< 2 Samueli 5 >
1 Mafuko onse a Israeli anabwera kwa Davide ku Hebroni ndipo anati, “Ife ndife mafupa ndi mnofu wanu.
Zonke izizwana zako-Israyeli zaya kuDavida eHebhroni zathi, “Thina siyinyama yakho legazi lakho.
2 Kale lija, pamene Sauli anali mfumu yathu, inu ndinu amene munkatsogolera Aisraeli pa nkhondo zawo. Ndipo Yehova anakuwuzani kuti, ‘Udzaweta anthu anga Aisraeli, ndipo udzakhala mfumu yawo.’”
Esikhathini esedlulayo, uSawuli eseseyinkosi yethu, wena nguwe owawukhokhela u-Israyeli emkhankasweni wakhe wezimpi. LoThixo wathi kuwe, ‘Wena uzakuba ngumelusi wabantu bami u-Israyeli, njalo uzakuba ngumbusi wabo.’”
3 Akuluakulu onse a Israeli atafika kwa Mfumu Davide ku Hebroni, mfumu inachita nawo pangano ku Hebroni pamaso pa Yehova, ndipo anamudzoza Davide kukhala mfumu ya Israeli.
Kwathi abadala bonke bako-Israyeli sebefikile enkosini uDavida eHebhroni, inkosi yenza isivumelwano labo eHebhroni phambi kukaThixo, basebegcoba uDavida ukuba abe yinkosi ko-Israyeli.
4 Davide anali ndi zaka makumi atatu pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira zaka makumi anayi.
UDavida waba yinkosi eleminyaka engamatshumi amathathu, wabusa iminyaka engamatshumi amane.
5 Analamulira Yuda ali ku Hebroni kwa zaka zisanu ndi ziwiri ndi miyezi isanu ndi umodzi, ndipo ali ku Yerusalemu analamulira Israeli yense ndi Yuda kwa zaka 33.
EHebhroni wabusa uJuda iminyaka eyisikhombisa lezinyanga eziyisithupha, kwathi eJerusalema wabusa u-Israyeli wonke loJuda iminyaka engamatshumi amathathu lantathu.
6 Mfumu ndi ankhondo ake anapita ku Yerusalemu kukathira nkhondo Ayebusi amene ankakhala kumeneko. Ayebusiwo anamuwuza Davide kuti, “Inu simulowa muno. Ngakhale osaona ndi olumala akhoza kukuthamangitsani.” Iwo ankaganiza kuti, “Davide sangathe kulowa momwemo.”
Inkosi labantu bayo baya eJerusalema ukuyahlasela amaJebusi ayehlala khona. AmaJebusi athi kuDavida, “Kawuyikungena lapha; leziphofu labaqhulayo bangakuvimba.” Acabanga athi, “UDavida angeke angene lapha.”
7 Komabe Davide analanda linga la Ziyoni, limene ndi mzinda wa Davide.
Kodwa uDavida wayithumba inqaba yaseZiyoni, uMuzi kaDavida.
8 Pa tsiku limenelo Davide anati, “Aliyense wogonjetsa Ayebusi ayenera kudzera mʼngalande ya madzi kuti akafike kwa iwo amene ndi ‘olumala ndi osaona,’ amene ndi adani a Davide.” Nʼchifukwa chake amanena kuti, “Olumala ndi osaona sadzalowa mʼnyumba yaufumu.”
Ngalolosuku uDavida wathi, “Lowo onqoba amaJebusi kuzamele asebenzise umgelo wamanzi ukuba afinyelele ‘abaqhulayo leziphofu’ labo abayizitha zikaDavida.” Yikho-nje besithi, “Iziphofu labaqhulayo” kabayikungena esigodlweni.
9 Tsono Davide anakhazikika mu lingamo ndipo mzindawu anawutcha, Mzinda wa Davide. Iye anamanga malo onse ozungulira kuyambira ku matsitso ozungulira khoma.
UDavida wasehlala enqabeni waseyibiza ngokuthi nguMuzi kaDavida. Wakha enhlangothini zonke zayo kusukela emadundulwini ayelapho kusiya phakathi.
10 Ndipo mphamvu za Davide zinkakulirakulira chifukwa anali ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
Waqhubeka njalo esiba lamandla ngoba uThixo uNkulunkulu uSomandla wayelaye.
