< 2 Samueli 8 >

1 Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndi kuwapambana ndipo analanda Metegi Ama kuchoka mʼmanja mwa Afilistiwo.
Mançile qiyğa Davud Filiştinaaşile ğamxha, manbı cus vukkanəxüb vuk'lek vukkeeka. Manbışde xılençe Meteg-Ammahıb g'ooşena.
2 Davide anagonjetsanso Amowabu. Iye anawalamula kuti agone pansi mʼmizere itatu pa gulu lililonse ndipo anawayeza ndi chingwe. Pa gulu lililonse ankapha anthu amene anali pa mizere iwiri yoyamba, kusiyapo mzere wachitatu. Kotero Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Davide ndipo ankapereka msonkho.
Qiyğa Davud Moavbışiler ğamexhena. Mang'vee manbı ç'iyelqa g'alyapk'as alivku, baağıka ulyoopku, manbı xhebne desteeqa bit'al ha'a. Xhebne desteyna q'öble deste mang'vee gyabat'anbı. Sa destemee mang'vee g'ookana. Moavbı Davudus nukarar vooxhe, mang'us nalok'bı qele giviyğal.
3 Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
Tsovayna paççah eyxhena Rexovna dix Hadadezer, Fərat eyhene damayne hiqiy-alladın ciga meed cune xılyaqa alğahasva arayle. Maa'ar Davud mang'ule ğamexhena.
4 Davide analanda magaleta 1,000, anthu 7,000 okwera magaleta pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
Davudee Hadadezerna aazıriy yighıd vəş balkanılyna, g'ad aazırır hoyhar arına esker aqqaqqa. Mang'une balkanaaşina vəş Davudee cus avqu, axuyne daşk'ayk qı'iyne balkanaaşinıd g'elin damarbı gyatxas ilekka.
5 Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
Damask vooxhen Arambı Tsovayne paççahıs Hadadezerıs kumagıs abımee, Davudee manbışda g'ayeq'vəd aazır insan gek'a.
6 Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
Davudee Damask vooxhene Arambışde ölkee cun g'oşunbı ulyozar ha'a. Mang'vee manbışike nukarar haa'a, manbışe Davudus nalok'bı qele giviyğal. Davud nyaqa hark'ıneeyir, Rəbbee mana ğama'ananiy.
7 Davide anatenga zishango zagolide za akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
Mang'vee Hadadezerıne insanaaşin k'ınəəğəken g'alxanbı alyaat'u, İyerusalimqa qadayle.
8 Mfumu Davide inatenga mkuwa wambiri kuchokera ku Beta ndi Berotai, mizinda ya Hadadezeri.
Paççah Davudee, Hadadezerne Betaxiy Berotay donane şaharbışeençe geed yez adayle.
9 Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri,
Xamatne paççahık'le Toik'le Davud Hadadezerne gırgıne g'oşunulecar ğamxhava g'iyxhe.
10 anatumiza mwana wake Yoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Yoramu anabweretsa ziwiya zasiliva, zagolide ndi zamkuwa.
Hadadezeree hammaşee Toika dəv'ə haa'a vuxha. Hadadezerıle ğamxhava Davud nəxüriyva qiyghanas, sayir mana tabrik ha'asva paççah Toiyee dix Yoram mang'une k'anyaqa g'ıxele. Yoramee Davudus k'ınəəğəyn, nuk'rayn, yezan karbı adayle.
11 Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko onse amene anawagonjetsa:
Paççah Davudee in cus adıyn k'ınəəğəyken, nuk'rayken, yezaken, vucee menne milletbışike g'ayşuyn karbı Rəbbis g'iysar.
12 Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki. Iye anaperekanso zolanda ku nkhondo zochokera kwa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba.
Mang'vee Edombışike, Moavbışike, Ammonbışike, Filiştinaaşike, Amalekbışike g'ayşuyn karbı Rəbbis g'iysar. Davudee Tsovayne paççahısse Rexovna dix eyxhene Hadadezerıssed g'ayşuyn karbıd Rəbbis g'iysar.
13 Ndipo Davide anatchuka atabwera kokakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
Davudee Q'evane q'aadalil Edombışda yits'ımoled aazır insan oot'al-ooxal hı'ı siyk'almee, mana gırgıng'uk'le ats'axhxhena.
14 Iye anayika maboma mʼdera lonse la Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
Edomne gırgıne suralqa mang'vee cun g'oşunbı ulyoozar hı'iyle qiyğa, Edombı mang'un g'ular vooxhe. Davud nyaqa hark'ıneeyir Rəbbee mana ğama'ananiy.
15 Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
Davud İzrailynacar paççah eyxhe. Mang'vee millet qotkuda vuk'lek ıkkekka, gırgıngunemeeyir mana qorkura ıxha.
16 Yowabu mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika.
Tseruya donane zəiyfayna dix Yoav g'oşunna xərna ıxha. Axiludna dix Yehoşafat taarix oyk'anna ıxha.
17 Zadoki mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Seraya anali mlembi;
Axituvna dix Tsadokiy Evyatarna dix Aximelek kaahinar vuxha. Seraya mirza ıxha.
18 Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti; ndipo ana a Davide anali ansembe.
Yehoyadayna dix Benaya Keretbışdayiy Peletbışda xərna ıxha. Davudun dixbı kaahinar vuxha.

< 2 Samueli 8 >