< 2 Samueli 7 >
1 Mfumu itakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, Yehova atayipatsa mpumulo kwa adani ake onse woyizungulira,
and to be for to dwell [the] king in/on/with house: palace his and LORD to rest to/for him from around from all enemy his
2 mfumuyo inawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Mulungu lili mu tenti.”
and to say [the] king to(wards) Nathan [the] prophet to see: behold! please I to dwell in/on/with house: home cedar and ark [the] God to dwell in/on/with midst [the] curtain
3 Natani anayankha mfumu kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu chifukwa Yehova ali nanu.”
and to say Nathan to(wards) [the] king all which in/on/with heart your to go: went to make: do for LORD with you
4 Usiku umenewo mawu a Yehova anafika kwa Natani ndipo anati,
and to be in/on/with night [the] he/she/it and to be word LORD to(wards) Nathan to/for to say
5 “Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti: kodi ndiwe amene udzandimangira Ine nyumba yokhalamo?
to go: went and to say to(wards) servant/slave my to(wards) David thus to say LORD you(m. s.) to build to/for me house: home to/for to dwell me
6 Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda uku ndi uku ndipo mokhala mwanga munali mu tenti.
for not to dwell in/on/with house: home to/for from day: today to ascend: establish I [obj] son: descendant/people Israel from Egypt and till [the] day: today [the] this and to be to go: walk in/on/with tent and in/on/with tabernacle
7 Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense atsogoleri awo, amene ndinamulamula kuweta anthu anga Aisraeli kuti, nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
in/on/with all which to go: walk in/on/with all son: descendant/people Israel word to speak: speak with one tribe: ruler Israel which to command to/for to pasture [obj] people my [obj] Israel to/for to say to/for what? not to build to/for me house: home cedar
8 “Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
and now thus to say to/for servant/slave my to/for David thus to say LORD Hosts I to take: take you from [the] pasture from after [the] flock to/for to be leader upon people my upon Israel
9 Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
and to be with you in/on/with all which to go: went and to cut: eliminate [emph?] [obj] all enemy your from face: before your and to make to/for you name great: large like/as name [the] great: large which in/on/with land: country/planet
10 Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja,
and to set: appoint place to/for people my to/for Israel and to plant him and to dwell underneath: stand him and not to tremble still and not to add: again son: descendant/people injustice to/for to afflict him like/as as which in/on/with first: previous
11 monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzakupatsaninso mpumulo kwa adani anu onse. “‘Yehova akulengeza kwa iwe kuti Iye mwini adzakhazikitsa banja lako:
and to/for from [the] day which to command to judge upon people my Israel and to rest to/for you from all enemy your and to tell to/for you LORD for house: household to make to/for you LORD
12 Masiku ako akadzatha ndipo ukadzakapuma ndi makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, imene idzachokera mʼthupi mwako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
for to fill day your and to lie down: lay down with father your and to arise: establish [obj] seed: children your after you which to come out: produce from belly your and to establish: establish [obj] kingdom his
13 Iye ndiye amene adzamangire nyumba Dzina langa, ndipo Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
he/she/it to build house: home to/for name my and to establish: establish [obj] throne kingdom his till forever: enduring
14 Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Akadzachita choyipa, Ineyo ndidzamulanga ndi ndodo ndi zikwapu za anthu.
I to be to/for him to/for father and he/she/it to be to/for me to/for son: child which in/on/with to pervert he and to rebuke him in/on/with tribe: staff human and in/on/with plague son: child man
15 Koma sindidzasiya kumukonda, monga ndinachitira ndi Sauli, amene ndinamuchotsa iwe usanakhale mfumu.
and kindness my not to turn aside: depart from him like/as as which to turn aside: remove from from with Saul which to turn aside: remove from to/for face: before your
16 Nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhala zamuyaya pamaso panga. Mpando wako waufumu udzakhazikika kwamuyaya!’”
and be faithful house: household your and kingdom your till forever: enduring to/for face: before your throne your to be to establish: establish till forever: enduring
17 Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
like/as all [the] word [the] these and like/as all [the] vision [the] this so to speak: speak Nathan to(wards) David
18 Choncho Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati: “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ine ndine yani, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?”
and to come (in): come [the] king David and to dwell to/for face: before LORD and to say who? I Lord YHWH/God and who? house: household my for to come (in): bring me till here
19 Ndipo kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Kodi umu ndi mmene mumachitira ndi munthu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse?
and be small still this in/on/with eye: appearance your Lord YHWH/God and to speak: speak also to(wards) house: household servant/slave your to/for from distant and this custom [the] man Lord YHWH/God
20 Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu? Pakuti Inu Ambuye Wamphamvuzonse mukumudziwa mtumiki wanu.
and what? to add David still to/for to speak: speak to(wards) you and you(m. s.) to know [obj] servant/slave your Lord YHWH/God
21 Chifukwa cha mawu anu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwachiwulula kwa mtumiki wanu.
in/on/with for the sake of word: promised your and like/as heart your to make: do [obj] all [the] greatness [the] this to/for to know [obj] servant/slave your
22 Inu ndinu wamkulu, Yehova Wamphamvuzonse! Palibe wina wofanana nanu, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha, monga tamvera ndi makutu athu.
upon so to magnify Lord YHWH/God for nothing like you and nothing God exception you in/on/with all which to hear: hear in/on/with ear our
23 Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina ndi milungu yawo pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
and who? like/as people your like/as Israel nation one in/on/with land: country/planet which to go: went God to/for to ransom to/for him to/for people and to/for to set: make to/for him name and to/for to make: do to/for you [the] greatness and to fear: revere to/for land: country/planet your from face: before people your which to ransom to/for you from Egypt nation and God his
24 Inu mwawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
and to establish: establish to/for you [obj] people your Israel to/for you to/for people till forever: enduring and you(m. s.) LORD to be to/for them to/for God
25 “Ndipo tsopano Yehova Mulungu, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake. Chitani monga mwalonjezera,
and now LORD God [the] word which to speak: speak upon servant/slave your and upon house: household his to arise: establish till forever: enduring and to make: do like/as as which to speak: speak
26 kotero dzina lanu lidzakhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
and to magnify name your till forever: enduring to/for to say LORD Hosts God upon Israel and house: household servant/slave your David to be to establish: establish to/for face: before your
27 “Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, mwaululira mtumiki wanu ponena kuti, ‘Ine ndidzakumangira iwe nyumba!’ Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
for you(m. s.) LORD Hosts God Israel to reveal: reveal [obj] ear: to ears servant/slave your to/for to say house: home to build to/for you upon so to find servant/slave your [obj] heart his to/for to pray to(wards) you [obj] [the] prayer [the] this
28 Inu Ambuye Wamphamvuzonse, ndinu Mulungu! Mawu anu ndi odalirika, ndipo mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
and now Lord YHWH/God you(m. s.) he/she/it [the] God and word your to be truth: certain and to speak: promise to(wards) servant/slave your [obj] [the] welfare [the] this
29 Ndipo tsopano chikukomereni kudalitsa banja la mtumiki wanu, kuti likhale mpaka muyaya pamaso panu. Pakuti Inu, Yehova Wamphamvuzonse, mwayankhula, ndipo ndi mʼdalitso wanu banja la mtumiki wanu lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”
and now be willing and to bless [obj] house: household servant/slave your to/for to be to/for forever: enduring to/for face: before your for you(m. s.) Lord YHWH/God to speak: speak and from blessing your to bless house: household servant/slave your to/for forever: enduring