< 2 Samueli 5 >

1 Mafuko onse a Israeli anabwera kwa Davide ku Hebroni ndipo anati, “Ife ndife mafupa ndi mnofu wanu.
İsrail'in bütün oymakları Hevron'da bulunan Davut'a gelip şöyle dediler: “Biz senin etin, kemiğiniz.
2 Kale lija, pamene Sauli anali mfumu yathu, inu ndinu amene munkatsogolera Aisraeli pa nkhondo zawo. Ndipo Yehova anakuwuzani kuti, ‘Udzaweta anthu anga Aisraeli, ndipo udzakhala mfumu yawo.’”
Geçmişte Saul kralımızken, savaşta İsrail'e komuta eden sendin. RAB sana, ‘Halkım İsrail'i sen güdecek, onlara sen önder olacaksın’ diye söz verdi.”
3 Akuluakulu onse a Israeli atafika kwa Mfumu Davide ku Hebroni, mfumu inachita nawo pangano ku Hebroni pamaso pa Yehova, ndipo anamudzoza Davide kukhala mfumu ya Israeli.
İsrail'in bütün ileri gelenleri Hevron'a, Kral Davut'un yanına gelince, kral RAB'bin önünde orada onlarla bir antlaşma yaptı. Onlar da Davut'u İsrail Kralı olarak meshettiler.
4 Davide anali ndi zaka makumi atatu pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira zaka makumi anayi.
Davut otuz yaşında kral oldu ve kırk yıl krallık yaptı.
5 Analamulira Yuda ali ku Hebroni kwa zaka zisanu ndi ziwiri ndi miyezi isanu ndi umodzi, ndipo ali ku Yerusalemu analamulira Israeli yense ndi Yuda kwa zaka 33.
Hevron'da yedi yıl altı ay Yahuda'ya, Yeruşalim'de otuz üç yıl bütün İsrail'e ve Yahuda'ya krallık yaptı.
6 Mfumu ndi ankhondo ake anapita ku Yerusalemu kukathira nkhondo Ayebusi amene ankakhala kumeneko. Ayebusiwo anamuwuza Davide kuti, “Inu simulowa muno. Ngakhale osaona ndi olumala akhoza kukuthamangitsani.” Iwo ankaganiza kuti, “Davide sangathe kulowa momwemo.”
Kral Davut'la adamları Yeruşalim'de yaşayan Yevuslular'a saldırmak için yola çıktılar. Yevuslular Davut'a, “Sen buraya giremezsin, körlerle topallar bile seni geri püskürtebilir” dediler. “Davut buraya giremez” diye düşünüyorlardı.
7 Komabe Davide analanda linga la Ziyoni, limene ndi mzinda wa Davide.
Ne var ki, Davut Siyon Kalesi'ni ele geçirdi. Daha sonra bu kaleye “Davut Kenti” adı verildi.
8 Pa tsiku limenelo Davide anati, “Aliyense wogonjetsa Ayebusi ayenera kudzera mʼngalande ya madzi kuti akafike kwa iwo amene ndi ‘olumala ndi osaona,’ amene ndi adani a Davide.” Nʼchifukwa chake amanena kuti, “Olumala ndi osaona sadzalowa mʼnyumba yaufumu.”
Davut o gün adamlarına şöyle demişti: “Yevuslular'ı kim yenilgiye uğratırsa Davut'un nefret ettiği şu ‘Topallarla körlere’ su kanalından ulaşmalı!” “Körlerle topallar saraya giremeyecek” denmesinin nedeni işte budur.
9 Tsono Davide anakhazikika mu lingamo ndipo mzindawu anawutcha, Mzinda wa Davide. Iye anamanga malo onse ozungulira kuyambira ku matsitso ozungulira khoma.
Bundan sonra Davut “Davut Kenti” adını verdiği kalede oturmaya başladı. Çevredeki bölgeyi, Millo'dan içeriye doğru uzanan bölümü inşa etti.
