< 2 Samueli 3 >

1 Nkhondo ya pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide inachitika nthawi yayitali. Mphamvu za Davide zinkakulirakulirabe, pamene banja la Sauli mphamvu zake zimapita zicheperachepera.
Il se fit donc une longue guerre entre la maison de Saül et la maison de David. David s’avançant, et toujours plus fort que lui-même, mais la maison de Saül décroissant de jour en jour.
2 Ana aamuna a Davide amene anabadwira ku Hebroni anali awa: Woyamba anali Amnoni, amayi ake anali Ahinoamu wa ku Yezireeli.
Et des fils naquirent à David à Hébron; et son premier-né fut Amnon, d’Achinoam la Jezraélite;
3 Mwana wachiwiri anali Kileabu, amayi ake anali Abigayeli mkazi wamasiye wa Nabala wa ku Karimeli. Wachitatu anali Abisalomu, amayi ake anali Maaka mwana wa Talimai mfumu ya Gesuri;
Et après lui Chéleab d’Abigaïl, femme de Nabal du Carmel; puis le troisième, Absalom, fils de Maacha, fille de Tholmaï, roi de Gessur;
4 wachinayi anali Adoniya, amayi ake anali Hagiti; wachisanu, Sefatiya amayi ake anali Abitali;
Ensuite le quatrième, Adonias, fils d’Haggith, et le cinquième, Saphathia, fils d’Abital;
5 ndipo wachisanu ndi chimodzi anali Itireamu, amayi ake anali Egila, mkazi wa Davide. Ana awa a Davide anabadwira ku Hebroni.
Et le sixième, Jéthraam d’Egla, femme de David; ceux-là naquirent à David à Hébron.
6 Pamene kunali nkhondo pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide, Abineri anayamba kudzipatsa yekha mphamvu pakati pa banja la Sauli.
Lors donc que la guerre était entre la maison de Saül et la maison de David, Abner, fils de Ner, gouvernait la maison de Saül.
7 Sauli anali ndi mzikazi dzina lake Rizipa mwana wa Ayiwa. Ndipo Isiboseti anati kwa Abineri, “Nʼchifukwa chiyani unagona ndi mzikazi wa abambo anga?”
Mais Saül avait eu une femme du second rang, du nom de Respha, fille d’Aïa. Et Isboseth dit à Abner:
8 Abineri anakwiya kwambiri chifukwa cha zimene Isi-Boseti ananena ndipo anamuyankha kuti “Kodi ukuyesa ndine mutu wagalu umene ali mbali ya Ayuda? Lero lino ndine wokhulupirika ku nyumba ya abambo ako, Sauli ndi banja lake ndi anzake. Ine sindinakupereke kwa Davide, koma tsopano ukundinena pa cholakwa chimene ndachita pa mkazi uyu!
Pourquoi t’es-tu approché de la femme du second rang de mon père? Abner, très irrité à cause des paroles d’Isboseth, répondit: Est-ce que je suis une tête de chien, moi l’adversaire de Juda aujourd’hui, qui ai fait miséricorde à la maison de Saül, ton père, à ses frères et à ses proches, et qui ne t’ai point livré aux mains de David, tandis que toi, tu as recherché aujourd’hui contre moi ce que tu aurais à reprendre au sujet de cette femme?
9 Mulungu andilange ine Abineri, andilange kwambiri, ngati sindichitira Davide zimene Yehova anamulonjeza iye mwa lumbiro.
Que Dieu fasse ceci à Abner, et qu’il lui ajoute cela, si je n’agis pas avec David, comme le Seigneur lui a juré,
10 Ndidzachotsa ufumu ku nyumba ya Sauli ndi kukhazikitsa ufumu wa Davide pa Aisraeli onse ndi Yuda kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba.”
Afin que le royaume soit transféré de la maison de Saül, et que le trône de David soit élevé sur Israël et sur Juda, depuis Dan jusqu’à Bersabée.
