< 2 Samueli 5 >

1 Mafuko onse a Israeli anabwera kwa Davide ku Hebroni ndipo anati, “Ife ndife mafupa ndi mnofu wanu.
And alle the lynagis of Israel camen to Dauid, in Ebron, and seiden, Lo! we ben thi boon and thi fleisch.
2 Kale lija, pamene Sauli anali mfumu yathu, inu ndinu amene munkatsogolera Aisraeli pa nkhondo zawo. Ndipo Yehova anakuwuzani kuti, ‘Udzaweta anthu anga Aisraeli, ndipo udzakhala mfumu yawo.’”
But also yistirdai and the thridde day ago, whanne Saul was kyng on vs, thou leddist out, and leddist ayen Israel; forsothe the Lord seide to thee, Thou schalt fede my puple Israel, and thou schalt be duyk on Israel.
3 Akuluakulu onse a Israeli atafika kwa Mfumu Davide ku Hebroni, mfumu inachita nawo pangano ku Hebroni pamaso pa Yehova, ndipo anamudzoza Davide kukhala mfumu ya Israeli.
Also and the eldere men of Israel camen to the kyng, in Ebron; and kyng Dauid smoot with hem boond of pees in Ebron, bifor the Lord; and thei anoyntiden Dauid in to kyng on Israel.
4 Davide anali ndi zaka makumi atatu pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira zaka makumi anayi.
Dauid was a sone of thretti yeer, whanne he bigan to regne, and he regnyde fourti yeer in Ebron;
5 Analamulira Yuda ali ku Hebroni kwa zaka zisanu ndi ziwiri ndi miyezi isanu ndi umodzi, ndipo ali ku Yerusalemu analamulira Israeli yense ndi Yuda kwa zaka 33.
he regnede on Juda seuene yeer and sixe monethis; forsothe in Jerusalem he regnede thretti and thre yeer, on al Israel and Juda.
6 Mfumu ndi ankhondo ake anapita ku Yerusalemu kukathira nkhondo Ayebusi amene ankakhala kumeneko. Ayebusiwo anamuwuza Davide kuti, “Inu simulowa muno. Ngakhale osaona ndi olumala akhoza kukuthamangitsani.” Iwo ankaganiza kuti, “Davide sangathe kulowa momwemo.”
And the kyng yede, and alle men that weren with hym, in to Jerusalem, to Jebusey, dweller of the lond. And it was seide of hem to Dauid, Thou schalt not entre hidur, no but thou do awei blynde men and lame, seiynge, Dauid schal not entre hydur.
7 Komabe Davide analanda linga la Ziyoni, limene ndi mzinda wa Davide.
Forsothe Dauid took the tour of Syon; this is the citee of Dauid.
8 Pa tsiku limenelo Davide anati, “Aliyense wogonjetsa Ayebusi ayenera kudzera mʼngalande ya madzi kuti akafike kwa iwo amene ndi ‘olumala ndi osaona,’ amene ndi adani a Davide.” Nʼchifukwa chake amanena kuti, “Olumala ndi osaona sadzalowa mʼnyumba yaufumu.”
For Dauid hadde `sette forth meede in that dai to hym, that hadde smyte Jebusei, and hadde touchid the goteris of roouys, and hadde take awey lame men and blynde, hatynge the lijf of Dauid. Therfor it is seid in prouerbe, A blynde man and lame schulen not entre in to the temple.
9 Tsono Davide anakhazikika mu lingamo ndipo mzindawu anawutcha, Mzinda wa Davide. Iye anamanga malo onse ozungulira kuyambira ku matsitso ozungulira khoma.
Forsothe Dauid dwellide in the tour, and clepide it the citee of Dauid; and he bildide bi cumpas fro Mello, and with ynne.
10 Ndipo mphamvu za Davide zinkakulirakulira chifukwa anali ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
And he entride profitynge and encreessynge; and the Lord God of oostis was with hym.
