< 2 Samueli 7 >

1 Mfumu itakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, Yehova atayipatsa mpumulo kwa adani ake onse woyizungulira,
Lorsque le roi habitait dans sa maison et que Yahvé lui avait accordé du repos contre tous ses ennemis de tous les côtés,
2 mfumuyo inawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Mulungu lili mu tenti.”
le roi dit à Nathan, le prophète: « Voici, j'habite dans une maison de cèdre, mais l'arche de Dieu habite dans des courtines. »
3 Natani anayankha mfumu kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu chifukwa Yehova ali nanu.”
Nathan dit au roi: « Va, fais tout ce que tu as dans le cœur, car Yahvé est avec toi. »
4 Usiku umenewo mawu a Yehova anafika kwa Natani ndipo anati,
Cette même nuit, la parole de Yahvé fut adressée à Nathan, en ces termes:
5 “Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti: kodi ndiwe amene udzandimangira Ine nyumba yokhalamo?
Va dire à mon serviteur David: « Yahvé dit: Veux-tu me construire une maison pour que j'y habite?
6 Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda uku ndi uku ndipo mokhala mwanga munali mu tenti.
Car je n'ai pas habité dans une maison depuis le jour où j'ai fait monter les enfants d'Israël hors d'Égypte, jusqu'à ce jour, mais je me suis déplacé dans une tente et dans un tabernacle.
7 Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense atsogoleri awo, amene ndinamulamula kuweta anthu anga Aisraeli kuti, nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
Dans tous les lieux où j'ai marché avec tous les enfants d'Israël, j'ai dit à quelqu'un des tribus d'Israël à qui j'avais ordonné d'être le berger de mon peuple d'Israël: « Pourquoi ne m'avez-vous pas bâti une maison de cèdre? ».
8 “Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
Maintenant, dites ceci à mon serviteur David: Yahvé des armées dit: « Je t'ai pris de la bergerie, de la suite des brebis, pour être prince sur mon peuple, sur Israël.
9 Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
J'ai été avec toi partout où tu es allé, et j'ai exterminé tous tes ennemis devant toi. Je te ferai un grand nom, comme le nom des grands qui sont sur la terre.
10 Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja,
J'établirai un lieu pour mon peuple d'Israël, et je le planterai, afin qu'il habite dans son lieu et ne soit plus déplacé. Les enfants du mal ne les affligeront plus, comme au début,
11 monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzakupatsaninso mpumulo kwa adani anu onse. “‘Yehova akulengeza kwa iwe kuti Iye mwini adzakhazikitsa banja lako:
et comme depuis le jour où j'ai ordonné à des juges d'être à la tête de mon peuple d'Israël. Je vous ferai reposer de tous vos ennemis. De plus, Yahvé te dit que Yahvé te fera une maison.
12 Masiku ako akadzatha ndipo ukadzakapuma ndi makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, imene idzachokera mʼthupi mwako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
Lorsque tes jours seront accomplis et que tu te coucheras avec tes pères, j'établirai ta descendance après toi, qui sortira de ton corps, et j'établirai son règne.
13 Iye ndiye amene adzamangire nyumba Dzina langa, ndipo Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
Il bâtira une maison à mon nom, et j'établirai pour toujours le trône de son royaume.
14 Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Akadzachita choyipa, Ineyo ndidzamulanga ndi ndodo ndi zikwapu za anthu.
Je serai son père, et il sera mon fils. S'il commet l'iniquité, je le châtierai avec la verge des hommes et avec les coups des enfants des hommes;
15 Koma sindidzasiya kumukonda, monga ndinachitira ndi Sauli, amene ndinamuchotsa iwe usanakhale mfumu.
mais ma bonté ne se retirera pas de lui, comme je l'ai fait pour Saül, que j'ai rejeté devant toi.
16 Nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhala zamuyaya pamaso panga. Mpando wako waufumu udzakhazikika kwamuyaya!’”
Ta maison et ton royaume seront assurés pour toujours devant toi. Ton trône sera affermi pour toujours. »'"
17 Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
Nathan adressa à David toutes ces paroles, et selon toute cette vision.
18 Choncho Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati: “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ine ndine yani, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?”
Alors le roi David entra et s'assit devant l'Éternel; et il dit: Qui suis-je, Seigneur Éternel, et quelle est ma maison, pour que tu m'aies conduit jusqu'ici?
19 Ndipo kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Kodi umu ndi mmene mumachitira ndi munthu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse?
C'était encore peu de chose à tes yeux, Seigneur Éternel, mais tu as parlé de la maison de ton serviteur pour un temps encore long, et cela parmi les hommes, Seigneur Éternel!
20 Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu? Pakuti Inu Ambuye Wamphamvuzonse mukumudziwa mtumiki wanu.
Que peut encore te dire David? Car tu connais ton serviteur, Seigneur Yahvé.
21 Chifukwa cha mawu anu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwachiwulula kwa mtumiki wanu.
C'est à cause de ta parole, et selon ton propre cœur, que tu as fait toute cette grandeur, pour la faire connaître à ton serviteur.
22 Inu ndinu wamkulu, Yehova Wamphamvuzonse! Palibe wina wofanana nanu, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha, monga tamvera ndi makutu athu.
C'est pourquoi tu es grand, Yahvé Dieu. Car il n'y a personne comme toi, et il n'y a pas d'autre Dieu que toi, d'après tout ce que nous avons entendu de nos oreilles.
23 Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina ndi milungu yawo pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
Quelle nation sur la terre est semblable à ton peuple, à Israël, que Dieu est allé racheter pour en faire un peuple, et pour se faire un nom, et pour faire de grandes choses pour toi, et des choses redoutables pour ton pays, devant ton peuple, que tu as racheté pour toi hors d'Égypte, d'entre les nations et leurs dieux?
24 Inu mwawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
Tu as établi pour toi ton peuple Israël, pour qu'il soit ton peuple à jamais; et toi, Yahvé, tu es devenu son Dieu.
25 “Ndipo tsopano Yehova Mulungu, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake. Chitani monga mwalonjezera,
« Maintenant, Yahvé Dieu, la parole que tu as prononcée sur ton serviteur et sur sa maison, confirme-la à jamais, et fais ce que tu as dit.
26 kotero dzina lanu lidzakhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
Que ton nom soit à jamais glorifié, en disant: L'Éternel des armées est Dieu sur Israël, et la maison de ton serviteur David sera affermie devant toi.
27 “Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, mwaululira mtumiki wanu ponena kuti, ‘Ine ndidzakumangira iwe nyumba!’ Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
Car toi, Éternel des armées, Dieu d'Israël, tu as révélé à ton serviteur: Je te bâtirai une maison. C'est pourquoi ton serviteur a trouvé dans son cœur de t'adresser cette prière.
28 Inu Ambuye Wamphamvuzonse, ndinu Mulungu! Mawu anu ndi odalirika, ndipo mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
« Maintenant, Seigneur Yahvé, tu es Dieu, et tes paroles sont vérité, et tu as promis ce bien à ton serviteur.
29 Ndipo tsopano chikukomereni kudalitsa banja la mtumiki wanu, kuti likhale mpaka muyaya pamaso panu. Pakuti Inu, Yehova Wamphamvuzonse, mwayankhula, ndipo ndi mʼdalitso wanu banja la mtumiki wanu lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”
Maintenant donc, qu'il te plaise de bénir la maison de ton serviteur, afin qu'elle subsiste à jamais devant toi, car c'est toi, Seigneur Yahvé, qui l'as dit. Que la maison de ton serviteur soit bénie à jamais par ta bénédiction. »

< 2 Samueli 7 >