< 2 Samueli 7 >

1 Mfumu itakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, Yehova atayipatsa mpumulo kwa adani ake onse woyizungulira,
Kwasekusithi lapho inkosi yayihlezi endlini yayo, leNkosi isiyiphumuzile inhlangothi zonke ezitheni zayo zonke,
2 mfumuyo inawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Mulungu lili mu tenti.”
inkosi yathi kuNathani umprofethi: Akubone, mina ngihlala endlini yemisedari, kodwa umtshokotsho kaNkulunkulu uhlala phakathi kwamakhetheni.
3 Natani anayankha mfumu kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu chifukwa Yehova ali nanu.”
UNathani wasesithi enkosini: Hamba wenze konke okusenhliziyweni yakho, ngoba iNkosi ilawe.
4 Usiku umenewo mawu a Yehova anafika kwa Natani ndipo anati,
Kodwa kwathi ngalobobusuku, ilizwi leNkosi lafika kuNathani lisithi:
5 “Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti: kodi ndiwe amene udzandimangira Ine nyumba yokhalamo?
Hamba uthi encekwini yami, kuDavida: Itsho njalo iNkosi: Wena uzangakhela yini indlu ukuze ngihlale kiyo?
6 Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda uku ndi uku ndipo mokhala mwanga munali mu tenti.
Ngoba kangizange ngihlale endlini kusukela osukwini engenyusa ngalo abantwana bakoIsrayeli eGibhithe kuze kube lamuhla, kodwa bengihamba ethenteni lethabhanekeleni.
7 Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense atsogoleri awo, amene ndinamulamula kuweta anthu anga Aisraeli kuti, nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
Kuzo zonke izindawo engihambe kuzo labo bonke abantwana bakoIsrayeli, ngake ngakhuluma ilizwi yini kwesinye sezizwe zakoIsrayeli, engasilaya ukwelusa abantu bami uIsrayeli ngisithi: Kungani lingangakhelanga indlu yemisedari?
8 “Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
Ngakho-ke uzakutsho njalo encekwini yami, kuDavida, uthi: Itsho njalo iNkosi yamabandla: Mina ngakuthatha esibayeni sezimvu, ekulandeleni izimvu, ukuba ngumbusi phezu kwabantu bami, phezu kukaIsrayeli;
9 Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
ngangilawe loba ngaphi lapho oya khona, ngaquma zonke izitha zakho ngaphambi kwakho; ngakwenzela ibizo elikhulu njengebizo labakhulu abasemhlabeni.
10 Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja,
Njalo ngizabamisela indawo abantu bami uIsrayeli, ngibagxumeke ukuze bahlale endaweni yabo, bangabe besanyikinyeka; labantwana benkohlakalo kabasayikubahlupha, njengakuqala,
11 monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzakupatsaninso mpumulo kwa adani anu onse. “‘Yehova akulengeza kwa iwe kuti Iye mwini adzakhazikitsa banja lako:
njalo kusukela osukwini engalaya ngalo abahluleli phezu kwabantu bami uIsrayeli; ngikuphumuze ezitheni zakho zonke. Futhi iNkosi iyakutshela ukuthi iNkosi izakwenzela indlu.
12 Masiku ako akadzatha ndipo ukadzakapuma ndi makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, imene idzachokera mʼthupi mwako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
Lapho insuku zakho sezigcwalisekile, usulele laboyihlo, ngizamisa inzalo yakho emva kwakho, ezaphuma emibilini yakho, ngiqinise umbuso wayo.
13 Iye ndiye amene adzamangire nyumba Dzina langa, ndipo Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
Yona izakwakhela ibizo lami indlu; njalo ngizaqinisa isihlalo sobukhosi sombuso wayo kuze kube nininini.
14 Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Akadzachita choyipa, Ineyo ndidzamulanga ndi ndodo ndi zikwapu za anthu.
Mina ngizakuba nguyise, layo ibe yindodana yami; ezakuthi uba isenza okubi, ngizayijezisa ngentonga yabantu, langemivimvinya yabantwana babantu.
15 Koma sindidzasiya kumukonda, monga ndinachitira ndi Sauli, amene ndinamuchotsa iwe usanakhale mfumu.
Kodwa umusa wami kawuyikusuka kiyo njengalokho ngawususa kuSawuli engamsusa ngaphambi kwakho.
16 Nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhala zamuyaya pamaso panga. Mpando wako waufumu udzakhazikika kwamuyaya!’”
