< 2 Samueli 3 >

1 Nkhondo ya pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide inachitika nthawi yayitali. Mphamvu za Davide zinkakulirakulirabe, pamene banja la Sauli mphamvu zake zimapita zicheperachepera.
И дуго беше рат између дома Сауловог и дома Давидовог; Али Давид све већма јачаше, а дом Саулов постајаше све слабији.
2 Ana aamuna a Davide amene anabadwira ku Hebroni anali awa: Woyamba anali Amnoni, amayi ake anali Ahinoamu wa ku Yezireeli.
И Давиду се родише синови у Хеврону: Првенац му беше Амнон од Ахиноаме Језраељанке;
3 Mwana wachiwiri anali Kileabu, amayi ake anali Abigayeli mkazi wamasiye wa Nabala wa ku Karimeli. Wachitatu anali Abisalomu, amayi ake anali Maaka mwana wa Talimai mfumu ya Gesuri;
Други беше Хилеав од Авигеје жене Навала Кармилца; трећи Авесалом син Махе кћери Талмаја цара гесурског;
4 wachinayi anali Adoniya, amayi ake anali Hagiti; wachisanu, Sefatiya amayi ake anali Abitali;
Четврти Адонија син Агитин; и пети Сефатија син Авиталин;
5 ndipo wachisanu ndi chimodzi anali Itireamu, amayi ake anali Egila, mkazi wa Davide. Ana awa a Davide anabadwira ku Hebroni.
И шести Итрам од Егле жене Давидове. Ти се родише Давиду у Хеврону.
6 Pamene kunali nkhondo pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide, Abineri anayamba kudzipatsa yekha mphamvu pakati pa banja la Sauli.
И док беше рат између дома Сауловог и дома Давидовог, Авенир брањаше дом Саулов.
7 Sauli anali ndi mzikazi dzina lake Rizipa mwana wa Ayiwa. Ndipo Isiboseti anati kwa Abineri, “Nʼchifukwa chiyani unagona ndi mzikazi wa abambo anga?”
А Саул имаше иночу по имену Ресфу, кћер Ајину; и Исвостеј рече Авениру: Зашто си спавао код иноче оца мог?
8 Abineri anakwiya kwambiri chifukwa cha zimene Isi-Boseti ananena ndipo anamuyankha kuti “Kodi ukuyesa ndine mutu wagalu umene ali mbali ya Ayuda? Lero lino ndine wokhulupirika ku nyumba ya abambo ako, Sauli ndi banja lake ndi anzake. Ine sindinakupereke kwa Davide, koma tsopano ukundinena pa cholakwa chimene ndachita pa mkazi uyu!
И Авенир се разгневи на речи Исвостејеве и рече: Јесам ли ја пасја глава, који сада чиним на Јуди милост дому Саула оца твог и браћи његовој и пријатељима његовим, и нисам те пустио у руке Давидове, те данас тражиш на мени зло ради те жене?
9 Mulungu andilange ine Abineri, andilange kwambiri, ngati sindichitira Davide zimene Yehova anamulonjeza iye mwa lumbiro.
Тако нека учини Бог Авениру, и тако нека дода, ако не учиним Давиду како му се Господ заклео,
10 Ndidzachotsa ufumu ku nyumba ya Sauli ndi kukhazikitsa ufumu wa Davide pa Aisraeli onse ndi Yuda kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba.”
Да се пренесе ово царство од дома Сауловог, и да се утврди престо Давидов над Израиљем и над Јудом, од Дана до Вирсавеје.
11 Isiboseti sanayerekezenso kunena mawu ena kwa Abineri, chifukwa ankamuopa.
И он не може више ништа одговорити Авениру, јер га се бојаше.
12 Kenaka Abineri anatuma amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Kodi dzikoli ndi la yani? Uchite mgwirizano ndi ine ndipo ndidzakuthandiza kuti Aisraeli onse azikutsatira.”
И Авенир посла посланике к Давиду од себе и поручи: Чија је земља? И поручи му: Учини веру са мном, и ево рука ће моја бити с тобом, да обратим к теби свега Израиља.
13 Davide anati, “Chabwino. Ine ndichita mgwirizano ndi iwe. Koma ndikukupempha chinthu chimodzi: Usabwere pamaso panga pokhapokha utabweretsa Mikala mwana wamkazi wa Sauli, ukamabwera kudzandiona.”
А он одговори: Добро; ја ћу учинити веру с тобом; али једно иштем од тебе, и то: да не видиш лице моје ако ми прво не доведеш Михалу, кћер Саулову, кад дођеш да видиш лице моје.
14 Ndipo Davide anatuma amithenga kwa Isi-Boseti mwana wa Sauli, kumulamula kuti, “Patse mkazi wanga Mikala, amene ndinamukwatira ndi makungu 100 a msonga za mavalo a Afilisti.”
