< 2 Samueli 1 >
1 Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
Après la mort de Saül, David revenait de la tuerie des Amalécites, et il était resté deux jours à Tsiklag.
2 Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
Le troisième jour, voici qu'un homme sortit du camp de la part de Saül, les vêtements déchirés et de la terre sur la tête. Lorsqu'il arriva à David, il se jeta à terre et lui témoigna du respect.
3 Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
David lui dit: « D'où viens-tu? » Il lui dit: « Je me suis échappé du camp d'Israël. »
4 Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
David lui dit: « Comment cela s'est-il passé? Dis-le-moi. » Il répondit: « Le peuple a fui la bataille, et beaucoup de gens sont tombés et sont morts. Saül et son fils Jonathan sont morts eux aussi. »
5 Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
David dit au jeune homme qui lui avait raconté: « Comment sais-tu que Saül et Jonathan, son fils, sont morts? »
6 Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
Le jeune homme qui le raconta dit: « Comme je me trouvais par hasard sur la montagne de Gilboa, voici que Saül s'appuyait sur sa lance; et voici que les chars et les cavaliers suivaient de près derrière lui.
7 Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
Quand il regarda derrière lui, il me vit et m'appela. Je répondis: Me voici!
8 Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
Il me dit: « Qui es-tu? Je lui répondis: Je suis un Amalécite.
9 “Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
Il me dit: « Mets-toi à côté de moi, je t'en prie, et tue-moi, car l'angoisse s'est emparée de moi, parce que ma vie est encore en moi.
10 “Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
Je me suis donc tenu à côté de lui et je l'ai tué, car j'étais sûr qu'il ne pourrait pas vivre après sa chute. J'ai pris la couronne qui était sur sa tête et le bracelet qui était à son bras, et je les ai apportés ici à mon seigneur. »
11 Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
Alors David saisit ses vêtements et les déchira, et tous les hommes qui étaient avec lui firent de même.
12 Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
Ils se lamentèrent, pleurèrent et jeûnèrent jusqu'au soir sur Saül et sur Jonathan, son fils, sur le peuple de l'Éternel et sur la maison d'Israël, parce qu'ils étaient tombés par l'épée.
13 Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
David dit au jeune homme qui lui a parlé: « D'où viens-tu? » Il répondit: « Je suis le fils d'un étranger, un Amalécite. »
14 Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
David lui dit: « Pourquoi n'as-tu pas eu peur d'étendre ta main pour faire périr l'oint de Yahvé? ».
15 Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
David appela l'un des jeunes hommes et dit: « Approche, et coupe-le! ». Il le frappa de telle sorte qu'il mourut.
16 Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
David lui dit: « Que ton sang retombe sur ta tête, car ta bouche a rendu témoignage contre toi, en disant: J'ai tué l'oint de l'Éternel. »
17 Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
David se lamenta ainsi sur Saül et sur Jonathan, son fils
18 Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
(et il leur ordonna d'enseigner aux fils de Juda le chant de l'arc; voici, cela est écrit dans le livre de Jashar):
19 “Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
« Ta gloire, Israël, a été tuée sur tes hauts lieux! Comme les puissants sont tombés!
20 “Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
Ne le dis pas à Gath. Ne le publiez pas dans les rues d'Ashkelon, de peur que les filles des Philistins ne se réjouissent, de peur que les filles des incirconcis ne triomphent.
21 “Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
Vous les montagnes de Gilboa, qu'il n'y ait ni rosée ni pluie sur vous, et pas de champs d'offrandes; car c'est là que le bouclier des puissants a été souillé et jeté, le bouclier de Saul n'a pas été oint d'huile.
22 “Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
Du sang des victimes, de la graisse des puissants, L'arc de Jonathan ne s'est pas retourné. L'épée de Saul n'est pas revenue vide.
23 “Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
Saül et Jonathan étaient charmants et agréables dans leur vie. Dans leur mort, ils n'ont pas été divisés. Ils étaient plus rapides que les aigles. Ils étaient plus forts que des lions.
24 “Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
Filles d'Israël, pleurez sur Saül, qui t'a délicatement vêtu d'écarlate, qui ont mis des ornements d'or sur vos vêtements.
25 “Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
Comme les puissants sont tombés au milieu de la bataille! Jonathan a été tué sur vos hauts lieux.
26 Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
Je suis dans l'angoisse pour toi, mon frère Jonathan. Vous avez été très agréable avec moi. Ton amour pour moi était merveilleux, surpassant l'amour des femmes.
27 “Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”
Comme les puissants sont tombés, et les armes de guerre ont péri! »