< 2 Samueli 6 >

1 Davide anasonkhanitsanso pamodzi ankhondo 3,000 osankhidwa pakati pa Aisraeli.
David samlede alt udsøgt Mandskab i Israel, 30000 Mand.
2 Iye pamodzi ndi ankhondo ake onse anapita ku Baalahi ku Yuda kukatenga Bokosi la Chipangano la Mulungu, limene limadziwika ndi Dzina lake, dzina la Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pakati pa Akerubi amene ali pa Bokosi la Chipanganolo.
Derpå brød David op med alle sine Krigere og drog til Ba'al i Juda for der at hente Guds Ark, over hvilken Hærskarers HERREs Navn er nævnet, han, som troner over Keruberne.
3 Iwo anayika Bokosi la Mulungu pa ngolo yatsopano nachoka nalo ku nyumba ya Abinadabu, imene inali pa phiri. Uza ndi Ahiyo ana a Abinadabu ndiwo ankayendetsa ngolo yatsopanoyo,
De satte da Guds Ark på en ny Vogn og førte den bort fra Abinadabs Hus på Højen, og Abinadabs Sønner Uzza og Ajo kørte Vognen,
4 imene inanyamula Bokosi la Mulungu, ndipo Ahiyo mwana wa Abinadabu ankayenda patsogolo pake.
således at Uzza gik ved Siden af og Ajo foran Guds Ark.
5 Davide pamodzi ndi Aisraeli onse ankakondwerera ndi mphamvu zawo zonse pamaso pa Yehova poyimba nyimbo pogwiritsa ntchito azeze, apangwe, matambolini, maseche ndi malipenga.
David og hele Israel legede af alle Kræfter for HERRENs Åsyn til Sang og til Citre, Harper, Pauker, Bjælder og Cymbler.
6 Atafika pa malo opunthira tirigu a Nakoni, Uza anatambalitsa dzanja lake kuti agwire Bokosi la Mulungu, chifukwa ngʼombe zinkafuna kugwa.
Men da de kom til Nakons Tærskeplads, rakte Uzza Hånden ud og greb fat i Guds Ark, fordi Okserne snublede.
7 Yehova anapsera mtima Uza chifukwa chochita chinthu chosayenera kuchitika. Choncho Mulungu anamukantha ndipo anafera pomwepo pambali pa Bokosi la Mulungulo.
Da blussede HERRENS Vrede op mod Uzza, og Gud slog ham der, fordi han rakte Hånden ud mod Arken, og han døde på Stedet ved Siden af Guds Ark.
8 Ndipo Davide anakhumudwa chifukwa Yehova anakantha Uza ndipo mpaka lero malowo amatchedwa Perezi Uza.
Men David græmmede sig over, at HERREN havde tilføjet Uzza et Brud. Derfor kaldte man Stedet Perez-Uzza, som det hedder den Dag i Dag.
9 Tsiku limenelo Davide anachita mantha ndi Yehova ndipo anati, “Kodi Bokosi la Yehova lingafike bwanji kwathu?”
Og David grebes den Dag af Frygt for HERREN og sagde: "Hvor kan da HERRENs Ark komme hen hos mig!"
10 Iye sanafunenso kubwera ndi Bokosi la Yehova kawo ku mzinda wake wa Davide. Mʼmalo mwake anapita nalo ku nyumba ya Obedi-Edomu Mgiti.
Og David vilde ikke flytte HERRENs Ark hen hos sig i Davidsbyen, men lod den sætte ind i Gatiten Obed-Edoms Hus.
11 Bokosi la Yehova linakhala mʼnyumba ya Obedi-Edomu Mgiti kwa miyezi itatu, ndipo Yehova anamudalitsa kwambiri iyeyo ndi banja lake lonse.
HERRENs Ark blev så i Gatiten Obed-Edoms Hus tre Måneder, og HERREN velsignede Obed-Edom og hele hans Hus.
12 Tsono Mfumu Davide anawuzidwa kuti, “Yehova wadalitsa nyumba ya Obedi-Edomu ndi zonse zimene ali nazo, chifukwa cha Bokosi la Mulungu.” Choncho Davide anapita kukatenga Bokosi la Mulungu ku nyumba ya Obedi-Edomu ndi kupita nalo ku mzinda wa Davide akukondwera kwambiri.