11 Isiboseti sanayerekezenso kunena mawu ena kwa Abineri, chifukwa ankamuopa.
Et il ne put rien répondre à Abner, parce qu’il le craignait.
12 Kenaka Abineri anatuma amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Kodi dzikoli ndi la yani? Uchite mgwirizano ndi ine ndipo ndidzakuthandiza kuti Aisraeli onse azikutsatira.”
Abner envoya donc des messagers à David de sa part, disant: À qui est la terre? et pour dire: Fais amitié avec moi, et ma main sera avec toi, et je ramènerai à toi tout Israël.
13 Davide anati, “Chabwino. Ine ndichita mgwirizano ndi iwe. Koma ndikukupempha chinthu chimodzi: Usabwere pamaso panga pokhapokha utabweretsa Mikala mwana wamkazi wa Sauli, ukamabwera kudzandiona.”
David répondit: Très bien; moi je ferai amitié avec toi, mais je demande de toi une seule chose, disant: Tu ne verras point ma face, avant que tu aies amené Michol, fille de Saül; car c’est ainsi que tu viendras et me verras.
14 Ndipo Davide anatuma amithenga kwa Isi-Boseti mwana wa Sauli, kumulamula kuti, “Patse mkazi wanga Mikala, amene ndinamukwatira ndi makungu 100 a msonga za mavalo a Afilisti.”
David ensuite envoya des messagers à Isboseth, fils de Saül, disant: Rends-moi ma femme Michol, que j’ai épousée pour cent prépuces de Philistins.
15 Kotero Isi-Boseti analamulira ndipo anakamutenga kwa mwamuna wake Palitieli mwana wa Laisi.
Isboseth donc envoya, et l’enleva à son mari, Phaltiel, fils de Laïs.
16 Koma mwamuna wake anapita naye akulira pambuyo pake njira yonse mpaka ku Bahurimu. Kenaka Abineri anati kwa iye, “Bwerera kwanu!” Ndipo anabwerera kwawo.
Et son mari la suivait, pleurant, jusqu’à Bahurim; et Abner lui dit: Va, et retourne-t’en. Et il s’en retourna.
17 Abineri anakambirana ndi akuluakulu a Israeli ndipo anati, “Kwa kanthawi mwakhala mukufuna kulonga Davide kuti akhale mfumu yanu.
Abner adressa aussi la parole aux anciens d’Israël, disant: Tant hier qu’avant-hier, vous cherchiez David, pour qu’il régnât sur vous.
18 Tsopano chitani zimenezo! Pakuti Yehova analonjeza Davide kuti, ‘Kudzera mwa mtumiki wanga Davide ndidzapulumutsa anthu anga Aisraeli mʼdzanja la Afilisti ndi kuwachotsa mʼmanja mwa adani awo.’”
Maintenant donc agissez, puisque le Seigneur a parlé à David, disant: C’est par la main de mon serviteur David que je sauverai mon peuple Israël de la main des Philistins, et devions ses ennemis.
19 Abineri anayankhulanso nawo yekha anthu a fuko la Benjamini. Kenaka anapita ku Hebroni kukamuwuza Davide zonse zimene Aisraeli ndi fuko lonse la Benjamini amafuna kuchita.
Abner parla aussi à la tribu de Benjamin. Et il s’en alla pour dire à David à Hébron, tout ce qui avait paru bon à Israël et à tout Benjamin.
20 Abineri, amene anali ndi anthu makumi awiri, atafika kwa Davide ku Hebroni, Davide anamukonzera phwando pamodzi ndi anthu ake.
Et il vint vers David à Hébron avec vingt hommes; et David fit à Abner, et à ses hommes qui étaient venus avec lui, un festin.
21 Ndipo Abineri anawuza Davide kuti, “Loleni kuti ndipite msanga kukasonkhanitsa Aisraeli onse kuti abwere kwa inu kuno, mbuye wanga mfumu, kuti adzachite nanu pangano, ndipo kuti muzilamulira kulikonse kumene mtima wanu ufuna.” Kotero Davide analola Abineri kuti apite, ndipo anapita mwamtendere.