И посла Давид посланике к Исвостеју, сину Сауловом, и поручи му: Дај ми жену моју Михалу, коју испросих за сто окрајака филистејских.
15 Kotero Isi-Boseti analamulira ndipo anakamutenga kwa mwamuna wake Palitieli mwana wa Laisi.
И Исвостеј посла те је узе од мужа, од Фалтила, сина Лаисовог.
16 Koma mwamuna wake anapita naye akulira pambuyo pake njira yonse mpaka ku Bahurimu. Kenaka Abineri anati kwa iye, “Bwerera kwanu!” Ndipo anabwerera kwawo.
А муж њен пође с њом, и једнако плакаше за њом до Ваурима. Тада му рече Авенир: Иди, врати се натраг. И он се врати.
17 Abineri anakambirana ndi akuluakulu a Israeli ndipo anati, “Kwa kanthawi mwakhala mukufuna kulonga Davide kuti akhale mfumu yanu.
Потом Авенир говори старешинама израиљским, и рече им: Пре тражисте Давида да буде цар над вама.
18 Tsopano chitani zimenezo! Pakuti Yehova analonjeza Davide kuti, ‘Kudzera mwa mtumiki wanga Davide ndidzapulumutsa anthu anga Aisraeli mʼdzanja la Afilisti ndi kuwachotsa mʼmanja mwa adani awo.’”
Ето сада учините; јер је Господ рекао за Давида говорећи: Преко Давида слуге свог избавићу народ свој Израиља из руку филистејских и из руку свих непријатеља њихових.
19 Abineri anayankhulanso nawo yekha anthu a fuko la Benjamini. Kenaka anapita ku Hebroni kukamuwuza Davide zonse zimene Aisraeli ndi fuko lonse la Benjamini amafuna kuchita.
Тако говори Авенир и синовима Венијаминовим. Потом отиде Авенир и у Хеврон да каже Давиду све што за добро нађе Израиљ и сав дом Венијаминов.
20 Abineri, amene anali ndi anthu makumi awiri, atafika kwa Davide ku Hebroni, Davide anamukonzera phwando pamodzi ndi anthu ake.
И кад дође Авенир к Давиду у Хеврон и с њим двадесет људи, учини Давид гозбу Авениру и људима који беху с њим.
21 Ndipo Abineri anawuza Davide kuti, “Loleni kuti ndipite msanga kukasonkhanitsa Aisraeli onse kuti abwere kwa inu kuno, mbuye wanga mfumu, kuti adzachite nanu pangano, ndipo kuti muzilamulira kulikonse kumene mtima wanu ufuna.” Kotero Davide analola Abineri kuti apite, ndipo anapita mwamtendere.
И рече Авенир Давиду: Да устанем и идем да скупим к цару господару свом сав народ Израиљев да учине веру с тобом, па да царујеш како ти душа жели. И Давид отпусти Авенира да иде с миром.
22 Nthawi yomweyo ankhondo a Davide ndi Yowabu anafika kuchokera kumene anakathira nkhondo ndipo anabweretsa katundu wambiri wolanda ku nkhondo. Koma Abineri sanalinso ndi Davide ku Hebroni, chifukwa Davide anamulola kuti apite, ndipo anapita mu mtendere.
А гле, слуге Давидове враћаху се с Јоавом из боја, и тераху са собом велик плен; а Авенир већ не беше код Давида у Хеврону, јер га отпусти, те отиде с миром.
23 Yowabu ndi asilikali onse amene anali naye atafika, anawuzidwa kuti Abineri mwana wa Neri anabwera kwa mfumu ndipo kuti mfumu yamulola kuti apite ndi kuti wapita ndi mtendere.
Јоав дакле и сва војска што беше с њим, дођоше онамо; и јавише Јоаву говорећи: Авенир син Ниров долазио је к цару, и он га отпусти те отиде с миром.
24 Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Mwachita chiyani? Taonani, Abineri anabwera kwa inu. Nʼchifukwa chiyani mwamulola kuti apite? Tsopanotu wapitadi!
И Јоав отиде к цару и рече: Шта учини? Гле, Авенир је долазио к теби; зашто га пусти те отиде?
25 Inu mukumudziwa bwino Abineri mwana wa Neri. Iye anabwera kudzakunamizani ndi kudzaona mayendedwe anu ndiponso kudzaona zonse zimene mukuchita.”
Познајеш ли Авенира сина Нировог? Долазио је да те превари, да види куда ходиш и да дозна све што радиш.
26 Kenaka Yowabu anachoka pamaso pa Davide ndipo anatumiza amithenga kutsatira Abineri, ndipo anabwera naye kuchokera ku chitsime cha Sira. Koma Davide sanadziwe zimenezi.