Lendlu yakho lombuso wakho kuzaqiniswa kuze kube nininini phambi kwami; isihlalo sakho sobukhosi sizaqiniswa kuze kube nininini.
17 Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
Njengokwalamazwi wonke lanjengokwalo wonke lo umbono, ngokunjalo uNathani wakhuluma kuDavida.
18 Choncho Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati: “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ine ndine yani, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?”
Yasingena inkosi uDavida, yahlala phambi kweNkosi, yathi: Ngingubani mina, Nkosi Jehova, lendlu yami iyini, ukuthi ungifikise kuze kube lapha?
19 Ndipo kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Kodi umu ndi mmene mumachitira ndi munthu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse?
Kanti lokhu kusekuncinyane emehlweni akho, Nkosi Jehova; usukhulumile futhi ngendlu yenceku yakho ngokwesikhathi esikhatshana; lalokhu yindlela yabantu, Nkosi Jehova.
20 Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu? Pakuti Inu Ambuye Wamphamvuzonse mukumudziwa mtumiki wanu.
Pho, uDavida angabe esengezelela ngokuthini kuwe? Ngoba wena uyayazi inceku yakho, Nkosi Jehova.
21 Chifukwa cha mawu anu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwachiwulula kwa mtumiki wanu.
Ngenxa yelizwi lakho lanjengokwenhliziyo yakho wenzile zonke lezizinto ezinkulu ukuze uzazise inceku yakho.
22 Inu ndinu wamkulu, Yehova Wamphamvuzonse! Palibe wina wofanana nanu, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha, monga tamvera ndi makutu athu.
Ngakho umkhulu, Nkosi Jehova; ngoba kakho onjengawe, njalo kakho uNkulunkulu ngaphandle kwakho, njengakho konke esikuzwileyo ngendlebe zethu.
23 Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina ndi milungu yawo pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
Yisiphi-ke isizwe esisodwa emhlabeni esinjengabantu bakho, njengoIsrayeli, uNkulunkulu owaya ukuzihlengela sona ukuba ngabantu, njalo wazenzela ibizo, walenzela izinto ezinkulu lezesabekayo, kusenzelwa ilizwe lakho, phambi kwabantu bakho, owazihlengela bona eGibhithe, ezizweni lakubonkulunkulu bazo?
24 Inu mwawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
Wasuziqinisela abantu bakho uIsrayeli ukuze babe ngabantu kuwe kuze kube nininini; lawe Nkosi usube nguNkulunkulu wabo.
25 “Ndipo tsopano Yehova Mulungu, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake. Chitani monga mwalonjezera,
Khathesi-ke, Nkosi Nkulunkulu, ilizwi olikhulume ngenceku yakho langendlu yayo liqinise kuze kube nininini, wenze njengokukhuluma kwakho.
26 kotero dzina lanu lidzakhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
Njalo kalibe likhulu ibizo lakho kuze kube nininini, kuthiwe: INkosi yamabandla inguNkulunkulu phezu kukaIsrayeli; lendlu yenceku yakho uDavida imiswe phambi kwakho.
27 “Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, mwaululira mtumiki wanu ponena kuti, ‘Ine ndidzakumangira iwe nyumba!’ Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
Ngoba wena, Nkosi yamabandla, Nkulunkulu kaIsrayeli, wembule endlebeni yenceku yakho, usithi: Ngizakwakhela indlu. Ngakho inceku yakho ithole enhliziyweni yayo ukuthi ikhuleke lumkhuleko kuwe.
28 Inu Ambuye Wamphamvuzonse, ndinu Mulungu! Mawu anu ndi odalirika, ndipo mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
Khathesi-ke, Nkosi Jehova, wena ungulowoNkulunkulu, lamazwi akho aliqiniso; ukhulume encekwini yakho lokhu okuhle.
29 Ndipo tsopano chikukomereni kudalitsa banja la mtumiki wanu, kuti likhale mpaka muyaya pamaso panu. Pakuti Inu, Yehova Wamphamvuzonse, mwayankhula, ndipo ndi mʼdalitso wanu banja la mtumiki wanu lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”
Ngakho-ke akuvume ubusise indlu yenceku yakho ukuze ibe phambi kwakho kuze kube nininini; ngoba wena, Nkosi Jehova, ukhulumile; langesibusiso sakho indlu yenceku yakho izabusiswa kuze kube nininini.

< 2 Samueli 7 >