< 2 Samueli 8 >

1 Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndi kuwapambana ndipo analanda Metegi Ama kuchoka mʼmanja mwa Afilistiwo.
Stalo se potom, že porazil David Filistinské, a zemdlil je; i vzal David Meteg Amma z ruky Filistinských.
2 Davide anagonjetsanso Amowabu. Iye anawalamula kuti agone pansi mʼmizere itatu pa gulu lililonse ndipo anawayeza ndi chingwe. Pa gulu lililonse ankapha anthu amene anali pa mizere iwiri yoyamba, kusiyapo mzere wachitatu. Kotero Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Davide ndipo ankapereka msonkho.
Porazil také Moábské a změřil je provazcem, na zemi je rozprostíraje; a odměřil jich dva provazce k zbití a celý provazec k živení. I učiněni jsou Moábští Davidovi služebníci, a dávali jemu plat.
3 Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
Porazil též David Hadadezera syna Rohobova, krále Soba, když byl vytáhl, aby rozšířil končiny své až k řece Eufraten.
4 Davide analanda magaleta 1,000, anthu 7,000 okwera magaleta pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
A pobral mu David tisíc vozů a sedm set jezdců, a dvadceti tisíc mužů pěších, a zpodřezoval David žily všechněm koňům vozníkům; toliko zanechal z nich ke stu vozům.
5 Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
Přitáhli pak byli Syrští od Damašku na pomoc Hadadezerovi králi Soba, ale David porazil z Syrských dvamecítma tisíc mužů.
6 Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
Tedy osadil David stráží Syrii Damašskou, a byli Syrští služebníci Davidovi, dávajíce plat; nebo zachovával Hospodin Davida, kamžkoli se obrátil.
7 Davide anatenga zishango zagolide za akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
Pobral také David štíty zlaté, kteréž měli služebníci Hadadezerovi, a přinesl je do Jeruzaléma.
8 Mfumu Davide inatenga mkuwa wambiri kuchokera ku Beta ndi Berotai, mizinda ya Hadadezeri.
Z Betach též a z Berot, měst Hadadezerových, nabral král David velmi mnoho mědi.
9 Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri,
A když uslyšel Tohi král Emat, že porazil David všecko vojsko Hadadezerovo,
10 anatumiza mwana wake Yoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Yoramu anabweretsa ziwiya zasiliva, zagolide ndi zamkuwa.
Poslal Tohi Jorama syna svého k králi Davidovi, aby ho pozdravil přátelsky, a spolu s ním se radoval z toho, že šťastně bojoval s Hadadezerem, a porazil ho; (nebo Hadadezer vedl válku proti Tohi). Kterýžto přinesl s sebou nádoby stříbrné, též nádoby zlaté a nádoby měděné.
11 Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko onse amene anawagonjetsa:
Ty také obětoval král David Hospodinu s stříbrem a zlatem posvěceným ze všech národů, kteréž podmanil,
12 Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki. Iye anaperekanso zolanda ku nkhondo zochokera kwa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba.
Totiž z Syrských a Moábských, též z synů Ammon a z Filistinských, i z Amalechitských a z kořistí Hadadezera syna Rohobova, krále Soba.
13 Ndipo Davide anatchuka atabwera kokakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
Zvelebil také David své jméno, když se navracoval od pobití osmnácti tisíců Syrských v údolí solnatém.
14 Iye anayika maboma mʼdera lonse la Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
Protož i nad Idumejskými stráž postavil, všecku krajinu Idumejskou stráží osadiv. I učiněni jsou všickni Idumejští služebníci Davidovi; nebo zachovával Hospodin Davida, kamž se koli obrátil.
15 Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
I kraloval David nade vším Izraelem, a činil David soud a spravedlnost všemu lidu svému.
16 Yowabu mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika.
Joáb pak syn Sarvie byl nad vojskem, a Jozafat syn Achiludův kancléřem;
17 Zadoki mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Seraya anali mlembi;
Sádoch také syn Achitobův a Achimelech syn Abiatarův kněžími, a Saraiáš písařem.
18 Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti; ndipo ana a Davide anali ansembe.
Benaiáš pak syn Joiadův byl nad Cheretejskými a Peletejskými, a synové Davidovi knížaty.

< 2 Samueli 8 >