10 Ndipo mphamvu za Davide zinkakulirakulira chifukwa anali ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
Davut giderek güçleniyordu. Çünkü Her Şeye Egemen Tanrı RAB onunlaydı.
11 Tsono Hiramu mfumu ya Turo inatumiza amithenga ake kwa Davide, pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndi amisiri a matabwa ndi amisiri a miyala, ndipo anamumangira Davide nyumba yaufumu.
Sur Kralı Hiram Davut'a ulaklar, sedir kütükleri, marangozlar ve taşçılar gönderdi. Bu adamlar Davut için bir saray yaptılar.
12 Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.
Böylece Davut RAB'bin kendisini İsrail Kralı atadığını ve halkı İsrail'in hatırı için krallığını yücelttiğini anladı.
13 Davide atafika ku Yerusalemu kuchokera ku Hebroni, anakwatira azikazi natenganso akazi ena kumeneko, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri.
Davut Hevron'dan ayrıldıktan sonra Yeruşalim'de kendine daha birçok cariye ve karı aldı. Davut'un erkek ve kız çocukları oldu.
14 Mayina a ana amene anabereka ku Yerusalemu ndi awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni,
Davut'un Yeruşalim'de doğan çocuklarının adları şunlardı: Şammua, Şovav, Natan, Süleyman,
15 Ibihari, Elisua, Nefegi, Yafiya,
Yivhar, Elişua, Nefek, Yafia,
16 Elisama, Eliada ndi Elifeleti.
Elişama, Elyada ve Elifelet.
17 Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anakalowa mu linga.
Filistliler Davut'un İsrail Kralı olarak meshedildiğini duyunca, bütün Filist ordusu onu aramak için yola çıktı. Bunu duyan Davut kaleye sığındı.
18 Ndipo Afilisti anabwera ndi kukhala momwazika mʼChigwa cha Refaimu.
Filistliler gelip Refaim Vadisi'ne yayılmışlardı.
19 Davide anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?” Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka ndithu mʼmanja mwako.”
Davut RAB'be danıştı: “Filistliler'e saldırayım mı? Onları elime teslim edecek misin?” RAB Davut'a, “Saldır” dedi, “Onları kesinlikle eline teslim edeceğim.”
20 Choncho Davide anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Yehova waphwanya adani anga ine ndikuona.” Choncho anawatcha malowa Baala Perazimu.
Bunun üzerine Davut Baal-Perasim'e gidip orada Filistliler'i bozguna uğrattı. Sonra, “Her şeyi yarıp geçen sular gibi, RAB düşmanlarımı önümden yarıp geçti” dedi. Bundan ötürü oraya Baal-Perasim adı verildi.
21 Afilisti anasiya mafano awo kumeneko ndipo Davide ndi ankhondo ake anawatenga.
Davut'la adamları, Filistliler'in orada bıraktığı putları alıp götürdüler.
22 Nthawi inanso Afilisti anabweranso namwazikana mʼChigwa cha Refaimu;
Filistliler bir kez daha gelip Refaim Vadisi'ne yayıldılar.
23 Davide anafunsa Yehova ndipo Yehovayo anayankha kuti, “Usapite molunjika koma uzungulire kumbuyo kwawo ndipo ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku.
Davut RAB'be danıştı. RAB şöyle karşılık verdi: “Buradan saldırma! Onları arkadan çevirip pelesenk ağaçlarının önünden saldır.
24 Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukayende mofulumira, chifukwa izi zikasonyeza kuti Yehova ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.”
Pelesenk ağaçlarının tepesinden yürüyüş sesi duyar duymaz, acele et. Çünkü ben Filist ordusunu bozguna uğratmak için önünsıra gitmişim demektir.”
25 Kotero Davide anachita zimene Yehova anamulamulira ndipo anakantha Afilisti njira yonse kuchokera ku Geba mpaka ku Gezeri.
Davut RAB'bin kendisine buyurduğu gibi yaptı ve Filistliler'i Geva'dan Gezer'e kadar bozguna uğrattı.

< 2 Samueli 5 >