11 Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
Mais David prenant ses vêtements, les déchira; ce que firent aussi tous les hommes qui étaient avec lui.
12 Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
Et ils furent dans le deuil, et ils pleurèrent et ils jeûnèrent jusqu’au soir, au sujet de Saül, de Jonathas, son fils, du peuple du Seigneur et de la maison d’Israël, parce qu’ils avaient succombé au glaive.
13 Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
Et David dit au jeune homme qui lui avait apporté la nouvelle: D’où es-tu? Il répondit: Je suis fils d’un étranger, d’un Amalécite.
14 Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
Et David lui dit: Pourquoi n’as-tu pas craint de lever ta main, pour tuer le christ du Seigneur?
15 Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
Et David appelant un de ses serviteurs, dit: Approche-toi, jette-toi sur lui. Le serviteur le frappa, et il mourut,
16 Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
Et David ajouta: Ton sang sur ta tête! car ta bouche a parlé contre toi, disant: C’est moi qui ai tué le christ du Seigneur.
17 Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
Alors David fit entendre cette complainte sur Saül et sur Jonathas, son fils
18 Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
(Et il ordonna qu’on enseignât l’arc aux enfants de Juda, comme il est écrit dans le Livre des Justes), et il dit: Considère, ô Israël, ceux qui sont morts sur tes hauts lieux, couverts de blessures.
19 “Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
Les illustres, ô Israël, ont été tués sur tes montagnes: comment des forts sont-ils tombés?
20 “Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
Ne l’annoncez pas dans Geth, ne l’annoncez pas dans les carrefours d’Ascalon, de peur que les filles des Philistins ne se livrent à la joie, et que les filles des incirconcis ne bondissent d’allégresse.
21 “Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
Montagnes de Gelboé, que ni pluie, ni rosée ne viennent sur vous: qu’il n’y ait point de champs de prémices, parce que là a été jeté un bouclier de forts, le bouclier de Saül, comme s’il n’avait pas été oint avec l’huile.
22 “Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
La flèche de Jonathas n’est jamais retournée en arrière, sans avoir du sang de ceux qui ont été tués, et de la graisse des forts, et le glaive de Saül n’est pas revenu en vain.
23 “Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
Saül et Jonathas, aimables et beaux dans leur vie, même à leur mort, n’ont pas été séparés; plus rapides que des aigles, plus forts que des lions.
24 “Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
Filles d’Israël, pleurez sur Saül, qui vous revêtait d’écarlate au milieu des délices, et vous fournissait de l’or pour votre parure.
25 “Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
Comment des forts sont-ils tombés dans la bataille? Jonathas a été tué sur tes hauteurs.
26 Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
Je pleure sur toi, mon frère, Jonathas, de la plus grande beauté, aimable au-dessus de l’amour des femmes. Comme une mère aime son fils unique, ainsi moi je te chérissais.
27 “Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”
Comment des forts sont-ils tombés, et des armes guerrières ont-elles péri?