< 2 Samueli 7 >

1 Mfumu itakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, Yehova atayipatsa mpumulo kwa adani ake onse woyizungulira,
Forsothe it was doon, whanne the kyng Dauid hadde sete in his hows, and the Lord hadde youe reste to hym on ech side fro alle hise enemyes,
2 mfumuyo inawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Mulungu lili mu tenti.”
he seyde to Nathan the prophete, Seest thou not, that Y dwelle in an hows of cedre, and the arke of God is put in the myddis of skynnys?
3 Natani anayankha mfumu kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu chifukwa Yehova ali nanu.”
And Nathan seide to the kyng, Go thou, and do al thing which is in thin herte, for the Lord is with thee.
4 Usiku umenewo mawu a Yehova anafika kwa Natani ndipo anati,
Forsothe it was don in that niyt, and lo! the word of the Lord, seiynge to Nathan, Go thou,
5 “Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti: kodi ndiwe amene udzandimangira Ine nyumba yokhalamo?
and speke to my servaunt Dauid, The Lord seith these thingis, Whether thou schalt bilde to me an hows to dwelle ynne?
6 Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda uku ndi uku ndipo mokhala mwanga munali mu tenti.
For Y `dwellide not in an hows fro the dai in which Y ledde the sones of Israel out of the lond of Egipt til in to this dai; but Y yede in tabernacle and in tent,
7 Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense atsogoleri awo, amene ndinamulamula kuweta anthu anga Aisraeli kuti, nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
bi alle places, to whiche Y passyde with alle the sones of Israel? Whether Y spekynge spak to oon of the lynagis of Israel, to whom Y comaundyde, that he schulde feede my puple Israel, and seide, Whi `bildidist thou not an hows of cedre to me?
8 “Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
And now thou schalt seie these thingis to my seruaunt Dauid, The Lord of oostis seith these thingis, Y took thee fro lesewis suynge flockis, that thou schuldist be duyk on my puple Israel, and Y was with thee in alle thingis,
9 Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
where euere thou yedist, and Y killide alle thin enemyes fro thi face, and Y made to thee a greet name bi the name of grete men that ben in erthe;
10 Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja,
and Y schall sette a place to my puple Israel, and Y schal plaunte hym, and Y schal dwelle with hym, and he schal no more be troblid, and the sones of wickidnesse schulen not adde, that thei turmente hym as bifor,
11 monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzakupatsaninso mpumulo kwa adani anu onse. “‘Yehova akulengeza kwa iwe kuti Iye mwini adzakhazikitsa banja lako:
fro the dai in which Y ordenede iugis on my puple Israel; and Y schal yyue reste to thee fro alle thin enemyes. And the Lord biforseith to thee, that `the Lord schal mak an hows to thee;
12 Masiku ako akadzatha ndipo ukadzakapuma ndi makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, imene idzachokera mʼthupi mwako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
and whanne thi daies be fillid, and thou hast slept with thi fadris, Y schal reyse thi seed aftir thee, which schal go out of thi wombe, and Y schal make `stidfast his rewme.
13 Iye ndiye amene adzamangire nyumba Dzina langa, ndipo Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
He schal bilde an hows to my name, and Y schal make stable the troone of his rewme til in to with outen ende;
14 Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Akadzachita choyipa, Ineyo ndidzamulanga ndi ndodo ndi zikwapu za anthu.
Y schal be to hym in to fadir, and he schal be to me in to a sone; and if he schal do ony thing wickidli, Y schal chastise hym in the yerde of men, and in the woundis of the sones of men.
15 Koma sindidzasiya kumukonda, monga ndinachitira ndi Sauli, amene ndinamuchotsa iwe usanakhale mfumu.
Forsothe Y schal not do awey my mercy fro hym, as Y dide awei fro Saul, whom Y remouede fro my face.
16 Nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhala zamuyaya pamaso panga. Mpando wako waufumu udzakhazikika kwamuyaya!’”
And thin hows schal be feithful, and thi rewme schal be til in to with outen ende bifor my face, and thi trone schal be stidfast contynueli.
17 Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
By alle these wordys, and bi al this reuelacioun, so Nathan spak to Dauid.
18 Choncho Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati: “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ine ndine yani, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?”
Forsothe Dauid the kyng entride, and satt bifor the Lord, and seide, Who am Y, my Lord God, and what is myn hows, that thou brouytist me hidur to?
19 Ndipo kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Kodi umu ndi mmene mumachitira ndi munthu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse?
But also this is seyn litil in thi siyt, my Lord God; no but thou schuldist speke also of the hows of thi seruaunt in to long tyme. Forsothe this is the lawe of Adam, Lord God;
20 Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu? Pakuti Inu Ambuye Wamphamvuzonse mukumudziwa mtumiki wanu.
what therfor may Dauid adde yit, that he speke to thee? For thou, Lord God, knowist thi seruaunt; thou hast do alle these grete thingis,
21 Chifukwa cha mawu anu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwachiwulula kwa mtumiki wanu.
for thi word, and bi thin herte, so that thou madist knowun to thi seruaunt.
22 Inu ndinu wamkulu, Yehova Wamphamvuzonse! Palibe wina wofanana nanu, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha, monga tamvera ndi makutu athu.
Herfor, Lord God, thou art magnyfied, for noon is lijk thee, ne there is no God outakun thee, in alle thingis whiche we herden with oure eeris.
23 Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina ndi milungu yawo pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
Sotheli what folk in erthe is as the puple of Israel, for which the Lord God yede, that he schulde ayenbie it to him in to a puple, and schulde sette to hym silf a name, and schulde do to it grete thingis, and orible on erthe, in castinge out therof the folk and `goddis therof fro the face of thi puple, which thou `ayen bouytist to thee fro Egipt?
24 Inu mwawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
And thou confermidist to thee thi puple Israel in to a puple euerlastynge, and thou, Lord, art maad in to God to hem.
25 “Ndipo tsopano Yehova Mulungu, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake. Chitani monga mwalonjezera,
Now therfor, Lord God, reise thou withouten ende the word that thou hast spoke on thi seruaunt and on his hows, and do as thou hast spoke;
26 kotero dzina lanu lidzakhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
and thy name be magnyfied til in to withouten ende, and be it seid, The Lord of oostis is God on Israel; and the hows of thi seruaunt Dauid schal be stablischid byfor the Lord;
27 “Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, mwaululira mtumiki wanu ponena kuti, ‘Ine ndidzakumangira iwe nyumba!’ Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
for thou, Lord of oostis, God of Israel, hast maad reuelacioun to the eere of thi seruaunt, and seidist, Y schal bilde an hows to thee; therfor thi seruaunt foond his herte, that he schulde preie thee bi this preier.
28 Inu Ambuye Wamphamvuzonse, ndinu Mulungu! Mawu anu ndi odalirika, ndipo mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
Now therfor, Lord God, thou art veri God, and thi wordis schulen be trewe; for thou hast spoke these goodis to thi seruaunt;
29 Ndipo tsopano chikukomereni kudalitsa banja la mtumiki wanu, kuti likhale mpaka muyaya pamaso panu. Pakuti Inu, Yehova Wamphamvuzonse, mwayankhula, ndipo ndi mʼdalitso wanu banja la mtumiki wanu lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”
therfor bigynne thou, and blesse the hows of thi seruaunt, that it be withouten ende bifor thee; for thou, Lord God, hast spoke these thingis, and bi thi blessyng the hows of thi seruaunt schal be blessid withouten ende.

< 2 Samueli 7 >