< 2 Samueli 1 >
1 Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
Après que Saül fut mort, David, étant revenu de la défaite des Amalécites, demeura à Tsiklag deux jours;
2 Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
Et le troisième jour on vit paraître un homme qui revenait du camp, d'auprès de Saül, ayant ses vêtements déchirés et de la terre sur sa tête; et, étant venu vers David, il se jeta contre terre et se prosterna.
3 Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
Et David lui dit: D'où viens-tu? Et il lui répondit: Je me suis échappé du camp d'Israël.
4 Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
David lui dit: Qu'est-il arrivé? Raconte-le-moi donc. Il répondit: Le peuple s'est enfui de la bataille, et même un grand nombre sont tombés morts; Saül aussi et Jonathan, son fils, sont morts.
5 Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
Et David dit au jeune homme qui lui donnait ces nouvelles: Comment sais-tu que Saül et Jonathan, son fils, sont morts?
6 Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
Et le jeune homme qui lui donnait ces nouvelles, répondit: Je me trouvais par hasard sur la montagne de Guilboa, et voici, Saül s'appuyait sur sa lance; et voici, les chars et les cavaliers etaient près de l'atteindre;
7 Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
Et, regardant en arrière, il me vit, et m'appela; et je répondis: Me voici.
8 Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
Et il me dit: Qui es-tu? Et je lui répondis: Je suis Amalécite.
9 “Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
Alors il me dit: Avance-toi vers moi, et me fais mourir; car je suis dans une grande angoisse, ma vie est encore toute en moi.
10 “Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
Je me suis donc approché de lui et je l'ai fait mourir; car je savais qu'il ne vivrait pas après s'être ainsi jeté sur son épée; puis j'ai pris la couronne qui était sur sa tête, et le bracelet qui était à son bras, et je les ai apportés ici à mon seigneur.
11 Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
Alors David prit ses vêtements, et les déchira; et tous les hommes qui étaient avec lui firent de même.
12 Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
Et ils menèrent deuil, et pleurèrent, et jeûnèrent jusqu'au soir à cause de Saül, et de Jonathan, son fils, et du peuple de l'Éternel, et de la maison d'Israël; parce qu'ils étaient tombés par l'épée.
13 Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
Mais David dit au jeune homme qui lui avait donné ces nouvelles: D'où es-tu? Et il répondit: Je suis fils d'un étranger amalécite.
14 Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
Et David lui dit: Comment n'as-tu pas craint d'avancer ta main pour tuer l'oint de l'Éternel?
15 Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
Alors David appela l'un de ses gens, et lui dit: Approche-toi, jette-toi sur lui! Il le frappa, et il mourut.
16 Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
Et David lui dit: Ton sang soit sur ta tête! car ta bouche a témoigné contre toi, en disant: J'ai fait mourir l'oint de l'Éternel.
17 Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
Alors David fit sur Saül et sur Jonathan, son fils, cette complainte,
18 Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
Qu'il ordonna d'enseigner aux enfants de Juda, la complainte de l'Arc; voici, elle est écrite au livre du Juste:
19 “Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
Ta gloire, ô Israël, a péri sur tes collines! Comment sont tombés les hommes vaillants?
20 “Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
N'allez point le dire dans Gath, ne l'annoncez point dans les places d'Askélon; de peur que les filles des Philistins ne se réjouissent, de peur que les filles des incirconcis ne triomphent.
21 “Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
Montagnes de Guilboa, que la rosée et la pluie ne tombent plus sur vous, qu'il n'y ait plus de champs dont on offre les prémices; car c'est là qu'a été jeté le bouclier des hommes forts, le bouclier de Saül, comme s'il n'eût pas été oint d'huile.
22 “Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
L'arc de Jonathan ne revenait jamais sans être teint du sang des blessés et de la graisse des vaillants; et l'épée de Saül ne retournait pas sans effet.
23 “Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
Saül et Jonathan, aimables et agréables pendant leur vie, n'ont point été séparés dans leur mort; ils étaient plus légers que les aigles, ils étaient plus forts que les lions.
24 “Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
Filles d'Israël, pleurez sur Saül, qui vous revêtait d'écarlate, dans les délices; qui vous faisait porter des ornements d'or sur vos habits!
25 “Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
Comment sont tombés les hommes forts au milieu de la bataille, et comment Jonathan a-t-il été tué sur tes collines?
26 Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
Jonathan, mon frère, je suis dans la douleur à cause de toi. Tu faisais tout mon plaisir; l'amour que j'avais pour toi était plus grand que celui des femmes.
27 “Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”
Comment sont tombés les vaillants? Comment se sont perdues les armes de la guerre?