< 2 Samueli 1 >

1 Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
Saul a dueknah hnukah David te Amalek a tloek lamkah ha mael. Te vaengah David Te Ziklag ah hnin nit om.
2 Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
Hnin thum a om phoeiah Saul taengkah hlang Te caem lamkah tarha ha pawk. A himbai te a pawnsoem la a lu dongkah laipi neh David taengla ha pawk vaengah lai la yalh tih a bawk.
3 Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
Anih te David loh, “Me lamkah lae na pawk,” a ti nah. Te dongah amah te, “Israel caem lamloh ka yong,” a ti nah.
4 Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
Te dongah anih te David loh, “Olka aka om te kai taengah thui laeh,” a ti nah hatah pilnam Te caemtloek lamkah rhaelrham tih pilnam muep a duek Te khaw, Saul a duek Te khaw, a capa Jonathan a duek khaw a thui pah.
5 Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
Te dongah amah taengla aka puen cadong te David loh, “Saul neh a capa Jonathan a duek te me tlam lae na ming?” a ti nah.
6 Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
Amah taengla aka puen cadong loh, “Gilboa tlang la ka thoeng rhoe ka thoeng. Te vaengah Saul Te amah kah caai dongah hangdang tih leng neh marhang caem boei rhoek loh anih Te tarha a cuuk thiluh.
7 Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
Te vaengah a hnukla ha mael tih kai m'hmuh hatah ng'khue tih, 'Kai ni he ue,’ ka ti nah.
8 Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
Te phoeiah kai te, “Nang ulae,” a ti. Te dongah anih te ka doo tih, “Kai Amalek ni,” ka ti nah.
9 “Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
Te vaengah, “Kai taengah pai lamtah kai he n'duek sak laeh, duekrhui loh kai n'tuuk tih ka khuiah ka hinglu khaw khak om pueng he,” a ti.
10 “Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
Tedae a cungku coeng he tah hing mahpawh tila ka ming dongah anih te ka pai tih ka duek sak. Te phoeiah a lu dongkah rhuisam neh a ban dongkah cak te ka loh tih ka boei taengla pahoi kang khuen,” a ti nah.
11 Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
Te dongah David loh a himbai te a paco tih a phen hatah a taengkah hlang rhoek long khaw boeih a rhoi uh.
12 Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
cunghang neh a cungku uh coeng dongah Israel imkhui ham khaw, BOEIPA kah pilnam ham khaw, Saul ham neh a capa Jonathan ham khaw a rhaengsae uh. Rhap uh tih kholaeh duela a yaeh uh.
13 Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
Te phoeiah amah taengla aka puen camoe te David loh, “Nang me lamkah lae,” a ti nah hatah, “Kai tah Amalek yinlai, hlang capa ni,” a ti nah.
14 Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
Tedae anih te David loh, “BOEIPA kah a koelh te thup hamla kut na hlah te balae tih na rhih pawh?” a ti nah.
15 Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
Te phoeiah David loh cadong pakhat te a khue tih, “Thoeih lamtah, a cuuk thil,” a ti nah. Te dongah a ngawn tih duek.
16 Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
Anih te David loh, “'BOEIPA kah a koelh te kai loh ka duek sak,’ na ti tih na ka loh namah taengah a phoe coeng dongah na thii khaw namah thii vanbangla namah lu soah tla saeh,” a ti nah.
17 Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
Saul neh a capa Jonathan te David loh rhahlung neh a rhaengsae.
18 Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
Te dongah Jashar cabu dongkah a daek liva laa he Judah ca rhoek a cang ham a thui.
19 “Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
Israel kirhang hlangrhalh nang loh, hmuensang ah balae tih a rhok la a cung uh.
20 “Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
Gath ah na puen pawh, Ashkelon tollong ah khaw na phong pawh. Philisti nu loh n'kokhah ve pumdul nu rhoek sundaep uh ve.
21 “Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
Gilboa tlang ah buemtui tla boel saeh, nang soah khotlan khaw bo boel saeh. Saul kah photling, hlangrhalh photling te na tuei dongah khocang hmuen loh situi nen khaw koelh boel saeh.
22 “Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
Hlangrhalh tha neh salaem thii he, Jonathan kah liva loh a hnuk la balkhong tak pawt tih Saul kah cunghang khaw kuttling la a mael moenih.
23 “Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
Saul neh Jonathan lung uh rhoi. A hing khuiah naepnoi rhoi tih a duek vaengah tuiphih pawh. Aatha lakah yanghoep rhoi tih, sathueng lakah a na rhoi.
24 “Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
Nangmih a lingdik neh omthennah aka bawn tih, na pueinak dongah sui cangen neh aka cam Israel nu rhoek loh, Saul te rhah uh lah.
25 “Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
Na hmuensang kah Jonathan te, hlangrhalh rhoek loh caemrhal laklo ah a rhok la a cungku sakuh.
26 Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
Ka manuca Jonathan nang ham kai n'daengdaeh. Kai taengah na hlahmae sut tih, yuu kah lungnah lakah khaw kai ham tah, nang kah lungnah ni khobaerhambae coeng.
27 “Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”
Balae tih hlangrhalh rhoek a cungku uh vaengah, caemtloek kah hnopai khaw a paltham.

< 2 Samueli 1 >