< 2 Samueli 8 >

1 Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndi kuwapambana ndipo analanda Metegi Ama kuchoka mʼmanja mwa Afilistiwo.
Depois disso, David bateu nos filisteus e os subjugou; e David tirou o freio da cidade mãe da mão dos filisteus.
2 Davide anagonjetsanso Amowabu. Iye anawalamula kuti agone pansi mʼmizere itatu pa gulu lililonse ndipo anawayeza ndi chingwe. Pa gulu lililonse ankapha anthu amene anali pa mizere iwiri yoyamba, kusiyapo mzere wachitatu. Kotero Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Davide ndipo ankapereka msonkho.
Ele derrotou Moab e os mediu com a linha, fazendo-os deitar no chão; e mediu duas linhas até a morte, e uma linha completa para se manterem vivos. Os moabitas se tornaram servos de David, e trouxeram tributo.
3 Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
David também atingiu Hadadezer, filho de Rehob, rei de Zobah, quando ele foi recuperar seu domínio no rio.
4 Davide analanda magaleta 1,000, anthu 7,000 okwera magaleta pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
David tirou dele mil setecentos cavaleiros e vinte mil homens de pé. Davi empurrou os cavalos das carruagens, mas reservou o suficiente deles para cem carruagens.
5 Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
Quando os sírios de Damasco vieram para ajudar Hadadezer, rei de Zobah, David atingiu vinte e dois mil homens dos sírios.
6 Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
Então Davi colocou guarnições na Síria de Damasco; e os sírios se tornaram servos de Davi, e trouxeram tributo. Yahweh deu vitória a Davi onde quer que ele fosse.
7 Davide anatenga zishango zagolide za akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
David pegou os escudos de ouro que estavam sobre os servos de Hadadezer, e os trouxe para Jerusalém.
8 Mfumu Davide inatenga mkuwa wambiri kuchokera ku Beta ndi Berotai, mizinda ya Hadadezeri.
De Betah e de Berothai, cidades de Hadadezer, o rei Davi tomou uma grande quantidade de bronze.
9 Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri,
Quando Toi, rei de Hamath, soube que David havia atingido todo o exército de Hadadezer,
10 anatumiza mwana wake Yoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Yoramu anabweretsa ziwiya zasiliva, zagolide ndi zamkuwa.
então Toi enviou seu filho Jorão ao rei David para saudá-lo e abençoá-lo, pois ele havia lutado contra Hadadezer e batido nele; pois Hadadezer tinha guerras com Toi. Jorão trouxe com ele vasos de prata, vasos de ouro e vasos de bronze.
11 Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko onse amene anawagonjetsa:
O rei David também os dedicou a Iavé, com a prata e o ouro que ele dedicou a todas as nações que ele subjugou -
12 Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki. Iye anaperekanso zolanda ku nkhondo zochokera kwa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba.
da Síria, dos Moab, dos filhos de Amon, dos filisteus, de Amalek, e do saque de Hadadezer, filho de Rehob, rei de Zobah.
13 Ndipo Davide anatchuka atabwera kokakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
David ganhou uma reputação quando retornou do ataque a dezoito mil homens dos sírios no Vale do Sal.
14 Iye anayika maboma mʼdera lonse la Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
Ele colocou guarnições em Edom. Em todos os Edom, ele colocou guarnições, e todos os Edomitas se tornaram servos de Davi. Yahweh deu vitória a David para onde quer que ele fosse.
15 Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
David reinou sobre todo Israel; e David executou justiça e retidão para todo o seu povo.
16 Yowabu mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika.
Joabe, filho de Zeruia, estava sobre o exército, Jeosafá, filho de Ailude, era registrador,
17 Zadoki mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Seraya anali mlembi;
Zadoque, filho de Aitube, e Aimeleque, filho de Abiatar, eram sacerdotes, Seraías, escriba,
18 Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti; ndipo ana a Davide anali ansembe.
Benaías, filho de Jeoiada, estava sobre os queretitas e os peletitas; e os filhos de Davi eram ministros chefes.

< 2 Samueli 8 >