Et Abner dit à David: Je me lèverai, afin que j’assemble près de vous, mon seigneur le roi, tout Israël, et que je fasse avec vous alliance, et que vous régniez sur tous, comme votre âme le désire. Lors donc que David eut reconduit Abner, et que celui-ci s’en fut allé en paix,
22 Nthawi yomweyo ankhondo a Davide ndi Yowabu anafika kuchokera kumene anakathira nkhondo ndipo anabweretsa katundu wambiri wolanda ku nkhondo. Koma Abineri sanalinso ndi Davide ku Hebroni, chifukwa Davide anamulola kuti apite, ndipo anapita mu mtendere.
Aussitôt les serviteurs de David et Joab vinrent, après avoir taillé en pièces des voleurs, et avec un très grand butin; mais Abner n’était pas avec David à Hébron, parce que déjà il l’avait quitté, et qu’il était parti en paix.
23 Yowabu ndi asilikali onse amene anali naye atafika, anawuzidwa kuti Abineri mwana wa Neri anabwera kwa mfumu ndipo kuti mfumu yamulola kuti apite ndi kuti wapita ndi mtendere.
Et Joab et toute l’armée qui était avec lui vinrent après; c’est pourquoi la nouvelle fut portée à Joab par des gens qui racontèrent: Abner, fils de Ner, est venu près du roi, et le roi l’a renvoyé, et il s’en est allé en paix.
24 Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Mwachita chiyani? Taonani, Abineri anabwera kwa inu. Nʼchifukwa chiyani mwamulola kuti apite? Tsopanotu wapitadi!
Et Joab entra chez le roi, et dit: Qu’avez-vous fait? Voilà qu’Abner est venu vers vous; pourquoi l’avez-vous renvoyé, et qu’il s’en est allé, et s’est retiré?
25 Inu mukumudziwa bwino Abineri mwana wa Neri. Iye anabwera kudzakunamizani ndi kudzaona mayendedwe anu ndiponso kudzaona zonse zimene mukuchita.”
Ignorez-vous qu’Abner, fils de Ner, n’est venu vers vous que pour vous tromper, et pour savoir votre sortie et votre entrée, et connaître tout ce que vous faites?
26 Kenaka Yowabu anachoka pamaso pa Davide ndipo anatumiza amithenga kutsatira Abineri, ndipo anabwera naye kuchokera ku chitsime cha Sira. Koma Davide sanadziwe zimenezi.
C’est pourquoi Joab, étant sorti d’avec David, envoya des messagers après Abner, et le fit revenir de la citerne de Sira, David l’ignorant.
27 Tsono Abineri atabwerera ku Hebroni, Yowabu anamutengera pambali ku chipata, kukhala ngati akufuna kuyankhula naye mwamseri. Ndipo kumeneko pobwezera imfa ya mʼbale wake Asaheli, Yowabu analasa iyeyo mʼmimba, ndipo anafa.
Et lorsqu’Abner fut retourné à Hébron, Joab l’amena à part au milieu de la porte, pour lui parler, en trahison, et là il le frappa dans l’aîne, et il le tua pour venger la mort d’Asaël, son frère.
28 Patapita nthawi, Davide atamva zimenezi anati, “Ine ndi ufumu wanga tidzakhala osalakwa pamaso pa Yehova pa imfa ya Abineri mwana wa Neri.
Lorsque David eut appris ce qui s’était passé, il dit: Je suis innocent, moi et mon royaume à jamais devant le Seigneur, du sang d’Abner, fils de Ner;
29 Mlandu umenewu ukhala pa Yowabu ndi banja lonse la abambo ake! Mʼbanja la Yowabu musadzasowe munthu wodwala matenda a chizonono kapena khate, kapena wolumala woyendera ndodo kapena wophedwa ndi lupanga, kapena wosowa chakudya.”