11 Tsono Hiramu mfumu ya Turo inatumiza amithenga ake kwa Davide, pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndi amisiri a matabwa ndi amisiri a miyala, ndipo anamumangira Davide nyumba yaufumu.
Also Hyram, kyng of Tire, sent messangeris to Dauid, and cedre trees, and crafti men of trees, and crafti men of stoonus to wallis; and thei bildiden the hows of Dauid.
12 Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.
And Dauid knew, that the Lord hadde confermed hym kyng on Israel, and that he hadde enhaunsid his rewme on his puple Israel.
13 Davide atafika ku Yerusalemu kuchokera ku Hebroni, anakwatira azikazi natenganso akazi ena kumeneko, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri.
Therfor Dauid took yit concubyns, and wyues of Jerusalem, after that he cam fro Ebron; and also othere sones and douytris weren borun to Dauid.
14 Mayina a ana amene anabereka ku Yerusalemu ndi awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni,
And these ben the names of hem that weren borun to hym in Jerusalem; Samua, and Sobab, and Nathan,
15 Ibihari, Elisua, Nefegi, Yafiya,
and Salomon, and Jobaar, and Helisua,
16 Elisama, Eliada ndi Elifeleti.
and Repheg, and Japhia, and Helysama, and Holida, and Heliphelech.
17 Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anakalowa mu linga.
Therfor Filisteis herden, that thei hadden anoyntid Dauid kyng on Israel, and alle Filisteis stieden to seke Dauid. And whanne Dauid hadde herd this, he yede doun into a strong hold.
18 Ndipo Afilisti anabwera ndi kukhala momwazika mʼChigwa cha Refaimu.
Forsothe Filisteis camen, and weren spred abrood in the valei of Raphaym.
19 Davide anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?” Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka ndithu mʼmanja mwako.”
And Dauid counseilide the Lord, and seide, Whether Y schal stie to Filisties, and whether thou schalt yyue hem in myn hond? And the Lord seide to Dauid, Stie thou, for Y schal bitake, and Y schal yyue Filisteis in thin hond.
20 Choncho Davide anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Yehova waphwanya adani anga ine ndikuona.” Choncho anawatcha malowa Baala Perazimu.
Therfor Dauid cam in to Baal Farasym, and smoot hem there, and seide, The Lord departide myn enemyes bifor me, as watris ben departid. Therfor the name of that place was clepid Baal Farasym.
21 Afilisti anasiya mafano awo kumeneko ndipo Davide ndi ankhondo ake anawatenga.
And thei leften there her sculptils, whiche Dauid took, and hise men.
22 Nthawi inanso Afilisti anabweranso namwazikana mʼChigwa cha Refaimu;
And Filisteis addiden yit, that thei schulden stie, and thei weren spred abrood in the valey of Raphaym.
23 Davide anafunsa Yehova ndipo Yehovayo anayankha kuti, “Usapite molunjika koma uzungulire kumbuyo kwawo ndipo ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku.
Sotheli Dauid councelide the Lord, and seide, Whether Y schal stie agens Filisties, and whether thou schalt bitake hem in to myn hondis? Which answeride, Thou schalt not stie ayens hem, but cumpasse thou bihynde her bak, and thou schalt come to hem on the contrarie side of the pere trees.
24 Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukayende mofulumira, chifukwa izi zikasonyeza kuti Yehova ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.”
And whanne thou schalt here the sown of cry goynge in the cop of `pere trees, thanne thou schalt biginne batel; for thanne the Lord schal go out befor thi face, that he smyte the castels of Filisteis.
25 Kotero Davide anachita zimene Yehova anamulamulira ndipo anakantha Afilisti njira yonse kuchokera ku Geba mpaka ku Gezeri.
Therfor Dauid dide as the Lord comaundide to hym; and he smoot Filisteys fro Gabaa til `the while thei camen to Jezer.

< 2 Samueli 5 >