< 2 Samueli 4 >

1 Isiboseti mwana wa Sauli atamva kuti Abineri waphedwa ku Hebroni, anataya mtima ndipo Aisraeli onse anachita mantha kwambiri.
А кад чу син Саулов да је погинуо Авенир у Хеврону, клонуше му руке, и сав се Израиљ смете.
2 Koma Isiboseti anali ndi anthu akuluakulu awiri amene ankatsogolera magulu a ankhondo. Mmodzi mwa iwo dzina lake linali Baana ndipo mnzakeyo anali Rekabu. Iwo anali ana a Rimoni wa banja la Beeroti wa fuko la Benjamini Beeroti. Iwo ankatengedwa ngati mbali imodzi ya Benjamini,
А имаше син Саулов две војводе над четама; једном беше име Вана, другом беше име Рихав, синови Римона Вироћанина, од синова Венијаминових; јер се и Вирот бројаше Венијамину;
3 chifukwa anthu a ku Beeroti anathawira ku Gitaimu ndipo akhala ali kumeneko ngati alendo mpaka lero lino.
А Вироћани беху побегли у Гитајим, где осташе као дошљаци до данашњег дана.
4 (Yonatani mwana wa Sauli anali ndi mwana wamwamuna amene anali wolumala mapazi ake onse awiri. Iye anali ndi zaka zisanu pamene nkhani ya Sauli ndi Yonatani inamveka kuchokera ku Yezireeli. Amene amamulera anamunyamula ndi kuthawa naye, koma pamene amachita zinthu mofulumira mwanayo anagwa ndipo analumala. Dzina lake linali Mefiboseti).
И имаше Јонатан, син Саулов, сина хромог на ногу, коме беше пет година кад дође глас о смрти Сауловој и Јонатановој из Језраела, те га узе дадиља његова и побеже, и кад брзо бежаше, он паде и охрону; а име му беше Мефивостеј.
5 Choncho Rekabu ndi Baana ana a Rimoni wa ku Beeroti ananyamuka kupita ku nyumba ya Isi-Boseti, ndipo anafika nthawi ya masana kukutentha pamene iye amapumula.
И пођоше синови Римона Вироћанина, Рихав и Вана, и дођоше у подне у кућу Исвостејеву; а он почиваше у подне.
6 Iwo analowa mʼchipinda chamʼkati ngati kuti amakatenga tirigu, ndipo anamulasa mʼmimba. Kenaka Rekabu ndi mʼbale wake Baana anathawa.
И уђоше у кућу као да узму пшенице, и прободоше га под пето ребро Рихав и Вана, и побегоше.
7 Iwo analowa mʼnyumbamo iye akugona pa bedi mʼchipinda chake. Atamulasa ndi kumupha, anadula mutu wake nʼkuwutenga, nayenda usiku wonse mʼnjira yopita ku Araba.
Кад уђоше у кућу, он лежаше на постељи својој у клети где спаваше, те га прободоше и убише, и одсекоше му главу и узеше је, па отидоше путем преко поља целу ону ноћ.
8 Iwo anabweretsa mutu wa Isi-Boseti kwa Davide ku Hebroni ndipo anati kwa mfumu, “Nawu mutu wa Isiboseti mwana wa Sauli, mdani wanu, amene anafuna kukuphani. Lero lino Yehova wabwezera mbuye wanga mfumu adani anu, Sauli ndi ana ake.”
И донесоше главу Исвостејеву Давиду у Хеврон, и рекоше цару: Ево главе Исвостеја сина Сауловог, непријатеља твог, који је тражио душу твоју; и Господ освети данас цара, господара мог, од Саула и семена његовог.
9 Davide anayankha Rekabu ndi mʼbale wake Baana, ana a Rimoni wa ku Beeroti kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene wandipulumutsa ku mavuto anga onse,
Али Давид одговарајући Рихаву и Вану, брату његовом, синовима Римона Вироћанина, рече им: Тако да је жив Господ, који је избавио душу моју из сваке невоље.
10 pamene munthu wina anandiwuza kuti, ‘Sauli wafa’ ndipo ankaganiza kuti wabweretsa nkhani yabwino, ine ndinamugwira ndi kumupha ku Zikilagi. Iyi inali mphotho imene ndinapereka kwa iyeyo chifukwa cha uthenga wake!
Кад оног који ми јави говорећи: Гле, погибе Саул, и мишљаше да ће ми јавити добре гласе, ухватих и убих у Сиклагу, и то му би од мене дар за гласе његове,
11 Nanji pamene anthu oyipa apha munthu wosalakwa ali mʼnyumba mwake ndiponso pa bedi lake! Kodi ine ndingaleke kukulangani ndi kukuchotsani pa dziko lapansi pano?”
А камоли људе безбожне, који убише човека правог, у кући његовој, на постељи његовој! Нећу ли тражити крв његову из ваших руку, и вас истребити са земље?
12 Kotero Davide analamulira ankhondo ake, ndipo anawapha. Iwo anawadula manja ndi mapazi ndi kupachika matupi awo pa dziwe la ku Hebroni. Koma anatenga mutu wa Isi-Boseti nawuyika mʼmanda a Abineri ku Hebroni.
И заповеди Давид момцима својим, те их погубише, и одсекоше им руке и ноге, и обесише код језера хевронског; а главу Исвостејеву узеше и погребоше у гробу Авенировом у Хеврону.

< 2 Samueli 4 >