< 2 Samueli 9 >

1 Davide anafunsa kuti, “Kodi alipo amene watsala mʼbanja la Sauli kuti ndimuchitire chifundo chifukwa cha Yonatani?”
Ja David sanoi: olleeko joku vielä jäänyt Saulin huoneesta, tehdäkseni laupiuden Jonatanin tähden hänelle.
2 Tsono panali mtumiki wina wa banja la Sauli wotchedwa Ziba. Iwo anamuyitana kuti aonekere pamaso pa Davide, ndipo mfumu inamufunsa kuti, “Kodi ndiwe Ziba?” Iyeyo anayankha kuti, “Ine mtumiki wanu.”
Niin oli palvelia Saulin huoneesta Ziba nimeltä, sen kutsuivat Davidin tykö. Ja kuningas sanoi hänelle: oletkos Ziba? Hän sanoi: olen, sinun palvelias.
3 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi palibe amene watsala wa banja la Sauli amene ndingamuchitire chifundo cha Mulungu?” Ziba anayankha mfumu kuti, “Alipo mwana wa Yonatani, koma ndi wolumala mapazi ake onse.”
Kuningas sanoi: onko vielä joku mies Saulin huoneesta, että minä Jumalan laupiuden tekisin hänelle? Ziba sanoi kuninkaalle: vielä on siellä Jonatanin poika, rampa jaloista.
4 Mfumu inafunsa kuti, “Ali kuti?” Ziba anayankha kuti, “Iye ali ku nyumba ya Makiri mwana wa Amieli ku Lodebara.”
Kuningas sanoi hänelle: kussa hän on? Ziba sanoi kuninkaalle: katso, hän on Lodabarissa, Makirin, Ammielin pojan huoneessa.
5 Kotero mfumu inamubweretsa kuchokera ku Lodebara, ku nyumba ya Makiri mwana wa Amieli.
Niin kuningas David lähetti ja antoi tuoda hänen Lodabarista, Makirin Ammielin pojan huoneesta.
6 Mefiboseti mwana wa Yonatani, mwana wa Sauli atafika kwa Davide, anawerama pansi kupereka ulemu kwa iye. Davide anati, “Mefiboseti!” Iye anayankha kuti, “Ine mtumiki wanu.”
Kuin MephiBoset, Saulin pojan Jonatanin poika tuli Davidin tykö, lankesi hän kasvoillensa ja kumarsi. Ja David sanoi: MephiBoset! Hän vastasi: tässä olen, sinun palvelias.
7 Davide anati kwa iye, “Usachite mantha, pakuti ndidzakuchitira ndithu chifundo chifukwa cha abambo ako Yonatani. Ine ndidzakubwezera iwe dziko lonse limene linali la agogo ako Sauli, ndipo iweyo udzadya ndi ine nthawi zonse.”
David sanoi hänelle: älä pelkää; sillä minä totisesti teen laupiuden sinun kanssas Jonatanin sinun isäs tähden, ja minä annan sinulle kaikki sinun isäs Saulin pellot jälleen, ja sinä syöt jokapäivä leipää minun pöydältäni.
8 Mefiboseti anawerama pansi ndipo anati, “Mtumiki wanu ndine yani kuti musamale galu wakufa ngati ine?”
Hän kumarsi ja sanoi: kuka olen minä sinun palvelias, ettäs käänsit sinus kuolleen koiran puoleen, niinkuin minä olen?
9 Kenaka Davide anayitanitsa Ziba, mtumiki wa Sauli, ndipo anati, “Ine ndapereka kwa chidzukulu cha mbuye wako chilichonse chimene chinali cha Sauli ndi banja lake.
Niin kutsui kuningas Ziban, Saulin palvelian, ja sanoi hänelle: minä olen antanut sinun herras pojalle kaiken sen mikä Saulin oma on ollut ja koko hänen huoneensa oma.
10 Iwe ndi ana ndi antchito anu muzimulimira mʼdziko lake ndipo muzibweretsa zokololazo kuti chidzukulu cha mbuye wako chikhale ndi chakudya. Ndipo Mefiboseti, chidzukulu cha mbuye wako adzadya ndi ine nthawi zonse.” (Tsono Ziba anali ndi ana aamuna khumi ndi asanu ndi antchito makumi awiri).
Niin pitää sinun, ja sinun lapses, ja palvelias viljelemän hänen peltojansa ja korjaaman herras pojalle leiväksi ja ravinnoksi. Mutta MephiBoset sinun herras poika syö jokapäivä leipää minun pöydältäni. Ja Ziballa oli viisitoistakymmentä poikaa ja kaksikymmentä palveliaa.
11 Ndipo Ziba anati kwa mfumu, “Mtumiki wanu adzachita chilichonse chimene mbuye wanga mfumu mudzalamulire wantchito wanu kuti achite.” Kotero Mefiboseti ankadya ndi Davide monga mmodzi wa ana a mfumu.
Ja Ziba sanoi kuninkaalle: kaikki mitä minun herrani kuningas on palveliallensa käskenyt, tekee palvelias; ja MephiBoset syököön minun pöydältäni, niinkuin yksi kuninkaan lapsista.
12 Mefiboseti anali ndi mwana wamngʼono wamwamuna wotchedwa Mika, ndipo onse a banja la Ziba anali antchito a Mefiboseti.
Ja MephiBosetilla oli yksi vähä poika nimeltä Miika; mutta kaikki, jotka Ziban huoneesta olivat, olivat MephiBosetin palveliat.
13 Ndipo Mefiboseti anakhala mu Yerusalemu chifukwa nthawi zonse amadya ndi mfumu. Iye anali wolumala mapazi ake onse.
Ja MephiBoset asui Jerusalemissa; sillä hän söi jokapäivä kuninkaan pöydältä; ja hän ontui molemmista jaloistansa.

< 2 Samueli 9 >