< 2 Samueli 3 >
1 Nkhondo ya pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide inachitika nthawi yayitali. Mphamvu za Davide zinkakulirakulirabe, pamene banja la Sauli mphamvu zake zimapita zicheperachepera.
Şaulneyiy Davudne nasılen səvxı'y xıliyda ts'ıts'exhe. Vaxt apk'ıniylette, Davudne nasılena guc hexxooxhe, Şaulnemee nasılena k'ıl qooxhe vuxha.
2 Ana aamuna a Davide amene anabadwira ku Hebroni anali awa: Woyamba anali Amnoni, amayi ake anali Ahinoamu wa ku Yezireeli.
Xevronee Davudus dixbı vooxhe. Ts'erriyna dix İzre'elyğançene Axinoamee uxuna Amnon ıxha.
3 Mwana wachiwiri anali Kileabu, amayi ake anali Abigayeli mkazi wamasiye wa Nabala wa ku Karimeli. Wachitatu anali Abisalomu, amayi ake anali Maaka mwana wa Talimai mfumu ya Gesuri;
Q'ör'esda Karmelyğançene Navalne sip'ıree Avigailee uxuna Kilav ıxha. Xhebır'esda Geşurne paççahne Talmayne yişşee Maakayee uxuna Avşalom ıxha.
4 wachinayi anali Adoniya, amayi ake anali Hagiti; wachisanu, Sefatiya amayi ake anali Abitali;
Yoq'ur'esda Haggitee uxuna Adoniya, xhor'esda Avitalee uxuna Şefatya,
5 ndipo wachisanu ndi chimodzi anali Itireamu, amayi ake anali Egila, mkazi wa Davide. Ana awa a Davide anabadwira ku Hebroni.
yixhır'esdar Davudne xhunaşşee Eglayee uxuna İtream ıxha. Davudus man gırgınbı dixbı Xevronee vuxha.
6 Pamene kunali nkhondo pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide, Abineri anayamba kudzipatsa yekha mphamvu pakati pa banja la Sauli.
Şaulnayiy Davudna nasıl siviyxəmee, Avneree Şaulne sural guc saa'a vuxha.
7 Sauli anali ndi mzikazi dzina lake Rizipa mwana wa Ayiwa. Ndipo Isiboseti anati kwa Abineri, “Nʼchifukwa chiyani unagona ndi mzikazi wa abambo anga?”
Şauluqa Ayyayna yiş Ritspa donana caariye yixha. İşboşetee Avnerık'le eyhen: – Nya'a ğu, yizde dekkıne caariyeyka g'ılexha?
8 Abineri anakwiya kwambiri chifukwa cha zimene Isi-Boseti ananena ndipo anamuyankha kuti “Kodi ukuyesa ndine mutu wagalu umene ali mbali ya Ayuda? Lero lino ndine wokhulupirika ku nyumba ya abambo ako, Sauli ndi banja lake ndi anzake. Ine sindinakupereke kwa Davide, koma tsopano ukundinena pa cholakwa chimene ndachita pa mkazi uyu!
İşboşetne mane cuvabıke Avnerıs geeb qəl vuxha, eyhen: – Nya'a zı vas, Yahudaabışin sura aqqına xvaana vuk'ulyne vob? Zı g'iyna yiğıniy yiğne dekkıne Şaulne nasılen, mang'une hambazaaşin sura aqqı. Zı ğu Davudne xılyaqa quvu deş. Ğu həşde mane zəiyfal-alla yizde gardanaqa bınah giviyxhe!
9 Mulungu andilange ine Abineri, andilange kwambiri, ngati sindichitira Davide zimene Yehova anamulonjeza iye mwa lumbiro.
Zı Davudus, Rəbbee mang'us k'ın g'assırıyn hide'eene, hasre Allahee Avnerne vuk'lelqa yiğbı alle'ecen!
10 Ndidzachotsa ufumu ku nyumba ya Sauli ndi kukhazikitsa ufumu wa Davide pa Aisraeli onse ndi Yuda kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba.”
Zı paççahiyvalla Şaulne nasılıke g'avşu, Davudusqa qevles. Mana İzrailynayiy Yahudeyayna, Danile Beer-Şevalqamee, paççah ixhes.
11 Isiboseti sanayerekezenso kunena mawu ena kwa Abineri, chifukwa ankamuopa.
İşboşetık'le man eyhenbı g'ayxhımee, mana Avnerıle qəyq'ən ıxhayke, mang'us alidghıniycad qeles dəxə axva.
