< 2 Samueli 5 >

1 Mafuko onse a Israeli anabwera kwa Davide ku Hebroni ndipo anati, “Ife ndife mafupa ndi mnofu wanu.
И приидоша вся племена Израилева к Давиду в Хеврон и глаголаша ему: се, кости твоя и плоть твоя мы есмы:
2 Kale lija, pamene Sauli anali mfumu yathu, inu ndinu amene munkatsogolera Aisraeli pa nkhondo zawo. Ndipo Yehova anakuwuzani kuti, ‘Udzaweta anthu anga Aisraeli, ndipo udzakhala mfumu yawo.’”
и вчера и третияго дне Саулу сущу царю над нами, ты был еси вводяй и изводяй Израиля, и рече Господь к тебе: ты упасеши люди Моя Израиля и ты будеши вождь людем Моим Израилю.
3 Akuluakulu onse a Israeli atafika kwa Mfumu Davide ku Hebroni, mfumu inachita nawo pangano ku Hebroni pamaso pa Yehova, ndipo anamudzoza Davide kukhala mfumu ya Israeli.
И приидоша вси старейшины Израилевы к царю в Хеврон, и положи им царь Давид завет в Хевроне пред Господем: и помазаша Давида на царство над всем Израилем.
4 Davide anali ndi zaka makumi atatu pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira zaka makumi anayi.
Сын тридесяти лет Давид внегда воцаритися ему, и царствова четыредесять лет:
5 Analamulira Yuda ali ku Hebroni kwa zaka zisanu ndi ziwiri ndi miyezi isanu ndi umodzi, ndipo ali ku Yerusalemu analamulira Israeli yense ndi Yuda kwa zaka 33.
седмь лет и месяцей шесть царствова в Хевроне над Иудою, и тридесять три лета царствова над всем Израилем и Иудою во Иерусалиме.
6 Mfumu ndi ankhondo ake anapita ku Yerusalemu kukathira nkhondo Ayebusi amene ankakhala kumeneko. Ayebusiwo anamuwuza Davide kuti, “Inu simulowa muno. Ngakhale osaona ndi olumala akhoza kukuthamangitsani.” Iwo ankaganiza kuti, “Davide sangathe kulowa momwemo.”
И пойде Давид и вси мужие его во Иерусалим ко Иевусею, живущему на земли той. И реша Давиду: не внидеши семо, яко восташа хромии и слепии глаголюще: яко не внидет Давид семо.
7 Komabe Davide analanda linga la Ziyoni, limene ndi mzinda wa Davide.
И взя Давид крепость Сионю: сия есть град Давидов.
8 Pa tsiku limenelo Davide anati, “Aliyense wogonjetsa Ayebusi ayenera kudzera mʼngalande ya madzi kuti akafike kwa iwo amene ndi ‘olumala ndi osaona,’ amene ndi adani a Davide.” Nʼchifukwa chake amanena kuti, “Olumala ndi osaona sadzalowa mʼnyumba yaufumu.”
И рече Давид в день той: всяк поражаяй Иевусеа да касается мечем и хромых и слепых и ненавидящих души Давидовы. Сего ради рекут: слепии и хромии не внидут в дом Господень.
9 Tsono Davide anakhazikika mu lingamo ndipo mzindawu anawutcha, Mzinda wa Davide. Iye anamanga malo onse ozungulira kuyambira ku matsitso ozungulira khoma.
И седе Давид в крепости, и наречеся сия град Давидов: и созда той град около от Краеградия, и дом свой.
10 Ndipo mphamvu za Davide zinkakulirakulira chifukwa anali ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
И идяше Давид идый и величаемь, и Господь Вседержитель с ним.
11 Tsono Hiramu mfumu ya Turo inatumiza amithenga ake kwa Davide, pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndi amisiri a matabwa ndi amisiri a miyala, ndipo anamumangira Davide nyumba yaufumu.
И посла Хирам царь Тирский послы к Давиду, и древа кедрова, и древоделей, и каменоделателей, и создаша дом Давиду.
12 Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.
И уразуме Давид, яко уготова его Господь в царя над Израилем, и яко вознесеся царство его людий Его ради Израиля.
13 Davide atafika ku Yerusalemu kuchokera ku Hebroni, anakwatira azikazi natenganso akazi ena kumeneko, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri.
И поят Давид еще жены и подложницы от Иерусалима по пришествии своем от Хеврона: и быша Давиду еще сынове и дщери.
14 Mayina a ana amene anabereka ku Yerusalemu ndi awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni,
И сия имена родившымся ему во Иерусалиме: Самус и Совав, и Нафан и Соломон,
15 Ibihari, Elisua, Nefegi, Yafiya,
и Евеар и Елисуе, и Нафек и Иефие,
16 Elisama, Eliada ndi Elifeleti.
и Елисама и Елидае и Елифалаф, Самае, Иесиваф, Нафан, Галамаан, Иеваар, Феисус, Елифалаф, Нагеф, Нафек, Ианафан и Леасамис, Ваалимаф, Елифааф.
17 Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anakalowa mu linga.
И услышаша иноплеменницы, яко помазася Давид царь над Израилем, и взыдоша вси иноплеменницы искати Давида. И услыша Давид, и сниде в крепость.
18 Ndipo Afilisti anabwera ndi kukhala momwazika mʼChigwa cha Refaimu.
Иноплеменницы же приидоша и соединишася во юдоли Титанстей.
19 Davide anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?” Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka ndithu mʼmanja mwako.”
И вопроси Давид Господа, глаголя: взыду ли ко иноплеменником? И предаси ли я в руце мои? И рече Господь к Давиду: взыди, яко предая предам иноплеменники в руце твои.
20 Choncho Davide anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Yehova waphwanya adani anga ine ndikuona.” Choncho anawatcha malowa Baala Perazimu.
И прииде Давид с Вышних Сечей и посече иноплеменники тамо. И рече Давид: изсече Господь враги моя иноплеменники предо мною, якоже пресекаются воды. Сего ради наречеся имя места того Свыше Сечей.
21 Afilisti anasiya mafano awo kumeneko ndipo Davide ndi ankhondo ake anawatenga.
И оставиша тамо (иноплеменницы) боги своя, и взя их Давид и мужие иже с ним (и рече Давид сожещи их во огни).
22 Nthawi inanso Afilisti anabweranso namwazikana mʼChigwa cha Refaimu;
И приложиша паки приити иноплеменницы и собрашася на юдоли Титанстей.
23 Davide anafunsa Yehova ndipo Yehovayo anayankha kuti, “Usapite molunjika koma uzungulire kumbuyo kwawo ndipo ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku.
И вопроси Давид Господа: взыду ли ко иноплеменником? И предаси ли их в руце мои? И рече ему Господь: не исходи на сретение им, но уклонися от них, и приступиши к ним близ дубравы плача:
24 Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukayende mofulumira, chifukwa izi zikasonyeza kuti Yehova ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.”
и будет, егда услышиши глас шума от дубравы плача, тогда снидеши к ним, яко тогда изыдет Господь пред тобою сещи на брани иноплеменники.
25 Kotero Davide anachita zimene Yehova anamulamulira ndipo anakantha Afilisti njira yonse kuchokera ku Geba mpaka ku Gezeri.
И сотвори Давид, якоже заповеда ему Господь, и изби иноплеменники от Гаваона даже до земли Газира.

< 2 Samueli 5 >