< 2 Samueli 9 >

1 Davide anafunsa kuti, “Kodi alipo amene watsala mʼbanja la Sauli kuti ndimuchitire chifundo chifukwa cha Yonatani?”
David dit: « Y a-t-il encore quelqu'un qui reste de la maison de Saül, pour que je lui fasse du bien à cause de Jonathan? »
2 Tsono panali mtumiki wina wa banja la Sauli wotchedwa Ziba. Iwo anamuyitana kuti aonekere pamaso pa Davide, ndipo mfumu inamufunsa kuti, “Kodi ndiwe Ziba?” Iyeyo anayankha kuti, “Ine mtumiki wanu.”
Il y avait dans la maison de Saül un serviteur dont le nom était Tsiba, et on l'appela auprès de David; le roi lui dit: « Es-tu Tsiba? ». Il a dit: « Je suis ton serviteur. »
3 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi palibe amene watsala wa banja la Sauli amene ndingamuchitire chifundo cha Mulungu?” Ziba anayankha mfumu kuti, “Alipo mwana wa Yonatani, koma ndi wolumala mapazi ake onse.”
Le roi dit: « N'y a-t-il pas encore quelqu'un de la maison de Saül, pour que je puisse lui montrer la bonté de Dieu? » Ziba dit au roi: « Jonathan a encore un fils, qui boite des pieds. »
4 Mfumu inafunsa kuti, “Ali kuti?” Ziba anayankha kuti, “Iye ali ku nyumba ya Makiri mwana wa Amieli ku Lodebara.”
Le roi lui dit: « Où est-il? » Ziba dit au roi: « Voici, il est dans la maison de Makir, fils d'Ammiel, à Lo Debar. »
5 Kotero mfumu inamubweretsa kuchokera ku Lodebara, ku nyumba ya Makiri mwana wa Amieli.
Le roi David l'envoya chercher dans la maison de Makir, fils d'Ammiel, à Lo Debar.
6 Mefiboseti mwana wa Yonatani, mwana wa Sauli atafika kwa Davide, anawerama pansi kupereka ulemu kwa iye. Davide anati, “Mefiboseti!” Iye anayankha kuti, “Ine mtumiki wanu.”
Mephiboscheth, fils de Jonathan, fils de Saül, vint auprès de David, tomba sur sa face et lui témoigna du respect. David dit: « Mephibosheth? » Il répondit: « Voici ton serviteur! »
7 Davide anati kwa iye, “Usachite mantha, pakuti ndidzakuchitira ndithu chifundo chifukwa cha abambo ako Yonatani. Ine ndidzakubwezera iwe dziko lonse limene linali la agogo ako Sauli, ndipo iweyo udzadya ndi ine nthawi zonse.”
David lui dit: « N'aie pas peur, car je te ferai du bien à cause de Jonathan, ton père, et je te rendrai tout le pays de Saül, ton père. Tu mangeras continuellement du pain à ma table. »
8 Mefiboseti anawerama pansi ndipo anati, “Mtumiki wanu ndine yani kuti musamale galu wakufa ngati ine?”
Il se prosterna, et dit: « Quel est ton serviteur, pour que tu regardes un chien mort comme moi? »
9 Kenaka Davide anayitanitsa Ziba, mtumiki wa Sauli, ndipo anati, “Ine ndapereka kwa chidzukulu cha mbuye wako chilichonse chimene chinali cha Sauli ndi banja lake.
Le roi appela Tsiba, serviteur de Saül, et lui dit: « Je donne au fils de ton maître tout ce qui appartenait à Saül et à toute sa maison.
10 Iwe ndi ana ndi antchito anu muzimulimira mʼdziko lake ndipo muzibweretsa zokololazo kuti chidzukulu cha mbuye wako chikhale ndi chakudya. Ndipo Mefiboseti, chidzukulu cha mbuye wako adzadya ndi ine nthawi zonse.” (Tsono Ziba anali ndi ana aamuna khumi ndi asanu ndi antchito makumi awiri).
Cultivez pour lui le pays, vous, vos fils et vos serviteurs. Fais la moisson, afin que le fils de ton maître ait du pain à manger; mais Mephibosheth, le fils de ton maître, mangera toujours du pain à ma table. » Or Tsiba avait quinze fils et vingt serviteurs.
11 Ndipo Ziba anati kwa mfumu, “Mtumiki wanu adzachita chilichonse chimene mbuye wanga mfumu mudzalamulire wantchito wanu kuti achite.” Kotero Mefiboseti ankadya ndi Davide monga mmodzi wa ana a mfumu.
Et Tsiba dit au roi: « Tout ce que mon seigneur le roi ordonne à son serviteur, ton serviteur le fera aussi. » Mephibosheth mangea donc à la table du roi comme l'un des fils du roi.
12 Mefiboseti anali ndi mwana wamngʼono wamwamuna wotchedwa Mika, ndipo onse a banja la Ziba anali antchito a Mefiboseti.
Mephibosheth avait un jeune fils, dont le nom était Mica. Tous ceux qui habitaient dans la maison de Tsiba étaient les serviteurs de Mephibosheth.
13 Ndipo Mefiboseti anakhala mu Yerusalemu chifukwa nthawi zonse amadya ndi mfumu. Iye anali wolumala mapazi ake onse.
Mephibosheth habitait donc à Jérusalem, car il mangeait continuellement à la table du roi. Il était boiteux des deux pieds.

< 2 Samueli 9 >