12 Kenaka Abineri anatuma amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Kodi dzikoli ndi la yani? Uchite mgwirizano ndi ine ndipo ndidzakuthandiza kuti Aisraeli onse azikutsatira.”
Qiyğa Avneree, Davudusqa cun insanar g'axuvu, eyhen: – İn ciga şavunne vod? Qora, zınayiy ğu cuvab g'ats'ak'vanas. Qiyğa gırgınacab İzrail yiğne suralqa ts'ıts'aa'as zı vas kumag ha'asın.
13 Davide anati, “Chabwino. Ine ndichita mgwirizano ndi iwe. Koma ndikukupempha chinthu chimodzi: Usabwere pamaso panga pokhapokha utabweretsa Mikala mwana wamkazi wa Sauli, ukamabwera kudzandiona.”
Davudee eyhen: – Geed yugda, zı vaka cuvab g'ats'ak'vanasın. Saccu ğu zasqa ı'qqəmee, vakasana Şaulna yiş Mikal ayre. Mana dena zasqa ımmayle.
14 Ndipo Davide anatuma amithenga kwa Isi-Boseti mwana wa Sauli, kumulamula kuti, “Patse mkazi wanga Mikala, amene ndinamukwatira ndi makungu 100 a msonga za mavalo a Afilisti.”
Davudee, İşboşetısqa Şaulne dixesqa cun insanar g'axuvu, eyhen: – Zı vəş sunnat hıdi'ına Filiştinğançena gik'ul-alla zas Şaulee hiyvuna yizda xhunaşşe Mikal zasqa seek'al hee'e.
15 Kotero Isi-Boseti analamulira ndipo anakamutenga kwa mwamuna wake Palitieli mwana wa Laisi.
İşboşetee, insan g'axuvu, zəiyfa adamiysse Layişne dixesse Paltielsee g'ayşes ileeka.
16 Koma mwamuna wake anapita naye akulira pambuyo pake njira yonse mpaka ku Bahurimu. Kenaka Abineri anati kwa iye, “Bwerera kwanu!” Ndipo anabwerera kwawo.
Məng'ı'na adamiy geşşe-geşşe Baxurimqamee xhunaşşeyqa qihna ayk'an. Maa'ad Avneree mang'uk'le eyhen: – Yı'q'əlqa sak'le. Manar siyk'alna.
17 Abineri anakambirana ndi akuluakulu a Israeli ndipo anati, “Kwa kanthawi mwakhala mukufuna kulonga Davide kuti akhale mfumu yanu.
Avner İzrailyne ağsaqqalaaşika yuşanxha, eyhen: – Şos mısa ıkkannaniy vor, Davuduke şos paççah ha'as!
18 Tsopano chitani zimenezo! Pakuti Yehova analonjeza Davide kuti, ‘Kudzera mwa mtumiki wanga Davide ndidzapulumutsa anthu anga Aisraeli mʼdzanja la Afilisti ndi kuwachotsa mʼmanja mwa adani awo.’”
Həşde vuşde yik'eençe ı'lğəən he'e! Rəbbee Davuduk'le dişdiy uvhu: «Zı Yizde nukarne Davudne xıleka, İzrail Filiştinaaşdeyiy gırgıne duşmanaaşine xılençe g'attivxhan haa'as».
19 Abineri anayankhulanso nawo yekha anthu a fuko la Benjamini. Kenaka anapita ku Hebroni kukamuwuza Davide zonse zimene Aisraeli ndi fuko lonse la Benjamini amafuna kuchita.
Avneree man, hark'ın, Benyaminaaşik'led eyhen. Qiyğa İzrailyneyiy Benyaminaaşde yik'eençe ılğəən Davudus yuşan ha'asva, mana Xevronqa hayk'an.
20 Abineri, amene anali ndi anthu makumi awiri, atafika kwa Davide ku Hebroni, Davide anamukonzera phwando pamodzi ndi anthu ake.
Xevroneeqa, Avnerıka sacigee Davudusqa g'ayre insan arayle. Davudee, Avnerısiy cune insanaaşis otxhun-ulyodğiy hele.
21 Ndipo Abineri anawuza Davide kuti, “Loleni kuti ndipite msanga kukasonkhanitsa Aisraeli onse kuti abwere kwa inu kuno, mbuye wanga mfumu, kuti adzachite nanu pangano, ndipo kuti muzilamulira kulikonse kumene mtima wanu ufuna.” Kotero Davide analola Abineri kuti apite, ndipo anapita mwamtendere.
