< 2 Samueli 4 >
1 Isiboseti mwana wa Sauli atamva kuti Abineri waphedwa ku Hebroni, anataya mtima ndipo Aisraeli onse anachita mantha kwambiri.
Der Sauls Søn hørte, at Abner var død i Hebron, da sank hans Hænder, og al Israel forfærdedes.
2 Koma Isiboseti anali ndi anthu akuluakulu awiri amene ankatsogolera magulu a ankhondo. Mmodzi mwa iwo dzina lake linali Baana ndipo mnzakeyo anali Rekabu. Iwo anali ana a Rimoni wa banja la Beeroti wa fuko la Benjamini Beeroti. Iwo ankatengedwa ngati mbali imodzi ya Benjamini,
Og Sauls Søn havde to Mænd, som vare Høvedsmænd for Tropperne, den enes Navn var Baena og den andens Navn Rekab, Beerothiteren Rimmons Sønner, af Benjamins Børn; thi Beeroth blev ogsaa regnet iblandt Benjamin.
3 chifukwa anthu a ku Beeroti anathawira ku Gitaimu ndipo akhala ali kumeneko ngati alendo mpaka lero lino.
Og Beerothiterne vare flygtede til Gitthajim og vare der som fremmede indtil denne Dag.
4 (Yonatani mwana wa Sauli anali ndi mwana wamwamuna amene anali wolumala mapazi ake onse awiri. Iye anali ndi zaka zisanu pamene nkhani ya Sauli ndi Yonatani inamveka kuchokera ku Yezireeli. Amene amamulera anamunyamula ndi kuthawa naye, koma pamene amachita zinthu mofulumira mwanayo anagwa ndipo analumala. Dzina lake linali Mefiboseti).
Og Jonathan, Sauls Søn, havde en Søn, som var lam paa begge Ben; han var fem Aar gammel, da Rygtet om Saul og Jonathan kom fra Jisreel, og hans Fostermoder tog ham og flyede, og det skete, der hun hastede med at fly, da faldt han og blev lam, og hans Navn var Mefiboseth.
5 Choncho Rekabu ndi Baana ana a Rimoni wa ku Beeroti ananyamuka kupita ku nyumba ya Isi-Boseti, ndipo anafika nthawi ya masana kukutentha pamene iye amapumula.
Saa gik Beerothiteren Rimmons Sønner, Rekab og Baena, og kom, der Dagen var hed, til Isboseths Hus; men han laa paa Sengen om Middagen.
6 Iwo analowa mʼchipinda chamʼkati ngati kuti amakatenga tirigu, ndipo anamulasa mʼmimba. Kenaka Rekabu ndi mʼbale wake Baana anathawa.
Og de kom ind i Huset, som om de vilde hente Hvede, og stak ham i Underlivet, og Rekab og Baena, hans Broder, undkom.
7 Iwo analowa mʼnyumbamo iye akugona pa bedi mʼchipinda chake. Atamulasa ndi kumupha, anadula mutu wake nʼkuwutenga, nayenda usiku wonse mʼnjira yopita ku Araba.
Thi de vare komne i Huset, der han laa paa sin Seng i sit Sovekammer, og de sloge ham og dræbte ham og borttoge hans Hoved, og de toge hans Hoved og gik bort ad Vejen over den slette Mark den ganske Nat.
8 Iwo anabweretsa mutu wa Isi-Boseti kwa Davide ku Hebroni ndipo anati kwa mfumu, “Nawu mutu wa Isiboseti mwana wa Sauli, mdani wanu, amene anafuna kukuphani. Lero lino Yehova wabwezera mbuye wanga mfumu adani anu, Sauli ndi ana ake.”
Og de førte Isboseths Hoved til David i Hebron, og de sagde til Kongen: Se, her er Hovedet af Isboseth, en Søn af din Fjende Saul, som søgte efter dit Liv; saa har Herren paa denne Dag givet min Herre, Kongen, Hævn over Saul og over hans Sæd.
9 Davide anayankha Rekabu ndi mʼbale wake Baana, ana a Rimoni wa ku Beeroti kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene wandipulumutsa ku mavuto anga onse,
Da svarede David Rekab og hans Broder Baena, Beerothiteren Rimmons Sønner, og sagde til dem: Saa vist som Herren lever, som har forløst min Sjæl af al Angest,
10 pamene munthu wina anandiwuza kuti, ‘Sauli wafa’ ndipo ankaganiza kuti wabweretsa nkhani yabwino, ine ndinamugwira ndi kumupha ku Zikilagi. Iyi inali mphotho imene ndinapereka kwa iyeyo chifukwa cha uthenga wake!
da en forkyndte mig og sagde: Se, Saul er død, og han var i sine egne Øjne som den, der bringer et godt Budskab, da greb jeg ham og ihjelslog ham i Ziklag, ham, som jeg skulde have givet Løn for hans Budskab;
11 Nanji pamene anthu oyipa apha munthu wosalakwa ali mʼnyumba mwake ndiponso pa bedi lake! Kodi ine ndingaleke kukulangani ndi kukuchotsani pa dziko lapansi pano?”
meget mere disse ugudelige Mænd, som have ihjelslaget en retfærdig Mand i hans Hus paa hans Seng; og nu, skulde jeg ikke udkræve hans Blod af eders Haand og udrydde eder af Jorden?
12 Kotero Davide analamulira ankhondo ake, ndipo anawapha. Iwo anawadula manja ndi mapazi ndi kupachika matupi awo pa dziwe la ku Hebroni. Koma anatenga mutu wa Isi-Boseti nawuyika mʼmanda a Abineri ku Hebroni.
Og David bød de unge Karle, og de sloge dem ihjel og afhuggede deres Hænder og deres Fødder og hængte dem over Fiskedammen i Hebron, men de toge Isboseths Hoved og begrove det i Abners Grav i Hebron.