Потом отишавши Јоав од Давида посла људе за Авениром да га врате од студенца Сире, а Давид не знаше за то.
27 Tsono Abineri atabwerera ku Hebroni, Yowabu anamutengera pambali ku chipata, kukhala ngati akufuna kuyankhula naye mwamseri. Ndipo kumeneko pobwezera imfa ya mʼbale wake Asaheli, Yowabu analasa iyeyo mʼmimba, ndipo anafa.
И кад се врати Авенир у Хеврон, одведе га Јоав на страну под врата као да говори с њим насамо; онде га удари под пето ребро, те умре за крв Асаила брата његовог.
28 Patapita nthawi, Davide atamva zimenezi anati, “Ine ndi ufumu wanga tidzakhala osalakwa pamaso pa Yehova pa imfa ya Abineri mwana wa Neri.
А кад Давид после то чу, рече: Ја нисам крив ни царство моје пред Господом довека за крв Авенира сина Нировог.
29 Mlandu umenewu ukhala pa Yowabu ndi banja lonse la abambo ake! Mʼbanja la Yowabu musadzasowe munthu wodwala matenda a chizonono kapena khate, kapena wolumala woyendera ndodo kapena wophedwa ndi lupanga, kapena wosowa chakudya.”
Нека падне на главу Јоавову и на сав дом оца његовог; и нека дом Јоавов не буде никад без човека болног од течења или губавог или који иде о штапу или који падне од мача или који нема хлеба.
30 (Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anapha Abineri chifukwa iye anapha mʼbale wawo Asaheli ku nkhondo ku Gibiyoni).
Тако Јоав и Ависај брат његов убише Авенира што он погуби Асаила брата њиховог код Гаваона у боју.
31 Ndipo Davide anati kwa Yowabu ndi anthu onse amene anali nawo, “Ngʼambani zovala zanu ndipo muvale ziguduli, muyende mukulira patsogolo pa Abineri.” Mfumu Davide mwini anayenda motsatira chitandacho.
И рече Давид Јоаву и свему народу који беше с њим: Раздерите хаљине своје и припашите кострет, и плачите за Авениром. И цар Давид иђаше за носилима.
32 Iwo anamuyika Abineri mʼmanda ku Hebroni ndipo mfumu inalira mokweza pa manda a Abineri. Ndipo anthu onse analiranso.
А кад погребоше Авенира у Хеврону, цар подиже глас свој и плака на гробу Авенировом; плака и сав народ.
33 Mfumu inayimba nyimbo iyi ya maliro a Abineri: “Abineri nʼkufa motere monga mmene chimafera chitsiru.
И наричући за Авениром рече: Умре ли Авенир како умире безумник?
34 Manja ako anali osamanga, mapazi ako anali osakulungidwa. Iwe wafa monga mmene amafera anthu pamaso pa anthu oyipa.” Ndipo anthu onse analiranso kulirira Abineri.
Руке твоје не бише везане, нити ноге твоје у оков оковане; пао си као што се пада од неваљалих људи. Тада још већма плака за њим сав народ.
35 Kenaka onse anabwera kwa Davide kumuwumiriza kuti adye kusanade. Koma Davide analumbira kuti, “Mulungu andilange ine, andilange kwambiri, ngati ndilawe buledi kapena chilichonse dzuwa lisanalowe!”
И дође сав народ нудећи Давида да једе шта, док још беше дан; али се Давид закле и рече: Бог нека ми учини тако, и тако нека дода, ако окусим хлеба или шта друго док не зађе сунце.
36 Anthu onse anadziwa zimenezi ndipo zinawakondweretsa ndithu. Zonse zimene mfumu inachita zinawakondweretsa.
И сав народ чу то, и би им по вољи; шта год чињаше цар, беше по вољи свему народу.
37 Kotero tsiku limeneli anthu onse ndi Aisraeli onse anadziwa kuti sikunali kufuna kwa mfumu kuti Abineri mwana wa Neri aphedwe.
И позна сав народ и сав Израиљ у онај дан да није било од цара што погибе Авенир син Ниров.
38 Ndipo mfumu inati kwa ankhondo ake, “Kodi inu simukudziwa kuti lero mu Israeli mwagwa kalonga ndi munthu wamkulu?
И цар рече слугама својим: Не знате ли да је војвода и то велики погинуо данас у Израиљу?
39 Ndipo lero, ngakhale ine ndine mfumu yodzozedwa, ndilibe mphamvu ndipo ana awa a Zeruya ndi amphamvu kwa ine. Yehova abwezere woyipa molingana ndi zoyipa zake!”
Али ја сам сада још слаб, ако и јесам помазани цар; а ови људи, синови Серујини, врло су ми силни. Нека Господ плати ономе који чини зло према злоћи његовој.

< 2 Samueli 3 >