< 2 Samueli 5 >
1 Mafuko onse a Israeli anabwera kwa Davide ku Hebroni ndipo anati, “Ife ndife mafupa ndi mnofu wanu.
Then came all the tribes of Israel to Dauid vnto Hebron, and said thus, Beholde, we are thy bones and thy flesh.
2 Kale lija, pamene Sauli anali mfumu yathu, inu ndinu amene munkatsogolera Aisraeli pa nkhondo zawo. Ndipo Yehova anakuwuzani kuti, ‘Udzaweta anthu anga Aisraeli, ndipo udzakhala mfumu yawo.’”
And in time past when Saul was our King, thou leddest Israel in and out: and the Lord hath sayde to thee, Thou shalt feede my people Israel, and thou shalt be a captaine ouer Israel.
3 Akuluakulu onse a Israeli atafika kwa Mfumu Davide ku Hebroni, mfumu inachita nawo pangano ku Hebroni pamaso pa Yehova, ndipo anamudzoza Davide kukhala mfumu ya Israeli.
So all the Elders of Israel came to the King to Hebron: and King Dauid made a couenant with them in Hebron before the Lord: and they anoynted Dauid King ouer Israel.
4 Davide anali ndi zaka makumi atatu pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira zaka makumi anayi.
Dauid was thirtie yeere olde when he began to reigne: and hee reigned fortie yeere.
5 Analamulira Yuda ali ku Hebroni kwa zaka zisanu ndi ziwiri ndi miyezi isanu ndi umodzi, ndipo ali ku Yerusalemu analamulira Israeli yense ndi Yuda kwa zaka 33.
In Hebron hee reigned ouer Iudah seuen yeere, and sixe moneths: and in Ierusalem hee reigned thirtie and three yeeres ouer all Israel and Iudah.
6 Mfumu ndi ankhondo ake anapita ku Yerusalemu kukathira nkhondo Ayebusi amene ankakhala kumeneko. Ayebusiwo anamuwuza Davide kuti, “Inu simulowa muno. Ngakhale osaona ndi olumala akhoza kukuthamangitsani.” Iwo ankaganiza kuti, “Davide sangathe kulowa momwemo.”
The King also and his men went to Ierusalem vnto the Iebusites, the inhabitants of the land: who spake vnto Dauid, saying, Except thou take away the blinde and the lame, thou shalt not come in hither: thinking that Dauid coulde not come thither.
7 Komabe Davide analanda linga la Ziyoni, limene ndi mzinda wa Davide.
But Dauid tooke the fort of Zion: this is the citie of Dauid.
8 Pa tsiku limenelo Davide anati, “Aliyense wogonjetsa Ayebusi ayenera kudzera mʼngalande ya madzi kuti akafike kwa iwo amene ndi ‘olumala ndi osaona,’ amene ndi adani a Davide.” Nʼchifukwa chake amanena kuti, “Olumala ndi osaona sadzalowa mʼnyumba yaufumu.”
Nowe Dauid had sayd the same day, Whosoeuer smiteth the Iebusites, and getteth vp to the gutters and smiteth the lame and blinde, which Dauids soule hateth, I will preferre him: therefore they saide, The blinde and the lame shall not come into that house.
9 Tsono Davide anakhazikika mu lingamo ndipo mzindawu anawutcha, Mzinda wa Davide. Iye anamanga malo onse ozungulira kuyambira ku matsitso ozungulira khoma.
So Dauid dwelt in that forte, and called it the citie of Dauid, and Dauid built rounde about it, from Millo, and inward.
10 Ndipo mphamvu za Davide zinkakulirakulira chifukwa anali ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
And Dauid prospered and grewe: for the Lord God of hostes was with him.
11 Tsono Hiramu mfumu ya Turo inatumiza amithenga ake kwa Davide, pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndi amisiri a matabwa ndi amisiri a miyala, ndipo anamumangira Davide nyumba yaufumu.
Hiram also king of Tyrus sent messengers to Dauid, and cedar trees, and carpenters, and masons for walles: and they built Dauid an house.
12 Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.
Then Dauid knewe that the Lord had stablished him King ouer Israel, and that he had exalted his kingdome for his people Israels sake.
13 Davide atafika ku Yerusalemu kuchokera ku Hebroni, anakwatira azikazi natenganso akazi ena kumeneko, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri.
And Dauid tooke him more concubines and wiues out of Ierusalem, after hee was come from Hebron, and more sonnes and daughters were borne to Dauid.
14 Mayina a ana amene anabereka ku Yerusalemu ndi awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni,
And these bee the names of the sonnes that were borne vnto him in Ierusale: Shammua, and Shobab, and Nathan, and Salomon,
15 Ibihari, Elisua, Nefegi, Yafiya,
And Ibhar, and Elishua, and Nepheg, and Iaphia,
16 Elisama, Eliada ndi Elifeleti.
And Elishama, and Eliada, and Eliphalet.
17 Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anakalowa mu linga.
But when the Philistims hearde that they had anoynted Dauid King ouer Israel, all the Philistims came vp to seeke Dauid: and when Dauid heard, he went downe to a fort.
18 Ndipo Afilisti anabwera ndi kukhala momwazika mʼChigwa cha Refaimu.
But the Philistims came, and spred themselues in the valley of Rephaim.
19 Davide anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?” Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka ndithu mʼmanja mwako.”
Then Dauid asked counsel of the Lord, saying, Shall I goe vp to the Philistims? wilt thou deliuer them into mine handes? And the Lord answered Dauid, Goe vp: for I will doubtlesse deliuer the Philistims into thine handes.
20 Choncho Davide anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Yehova waphwanya adani anga ine ndikuona.” Choncho anawatcha malowa Baala Perazimu.
Then Dauid came to Baal-perazim, and smote them there, and sayde, The Lord hath deuided mine enemies asunder before mee, as waters be deuided asunder: therefore he called the name of that place, Baal-perazim.
21 Afilisti anasiya mafano awo kumeneko ndipo Davide ndi ankhondo ake anawatenga.
And there they left their images, and Dauid and his men burnt them.
22 Nthawi inanso Afilisti anabweranso namwazikana mʼChigwa cha Refaimu;
Againe the Philistims came vp, and spred themselues in the valley of Rephaim.
23 Davide anafunsa Yehova ndipo Yehovayo anayankha kuti, “Usapite molunjika koma uzungulire kumbuyo kwawo ndipo ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku.
And when Dauid asked counsell of the Lord, hee answered, Thou shalt not goe vp, but turne about behinde them, and come vpon them ouer against the mulberie trees.
24 Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukayende mofulumira, chifukwa izi zikasonyeza kuti Yehova ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.”
And when thou hearest the noyse of one going in the toppes of the mulberie trees, then remoue: for then shall the Lord goe out before thee, to smite the hoste of the Philistims.
25 Kotero Davide anachita zimene Yehova anamulamulira ndipo anakantha Afilisti njira yonse kuchokera ku Geba mpaka ku Gezeri.
Then Dauid did so as the Lord had commanded him, and smote the Philistims from Geba, vntil thou come to Gazer.