Da nu Kong David fik Underretning om, at HERREN for Guds Arks Skyld havde velsignet Obed-Edoms Hus og alt, hvad hans var, gik han hen og lod under Festglæde Guds Ark bringe op fra Obed-Edoms Hus til Davidsbyen.
13 Anthu amene ananyamula Bokosi la Yehova ankati akayenda mapazi asanu ndi limodzi, iye ankapereka nsembe ngʼombe yayimuna ndi mwana wangʼombe wonenepa.
Og da de, som bar HERRENs Ark, havde gået seks Skridt, ofrede han en Okse og en Fedekalv.
14 Davide ankavina ndi mphamvu zake zonse pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala,
Og David dansede af alle Kræfter for HERRENs Åsyn, iført en linned Efod.
15 pamene iyeyo pamodzi ndi Aisraeli onse ankabwera ndi Bokosi la Yehova, akufuwula ndi kuyimba malipenga.
Således bragte David og hele Israel HERRENs Ark op under Festjubel og Hornblæsning.
16 Bokosi la Yehova likulowa mu Mzinda wa Davide, Mikala mwana wamkazi wa Sauli ankaona ali pa zenera. Ndipo ataona Mfumu Davide ikulumpha ndi kuvina pamaso pa Yehova, ankamunyogodola mu mtima mwake.
Men da HERRENs Ark kom til Davidsbyen, så Sauls Datter Mikal ud af Vinduet; og da hun så Kong David springe og danse for HERRENs Åsyn, ringeagtede hun ham i sit Hjerte.
17 Iwo anabwera nalo Bokosi la Yehova ndipo analiyika pamalo pake mʼkati mwa tenti imene Davide anayimika ndipo Davideyo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova.
De førte så HERRENs Ark ind og stillede den på Plads midt i det Telt, David havde rejst den, og David ofrede Brændofre og Takofre for HERRENs Åsyn.
18 Atatsiriza kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, iye anadalitsa anthu mʼdzina la Yehova Wamphamvuzonse.
Og da David var færdig med Brændofrene og Takofrene, velsignede han Folket i Hærskarers HERREs Navn
19 Kenaka iye anagawira Aisraeli onsewo, aamuna ndi aakazi, aliyense buledi mmodzi, nthuli yanyama, ndiponso keke yamphesa zowuma. Ndipo anthu onse anachokapo, napita aliyense ku nyumba kwake.
og uddelte til alt Folket, til hver enkelt af hele Israels Mængde, både Mand og Kvinde, et Brød, et Stykke Kød og en Rosinkage; derpå gik alt Folket hver til sit.
20 Davide atabwerera ku nyumba kwake kukadalitsa banja lake, Mikala mwana wamkazi wa Sauli anatuluka kudzakumana naye ndipo anati, “Kodi mfumu ya Israeli ingatero kudzilemekeza kwake lero, kudzithyolathyola pamaso pa akapolo aakazi, antchito ake ngati munthu wamba.”
Men da David vendte hjem for at velsigne sit Hus, gik Sauls Datter Mikal ham i Møde og sagde: "Hvor ærbart Israels Konge opførte sig i Dag, da han blottede sig for sine Undersåtters Trælkvinders Øjne, som letfærdige Mennesker plejer at gøre!"
21 Davide anamuyankha Mikala kuti, “Ndachita zimenezi molemekeza Yehova, amene anandisankha ine kupambana abambo ako, kapenanso kupambana banja la abambo ako. Ndipo anandisankha kuti ndikhale wolamulira Aisraeli, anthu a Yehova. Nʼchifukwa chake ndidzasangalalabe pamaso pa Yehova.
David svarede Mikal: "For HERRENs Åsyn vil jeg lege, så sandt HERREN lever, som udvalgte mig fremfor din Fader og hele hans Hus, så han satte mig til Fyrste over HERRENs Folk Israel; jeg vil lege for HERRENs Åsyn,
22 Ineyo ndidzadzinyoza kuposa apa, ndipo ndidzakhala wonyozeka mʼmaso mwako. Koma pakati pa akapolo aakazi awa amene umanena za iwo, ndidzalemekezedwa.”
selv om jeg derved nedværdiges og synker endnu dybere i dine Øjne; men hos Trælkvinderne, du talte om, skal jeg vinde Ære!"
23 Ndipo Mikala mwana wa Sauli sanakhalenso ndi mwana mpaka anamwalira.
Og Sauls Datter Mikal fik til sin Dødedag intet Barn.

< 2 Samueli 6 >