< 2 Samueli 4 >

1 Isiboseti mwana wa Sauli atamva kuti Abineri waphedwa ku Hebroni, anataya mtima ndipo Aisraeli onse anachita mantha kwambiri.
Lapho isizwile indodana kaSawuli ukuthi uAbhineri ufele eHebroni, izandla zakhe zaba buthakathaka, loIsrayeli wonke wakhathazeka.
2 Koma Isiboseti anali ndi anthu akuluakulu awiri amene ankatsogolera magulu a ankhondo. Mmodzi mwa iwo dzina lake linali Baana ndipo mnzakeyo anali Rekabu. Iwo anali ana a Rimoni wa banja la Beeroti wa fuko la Benjamini Beeroti. Iwo ankatengedwa ngati mbali imodzi ya Benjamini,
Njalo indodana kaSawuli yayilamadoda amabili ayeyizinduna zamaviyo; ibizo lenye lalinguBahana, lebizo lenye linguRekabi, amadodana kaRimoni, umBherothi, wabantwana bakoBhenjamini. Ngoba iBherothi layo yayibalelwa koBhenjamini;
3 chifukwa anthu a ku Beeroti anathawira ku Gitaimu ndipo akhala ali kumeneko ngati alendo mpaka lero lino.
lamaBherothi abalekela eGithayimi, aba ngabahlali njengabezizwe khona kuze kube lamuhla.
4 (Yonatani mwana wa Sauli anali ndi mwana wamwamuna amene anali wolumala mapazi ake onse awiri. Iye anali ndi zaka zisanu pamene nkhani ya Sauli ndi Yonatani inamveka kuchokera ku Yezireeli. Amene amamulera anamunyamula ndi kuthawa naye, koma pamene amachita zinthu mofulumira mwanayo anagwa ndipo analumala. Dzina lake linali Mefiboseti).
UJonathani indodana kaSawuli wayelendodana eyayiyisilima enyaweni. Yayileminyaka emihlanu ekufikeni kombiko ngoSawuli loJonathani uvela eJizereyeli; lomlizane wayo wayithatha, wabaleka; kwasekusithi ekuphangiseni kwakhe ukubaleka, yawa yaba yisilima. Lebizo layo lalinguMefiboshethi.
5 Choncho Rekabu ndi Baana ana a Rimoni wa ku Beeroti ananyamuka kupita ku nyumba ya Isi-Boseti, ndipo anafika nthawi ya masana kukutentha pamene iye amapumula.
Lamadodana kaRimoni, umBherothi, uRekabi loBahana, ahamba, ekutshiseni kwelanga afika endlini kaIshiboshethi, owayelele embhedeni emini enkulu.
6 Iwo analowa mʼchipinda chamʼkati ngati kuti amakatenga tirigu, ndipo anamulasa mʼmimba. Kenaka Rekabu ndi mʼbale wake Baana anathawa.
Bona bangena endlini phakathi kungathi bathatha ingqoloyi, bamtshaya kubambo lwesihlanu; uRekabi loBahana umfowabo basebebaleka.
7 Iwo analowa mʼnyumbamo iye akugona pa bedi mʼchipinda chake. Atamulasa ndi kumupha, anadula mutu wake nʼkuwutenga, nayenda usiku wonse mʼnjira yopita ku Araba.
Ngoba bengena endlini, wayelele embhedeni wakhe endlini yakhe yokulala, bamtshaya, bambulala, bamquma ikhanda; bathatha ikhanda lakhe, bahamba ngendlela yamagceke ubusuku bonke.
8 Iwo anabweretsa mutu wa Isi-Boseti kwa Davide ku Hebroni ndipo anati kwa mfumu, “Nawu mutu wa Isiboseti mwana wa Sauli, mdani wanu, amene anafuna kukuphani. Lero lino Yehova wabwezera mbuye wanga mfumu adani anu, Sauli ndi ana ake.”
Basebelisa ikhanda likaIshiboshethi kuDavida eHebroni. Bathi enkosini: Khangela, ikhanda likaIshiboshethi indodana kaSawuli, isitha sakho ebesidinga impilo yakho; iNkosi inike impindiselo lamuhla enkosini yami, inkosi, kuSawuli lakuyo inzalo yakhe.
9 Davide anayankha Rekabu ndi mʼbale wake Baana, ana a Rimoni wa ku Beeroti kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene wandipulumutsa ku mavuto anga onse,
Kodwa uDavida wabaphendula uRekabi loBahana umfowabo, amadodana kaRimoni umBherothi, wathi kubo: Kuphila kukaJehova, ohlenge umphefumulo wami kuyo yonke inhlupheko,
10 pamene munthu wina anandiwuza kuti, ‘Sauli wafa’ ndipo ankaganiza kuti wabweretsa nkhani yabwino, ine ndinamugwira ndi kumupha ku Zikilagi. Iyi inali mphotho imene ndinapereka kwa iyeyo chifukwa cha uthenga wake!
lapho owangibikelayo esithi: Khangela, uSawuli ufile; njalo enjengomthwali wendaba ezinhle emehlweni akhe, ngamxhakalaza, ngambulala eZikilagi, kulokuthi ngimvuzele indaba ezinhle.
11 Nanji pamene anthu oyipa apha munthu wosalakwa ali mʼnyumba mwake ndiponso pa bedi lake! Kodi ine ndingaleke kukulangani ndi kukuchotsani pa dziko lapansi pano?”
Pho kangakanani, lapho abantu ababi bebulele umuntu olungileyo endlini yakhe esembhedeni wakhe; ngakho-ke angiyikubiza yini igazi lakhe esandleni senu, ngilisuse emhlabeni?
12 Kotero Davide analamulira ankhondo ake, ndipo anawapha. Iwo anawadula manja ndi mapazi ndi kupachika matupi awo pa dziwe la ku Hebroni. Koma anatenga mutu wa Isi-Boseti nawuyika mʼmanda a Abineri ku Hebroni.
UDavida waselaya amajaha, ababulala, aquma izandla zabo lenyawo zabo, abaphanyeka echibini leHebroni. Kodwa athatha ikhanda likaIshiboshethi, alingcwaba engcwabeni likaAbhineri eHebroni.

< 2 Samueli 4 >