< 2 Samueli 5 >

1 Mafuko onse a Israeli anabwera kwa Davide ku Hebroni ndipo anati, “Ife ndife mafupa ndi mnofu wanu.
Entonces todas las tribus de Israel vinieron a David en Hebrón y dijeron: En verdad, somos tu hueso y tu carne.
2 Kale lija, pamene Sauli anali mfumu yathu, inu ndinu amene munkatsogolera Aisraeli pa nkhondo zawo. Ndipo Yehova anakuwuzani kuti, ‘Udzaweta anthu anga Aisraeli, ndipo udzakhala mfumu yawo.’”
En el pasado, cuando Saúl era rey sobre nosotros, eras tú a la cabeza de Israel cuando salían o entraban. Y el Señor te dijo: Tú debes ser el guardián de mi pueblo, Israel y su gobernante.
3 Akuluakulu onse a Israeli atafika kwa Mfumu Davide ku Hebroni, mfumu inachita nawo pangano ku Hebroni pamaso pa Yehova, ndipo anamudzoza Davide kukhala mfumu ya Israeli.
Entonces todos los responsables de Israel vinieron al rey en Hebrón; y el rey David llegó a un acuerdo con ellos en Hebrón delante del Señor; y lo ungieron a David y lo hicieron rey sobre Israel.
4 Davide anali ndi zaka makumi atatu pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira zaka makumi anayi.
David tenía treinta años cuando comenzó a reinar, y fue rey durante cuarenta años.
5 Analamulira Yuda ali ku Hebroni kwa zaka zisanu ndi ziwiri ndi miyezi isanu ndi umodzi, ndipo ali ku Yerusalemu analamulira Israeli yense ndi Yuda kwa zaka 33.
Fue rey sobre Judá en Hebrón durante siete años y seis meses, y en Jerusalén, sobre todo Israel y Judá, durante treinta y tres años.
6 Mfumu ndi ankhondo ake anapita ku Yerusalemu kukathira nkhondo Ayebusi amene ankakhala kumeneko. Ayebusiwo anamuwuza Davide kuti, “Inu simulowa muno. Ngakhale osaona ndi olumala akhoza kukuthamangitsani.” Iwo ankaganiza kuti, “Davide sangathe kulowa momwemo.”
Y el rey y sus hombres fueron a Jerusalén contra los jebuseos, la gente de la tierra; y dijeron a David: No entrarás aquí; sino que los ciegos y los cojos te mantendrán fuera; porque dijeron: David no podrá entrar aquí.
7 Komabe Davide analanda linga la Ziyoni, limene ndi mzinda wa Davide.
Pero David tomó el lugar fuerte de Sión, que es el pueblo de David.
8 Pa tsiku limenelo Davide anati, “Aliyense wogonjetsa Ayebusi ayenera kudzera mʼngalande ya madzi kuti akafike kwa iwo amene ndi ‘olumala ndi osaona,’ amene ndi adani a Davide.” Nʼchifukwa chake amanena kuti, “Olumala ndi osaona sadzalowa mʼnyumba yaufumu.”
Y aquel día, David dijo: Quien haga un ataque a los jebuseos, déjalo subir por la tubería y mata a todos los ciegos y cojos que son odiados por David. Y es por eso que dicen: Los ciegos y los cojos pies débiles pueden no entrar al templo del Señor.
9 Tsono Davide anakhazikika mu lingamo ndipo mzindawu anawutcha, Mzinda wa Davide. Iye anamanga malo onse ozungulira kuyambira ku matsitso ozungulira khoma.
Entonces David tomó la torre fuerte para su lugar de vida, y la llamó pueblo de David. Y David construyó murallas alrededor, desde él milo hacia adentro.
10 Ndipo mphamvu za Davide zinkakulirakulira chifukwa anali ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
Y David se hizo cada vez más grande; porque el Señor, el Dios de los ejércitos, estaba con él.
11 Tsono Hiramu mfumu ya Turo inatumiza amithenga ake kwa Davide, pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndi amisiri a matabwa ndi amisiri a miyala, ndipo anamumangira Davide nyumba yaufumu.
E Hiram, rey de Tiro, envió hombres a David, con cedros, carpinteros y canteros; y construyeron el palacio de David.
12 Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.
Y David vio que él Señor había salvado su posición de rey sobre Israel, y que había engrandecido su reino en atención a su pueblo Israel.
13 Davide atafika ku Yerusalemu kuchokera ku Hebroni, anakwatira azikazi natenganso akazi ena kumeneko, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri.
Después de que él viniera de Hebrón, David tomó más mujeres y esposas en Jerusalén, y tuvo más hijos e hijas.
14 Mayina a ana amene anabereka ku Yerusalemu ndi awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni,
Estos son los nombres de aquellos cuyo nacimiento tuvo lugar en Jerusalén: Samúa y Sobab y Natán y Salomón,
15 Ibihari, Elisua, Nefegi, Yafiya,
E Ibhar, Elisua, Nefeg, y Jafia,
16 Elisama, Eliada ndi Elifeleti.
Y Elisama, Eliada y Elifelet.
17 Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anakalowa mu linga.
Y cuando los filisteos tuvieron noticias de que David había sido hecho rey sobre Israel, todos subieron en busca de David; y David, oyéndolo, descendió a la fortaleza.
18 Ndipo Afilisti anabwera ndi kukhala momwazika mʼChigwa cha Refaimu.
Y cuando llegaron los filisteos, fueron en todas direcciones en el valle de Refaim.
19 Davide anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?” Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka ndithu mʼmanja mwako.”
Y David, deseando instrucciones del Señor, dijo: ¿Debo subir contra los filisteos? ¿Los entregarás en mis manos? Y el Señor dijo: Sube, porque ciertamente entregaré a los filisteos en tus manos.
20 Choncho Davide anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Yehova waphwanya adani anga ine ndikuona.” Choncho anawatcha malowa Baala Perazimu.
Entonces David fue a Baal-perazim y los venció allí; y él dijo: El Señor ha dejado que las fuerzas que luchan contra mí se rompan ante mí como se rompe un muro por las aguas que corren. Así que ese lugar se llamaba Baal-perazim.
21 Afilisti anasiya mafano awo kumeneko ndipo Davide ndi ankhondo ake anawatenga.
Y cuando los filisteos huyeron, no se llevaron sus imágenes con ellos, y David y sus hombres se los llevaron.
22 Nthawi inanso Afilisti anabweranso namwazikana mʼChigwa cha Refaimu;
Y volvieron los filisteos otra vez, y se fueron en todas direcciones en el valle de Refaim.
23 Davide anafunsa Yehova ndipo Yehovayo anayankha kuti, “Usapite molunjika koma uzungulire kumbuyo kwawo ndipo ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku.
Y cuando David fue en dirección al Señor, él le dijo: No debes subir contra ellos delante de ellos; pero haz un círculo alrededor de ellos desde la parte posterior y ven sobre ellos frente a los árboles de especias.
24 Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukayende mofulumira, chifukwa izi zikasonyeza kuti Yehova ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.”
Luego, al oír un ruido como de pasos en las copas de los árboles, avanza rápidamente, porque el Señor ha salido delante de ti para vencer al ejército de los filisteos.
25 Kotero Davide anachita zimene Yehova anamulamulira ndipo anakantha Afilisti njira yonse kuchokera ku Geba mpaka ku Gezeri.
E hizo David como él Señor le había dicho; y venció a los filisteos, atacándolos desde Gabaón hasta cerca de Gezer.

< 2 Samueli 5 >