Mais qu’il retombe sur la tête de Joab et sur toute la maison de son père; et que ne manque point dans la maison de Joab quelqu’un ayant la gonorrhée, quelqu’un infecté de la lèpre, quelqu’un tenant le fuseau, quelqu’un tombant sous le glaive, et quelqu’un dépourvu de pain.
30 (Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anapha Abineri chifukwa iye anapha mʼbale wawo Asaheli ku nkhondo ku Gibiyoni).
Ainsi Joab et Abisaï, son frère, tuèrent Abner, parce qu’il avait tué Asaël, leur frère, à Gabaon, dans le combat.
31 Ndipo Davide anati kwa Yowabu ndi anthu onse amene anali nawo, “Ngʼambani zovala zanu ndipo muvale ziguduli, muyende mukulira patsogolo pa Abineri.” Mfumu Davide mwini anayenda motsatira chitandacho.
David donc dit à Joab et à tout le peuple qui était avec lui: Déchirez vos vêtements, ceignez-vous de sacs, et pleurez aux funérailles d’Abner: or, le roi David suivait le cercueil.
32 Iwo anamuyika Abineri mʼmanda ku Hebroni ndipo mfumu inalira mokweza pa manda a Abineri. Ndipo anthu onse analiranso.
Et lorsqu’on eut enseveli Abner à Hébron, David leva sa voix et pleura sur le tombeau d’Abner; et tout le peuple aussi pleura.
33 Mfumu inayimba nyimbo iyi ya maliro a Abineri: “Abineri nʼkufa motere monga mmene chimafera chitsiru.
Et le roi se lamentant, et pleurant Abner, dit: Ce n’est nullement comme ont coutume de mourir les lâches, qu’est mort Abner.
34 Manja ako anali osamanga, mapazi ako anali osakulungidwa. Iwe wafa monga mmene amafera anthu pamaso pa anthu oyipa.” Ndipo anthu onse analiranso kulirira Abineri.
Tes mains n’ont pas été liées, et tes pieds n’ont pas été chargés de fer; mais comme on a coutume de tomber devant des fils d’iniquité, ainsi tu es tombé. Alors tout le peuple redoubla de pleurs sur lui.
35 Kenaka onse anabwera kwa Davide kumuwumiriza kuti adye kusanade. Koma Davide analumbira kuti, “Mulungu andilange ine, andilange kwambiri, ngati ndilawe buledi kapena chilichonse dzuwa lisanalowe!”
Et lorsque toute la multitude fut venue pour prendre de la nourriture avec David, le jour étant encore brillant, David jura, disant: Que Dieu me fasse ceci, et qu’il ajoute cela, si avant le coucher du soleil je goûte du pain ou de quelque autre chose!
36 Anthu onse anadziwa zimenezi ndipo zinawakondweretsa ndithu. Zonse zimene mfumu inachita zinawakondweretsa.
Et tout le peuple entendit, et ils agréèrent tout ce que le roi fit en la présence de tout le peuple.
37 Kotero tsiku limeneli anthu onse ndi Aisraeli onse anadziwa kuti sikunali kufuna kwa mfumu kuti Abineri mwana wa Neri aphedwe.
Et toute la multitude connut, et tout Israël en ce jour-là, qu’il n’avait pas été décidé par le roi qu’Abner, fils de Ner. serait tué.
38 Ndipo mfumu inati kwa ankhondo ake, “Kodi inu simukudziwa kuti lero mu Israeli mwagwa kalonga ndi munthu wamkulu?
Le roi dit aussi à ses serviteurs: Est-ce que vous ignorez qu’un prince et un grand est tombé aujourd’hui en Israël?
39 Ndipo lero, ngakhale ine ndine mfumu yodzozedwa, ndilibe mphamvu ndipo ana awa a Zeruya ndi amphamvu kwa ine. Yehova abwezere woyipa molingana ndi zoyipa zake!”
Pour moi, je suis encore faible, quoique oint roi; mais les fils de Sarvia sont durs pour moi: que le Seigneur rende à celui qui fait le mal, selon sa malice.

< 2 Samueli 3 >