11 Tsono Hiramu mfumu ya Turo inatumiza amithenga ake kwa Davide, pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndi amisiri a matabwa ndi amisiri a miyala, ndipo anamumangira Davide nyumba yaufumu.
Ngalesosikhathi uHiramu inkosi yaseThire wathuma izithunywa kuDavida zilezigodo zemisedari lababazi bamapulanka kanye lababazi bamatshe, bakhela uDavida isigodlo.
12 Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.
UDavida wakwazi ukuthi uThixo wayembekile ukuba abe yinkosi yako-Israyeli wawuphakamisa lombuso wakhe ngenxa yabantu bakhe u-Israyeli.
13 Davide atafika ku Yerusalemu kuchokera ku Hebroni, anakwatira azikazi natenganso akazi ena kumeneko, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri.
Esesukile eHebhroni uDavida wathatha abanye abafazi beceleni kanye labafazi eJerusalema, kwazalwa amanye amadodana lamadodakazi futhi.
14 Mayina a ana amene anabereka ku Yerusalemu ndi awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni,
Nanka amabizo abantwana abazalelwa khona: uShamuwa, uShobabi, uNathani, uSolomoni,
15 Ibihari, Elisua, Nefegi, Yafiya,
u-Ibhari, u-Elishuwa, uNefegi, uJafiya,
16 Elisama, Eliada ndi Elifeleti.
u-Elishama, u-Eliyada kanye lo-Elifelethi.
17 Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anakalowa mu linga.
Kwathi amaFilistiya esezwe ukuthi uDavida wayegcotshwe ukuba yinkosi yako-Israyeli wonke aphuma ehlome ephelele esiyamdinga, kodwa uDavida wakuzwa lokho wasesehlela enqabeni.
18 Ndipo Afilisti anabwera ndi kukhala momwazika mʼChigwa cha Refaimu.
AmaFilistiya ayesefikile njalo esegcwele eSigodini saseRefayi,
19 Davide anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?” Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka ndithu mʼmanja mwako.”
ngakho uDavida wabuza uThixo wathi, “Ngingayawahlasela amaFilistiya na? Uzawanikela kimi na?” UThixo wamphendula wathi, “Hamba, ngoba impela amaFilistiya ngizawanikela kuwe.”
20 Choncho Davide anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Yehova waphwanya adani anga ine ndikuona.” Choncho anawatcha malowa Baala Perazimu.
Ngakho uDavida waya eBhali Pherazimi, lapho awehlula khona. Wathi, “Njengamanzi efohla, uThixo ufohlele ezitheni zami phambi kwami.” Ngakho leyondawo yasibizwa ngokuthi yiBhali Pherazimi.
21 Afilisti anasiya mafano awo kumeneko ndipo Davide ndi ankhondo ake anawatenga.
AmaFilistiya abaleka atshiya izithombe zawo khonapho, uDavida labantu bakhe bazithatha bahamba lazo.
22 Nthawi inanso Afilisti anabweranso namwazikana mʼChigwa cha Refaimu;
AmaFilistiya aphinda njalo abuya, agcwala eSigodini saseRefayi;
23 Davide anafunsa Yehova ndipo Yehovayo anayankha kuti, “Usapite molunjika koma uzungulire kumbuyo kwawo ndipo ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku.
ngakho uDavida wabuza uThixo, yena waphendula wathi, “Ungayi uqondile, kodwa bhoda ngemva kwawo uwahlasele maqondana lezihlahla zebhalisamu.
24 Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukayende mofulumira, chifukwa izi zikasonyeza kuti Yehova ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.”
Kuzakuthi lapho usizwa izisinde zabahambayo ezihlahleni zebhalisamu, uqhubeke ngokuphangisa, ngoba lokho kuzakutsho ukuthi uThixo usehambe phambi kwakho ukuyahlasela amabutho amaFilistiya.”
25 Kotero Davide anachita zimene Yehova anamulamulira ndipo anakantha Afilisti njira yonse kuchokera ku Geba mpaka ku Gezeri.
Ngakho uDavida wenza njengokulaywa kwakhe nguThixo, njalo amaFilistiya wawacakazela phansi umango wonke kusukela eGibhiyoni kusiya eGezeri.