Avneree Davuduk'le eyhen: – Hasre zı həşde hark'ın, gırgına İzrail yizde xərıng'usqa, paççahısqa, saa'as. Ğunar manbışika cuvab g'ats'ak'vne. Qiyğab vas nişşisiy vukkan, xəbvalla hee'e. Məxüd ıxha Davudee Avner vuççud hidi'ı g'ekkana.
22 Nthawi yomweyo ankhondo a Davide ndi Yowabu anafika kuchokera kumene anakathira nkhondo ndipo anabweretsa katundu wambiri wolanda ku nkhondo. Koma Abineri sanalinso ndi Davide ku Hebroni, chifukwa Davide anamulola kuti apite, ndipo anapita mu mtendere.
Mane gahıl Yoav, Davudne insanaaşika dəv'eençe sark'ıl eyxhe. Manbışe mebınbışike g'ayşuyn geed kar adayle. Mane gahıl Avner, Davudusse Xevronğançe ark'ın eyxhe. Davudee, Avner vuççud hidi'ı, g'aykkı ıxha.
23 Yowabu ndi asilikali onse amene anali naye atafika, anawuzidwa kuti Abineri mwana wa Neri anabwera kwa mfumu ndipo kuti mfumu yamulola kuti apite ndi kuti wapita ndi mtendere.
Yoav, gırgıne g'oşunuka sark'ıling'a, mang'uk'le eyhen: – Nerna dix Avneriy arı. Paççahee mang'uk vuççud hidi'ı, g'aykkına.
24 Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Mwachita chiyani? Taonani, Abineri anabwera kwa inu. Nʼchifukwa chiyani mwamulola kuti apite? Tsopanotu wapitadi!
Yoav, paççahne k'anyaqa qarı, eyhen: – Ğu hı'iyn kar hucoone? Yiğne k'anyaqa Avnerniy'e arı? Ğu nya'a mana g'aykkı? Həşde mana ark'ınna.
25 Inu mukumudziwa bwino Abineri mwana wa Neri. Iye anabwera kudzakunamizani ndi kudzaona mayendedwe anu ndiponso kudzaona zonse zimene mukuchita.”
Vak'lecar Nerna dix Avner ats'ana. Mang'vee vas horbı ha'asva, yiğın hark'ın-qaraylen cigayiy ğu g'ecen işbı ats'axhxhesvacar arı ıxha.
26 Kenaka Yowabu anachoka pamaso pa Davide ndipo anatumiza amithenga kutsatira Abineri, ndipo anabwera naye kuchokera ku chitsime cha Sira. Koma Davide sanadziwe zimenezi.
Yoav Davudusse qığeç'umee, mang'vee Avnerıqa qihna cun insanar g'uxoole. Manbışer Avner Sira eyhene kahrızısse yı'q'əlqa sak'al ha'a. Davuduk'le man ats'acad eyxhe deş.
27 Tsono Abineri atabwerera ku Hebroni, Yowabu anamutengera pambali ku chipata, kukhala ngati akufuna kuyankhula naye mwamseri. Ndipo kumeneko pobwezera imfa ya mʼbale wake Asaheli, Yowabu analasa iyeyo mʼmimba, ndipo anafa.
Avner Xevronqa sak'ımee, Yoavee cona q'öyrecab, yuşan haa'asın xhinne, mana şaharne akkabışiyle aqa akkyayhe. Qiyğad cune çocul Asahelil-alla, mang'une vuxhnes g'ılıncıqa ı'xı', gek'ana.
28 Patapita nthawi, Davide atamva zimenezi anati, “Ine ndi ufumu wanga tidzakhala osalakwa pamaso pa Yehova pa imfa ya Abineri mwana wa Neri.
Davuduk'le, man ats'axhxhamee, eyhen: – Rəbbine ögil Nerne duxayne Avnerne ebal-alla, mısacab zaliy yizde ölkal bınah aaxvas deş.
29 Mlandu umenewu ukhala pa Yowabu ndi banja lonse la abambo ake! Mʼbanja la Yowabu musadzasowe munthu wodwala matenda a chizonono kapena khate, kapena wolumala woyendera ndodo kapena wophedwa ndi lupanga, kapena wosowa chakudya.”
Havaasre mana bınah Yoavılqayiy mang'une xizanılqa vuxhecen. Hasre Yoavne nasılee maşika gyatsts'ıyn ı'xnabınana insan deşda, əsaka iykarna insan deşda, g'ılıncıke qek'ana insan deşda, mıssınçika qek'ana insan deşda gah mooxhecen.
30 (Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anapha Abineri chifukwa iye anapha mʼbale wawo Asaheli ku nkhondo ku Gibiyoni).
Yoaveeyiy cune çocee Avişayee Avner gek'ana. Manbışe mana cona çoc Asahel Giveonee əlyhəəne dəv'ee gik'uynçil-alla gek'a.
31 Ndipo Davide anati kwa Yowabu ndi anthu onse amene anali nawo, “Ngʼambani zovala zanu ndipo muvale ziguduli, muyende mukulira patsogolo pa Abineri.” Mfumu Davide mwini anayenda motsatira chitandacho.
Qiyğa Davudee Yoavık'leyiy cune k'anene insanaaşik'le eyhen: – Tanalinbı qıt'axxı, palanbı ale'e, Avnernemee gyaaşe. Avner qıkkek'ane mıghırıqa qihna vuc paççah Davud ayk'an.
32 Iwo anamuyika Abineri mʼmanda ku Hebroni ndipo mfumu inalira mokweza pa manda a Abineri. Ndipo anthu onse analiranso.
Avner Xevronee k'eyxha. Paççah mang'une nyuq'vnel oo axtıra geşşena. Mang'uka sacigee milletıd geşşen.
33 Mfumu inayimba nyimbo iyi ya maliro a Abineri: “Abineri nʼkufa motere monga mmene chimafera chitsiru.
Paççah Davud Avnerne nyuq'vnel oo inva eyhe-eyhe geşşu: Avner məxür, g'eliqqa huvu, gik'as dexheyiy.
34 Manja ako anali osamanga, mapazi ako anali osakulungidwa. Iwe wafa monga mmene amafera anthu pamaso pa anthu oyipa.” Ndipo anthu onse analiranso kulirira Abineri.
Yiğın xıleppı ayt'ıl ıxha deş, G'elybışisıb zincır üvxü vuxha deş. Ğu sixnareeşine ögil qukkyoyk'alan xhinne qukkyork'ul. Manva uvhumee, millet meed Avnernemee geşşen.
35 Kenaka onse anabwera kwa Davide kumuwumiriza kuti adye kusanade. Koma Davide analumbira kuti, “Mulungu andilange ine, andilange kwambiri, ngati ndilawe buledi kapena chilichonse dzuwa lisanalowe!”
Qiyğa manbışin gırgınbı abı, Davudee, exha qixhesse, kar oxhnecenva mana ittunçil aqqaqqa ıxha. Davudeeme, k'ın g'assır, eyhen: – Verığ k'yooçesse, yizde ghalek gıney, medın kar set'veene, havaasre Allahee zalqa ver ablee'ecen!
36 Anthu onse anadziwa zimenezi ndipo zinawakondweretsa ndithu. Zonse zimene mfumu inachita zinawakondweretsa.
Milletık'le paççahee ha'an g'acu, man gırgın manbışde yik'eençe eyxhe. Paççahee ha'an gırgıncad milletıs ıkkiykanan.
37 Kotero tsiku limeneli anthu onse ndi Aisraeli onse anadziwa kuti sikunali kufuna kwa mfumu kuti Abineri mwana wa Neri aphedwe.
Mane yiğıl gırgıne milletık'leyiy gırgıne İzrailik'lecad ats'axhxhen, Nerna dix Avner paççahee gidek'u ıxhay.
38 Ndipo mfumu inati kwa ankhondo ake, “Kodi inu simukudziwa kuti lero mu Israeli mwagwa kalonga ndi munthu wamkulu?
Paççahee cune insanaaşik'le eyhen: – G'iyna İzrailee xərna, qıvaats'ına insan qik'uva ats'a dişde?
39 Ndipo lero, ngakhale ine ndine mfumu yodzozedwa, ndilibe mphamvu ndipo ana awa a Zeruya ndi amphamvu kwa ine. Yehova abwezere woyipa molingana ndi zoyipa zake!”
G'iyna zı g'əyxı'na paççahır ixheene, zaqa guc k'ılyba vob. Tseruyayn dixbı, Yoaviy Avişay, zale nimee vuxhee gucuka vob. Havaasre Rəbbee pisvalla haa'ang'us, haa'ane pisvallays sik'ı helecen!