< 2 Samueli 3 >
1 Nkhondo ya pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide inachitika nthawi yayitali. Mphamvu za Davide zinkakulirakulirabe, pamene banja la Sauli mphamvu zake zimapita zicheperachepera.
La guerre fut longue entre la maison de Saül et la maison de David. David allait se fortifiant, et la maison de Saül allait s’affaiblissant.
2 Ana aamuna a Davide amene anabadwira ku Hebroni anali awa: Woyamba anali Amnoni, amayi ake anali Ahinoamu wa ku Yezireeli.
Il naquit à David des fils à Hébron. Son premier-né fut Ammon, d’Achinoam de Jezraël;
3 Mwana wachiwiri anali Kileabu, amayi ake anali Abigayeli mkazi wamasiye wa Nabala wa ku Karimeli. Wachitatu anali Abisalomu, amayi ake anali Maaka mwana wa Talimai mfumu ya Gesuri;
le second Chéléab, d’Abigaïl de Carmel, femme de Nabal; le troisième Absalom, fils de Maaca, fille de Tholmaï, roi de Gessur;
4 wachinayi anali Adoniya, amayi ake anali Hagiti; wachisanu, Sefatiya amayi ake anali Abitali;
le quatrième Adonias, fils de Haggith; le cinquième Saphathia, fils d’Abital,
5 ndipo wachisanu ndi chimodzi anali Itireamu, amayi ake anali Egila, mkazi wa Davide. Ana awa a Davide anabadwira ku Hebroni.
et le sixième Jéthraam, d’Egla, femme de David. Tels sont les fils qui naquirent à David à Hébron.
6 Pamene kunali nkhondo pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide, Abineri anayamba kudzipatsa yekha mphamvu pakati pa banja la Sauli.
Pendant qu’il y avait guerre entre la maison de Saül et la maison de David, Abner se fortifiait dans la maison de Saül.
7 Sauli anali ndi mzikazi dzina lake Rizipa mwana wa Ayiwa. Ndipo Isiboseti anati kwa Abineri, “Nʼchifukwa chiyani unagona ndi mzikazi wa abambo anga?”
Or Saül avait eu une concubine, nommée Respha, fille d’Aia. Et Isboseth dit à Abner:
8 Abineri anakwiya kwambiri chifukwa cha zimene Isi-Boseti ananena ndipo anamuyankha kuti “Kodi ukuyesa ndine mutu wagalu umene ali mbali ya Ayuda? Lero lino ndine wokhulupirika ku nyumba ya abambo ako, Sauli ndi banja lake ndi anzake. Ine sindinakupereke kwa Davide, koma tsopano ukundinena pa cholakwa chimene ndachita pa mkazi uyu!
« Pourquoi es-tu venu vers la concubine de mon père? » Abner, très irrité des paroles d’Isboseth, répondit: « Suis-je une tête de chien appartenant à Juda? Aujourd’hui je montre de la faveur à la maison de Saül, ton père, à ses frères et à ses amis, et je ne t’ai pas livré aux mains de David, et c’est aujourd’hui que tu me reproches une faute avec cette femme?
9 Mulungu andilange ine Abineri, andilange kwambiri, ngati sindichitira Davide zimene Yehova anamulonjeza iye mwa lumbiro.
Que Dieu traite Abner dans toute sa rigueur, si je n’agis pas avec David selon ce que Yahweh lui a juré,
10 Ndidzachotsa ufumu ku nyumba ya Sauli ndi kukhazikitsa ufumu wa Davide pa Aisraeli onse ndi Yuda kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba.”
en disant qu’il enlèverait la royauté de la maison de Saül, et qu’il établirait le trône de David sur Israël et sur Juda, depuis Dan jusqu’à Bersabée! »
11 Isiboseti sanayerekezenso kunena mawu ena kwa Abineri, chifukwa ankamuopa.
Isboseth ne put répondre un seul mot à Abner, parce qu’il le craignait.
12 Kenaka Abineri anatuma amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Kodi dzikoli ndi la yani? Uchite mgwirizano ndi ine ndipo ndidzakuthandiza kuti Aisraeli onse azikutsatira.”
Abner envoya des messagers à David pour lui dire de sa part: « A qui est le pays? Fais ton alliance avec moi, et voici que ma main t’aidera pour tourner vers toi tout Israël. »
13 Davide anati, “Chabwino. Ine ndichita mgwirizano ndi iwe. Koma ndikukupempha chinthu chimodzi: Usabwere pamaso panga pokhapokha utabweretsa Mikala mwana wamkazi wa Sauli, ukamabwera kudzandiona.”
Il répondit: « Bien! je ferai alliance avec toi; mais je te demande une chose, c’est que tu ne voies pas ma face sans m’amener Michol, fille de Saül, lorsque tu viendras pour voir ma face. »
14 Ndipo Davide anatuma amithenga kwa Isi-Boseti mwana wa Sauli, kumulamula kuti, “Patse mkazi wanga Mikala, amene ndinamukwatira ndi makungu 100 a msonga za mavalo a Afilisti.”
Et David envoya des messagers à Isboseth, fils de Saül, pour lui dire: « Donne-moi ma femme Michol, que j’ai épousée pour cent prépuces de Philistins. »
15 Kotero Isi-Boseti analamulira ndipo anakamutenga kwa mwamuna wake Palitieli mwana wa Laisi.
Isboseth l’envoya prendre à son mari Phaltiel, fils de Laïs;
16 Koma mwamuna wake anapita naye akulira pambuyo pake njira yonse mpaka ku Bahurimu. Kenaka Abineri anati kwa iye, “Bwerera kwanu!” Ndipo anabwerera kwawo.
et son mari l’accompagna, marchant et pleurant derrière elle, jusqu’à Bathurim. Là Abner lui dit: « Va, retourne chez toi. » Et il s’en retourna.
17 Abineri anakambirana ndi akuluakulu a Israeli ndipo anati, “Kwa kanthawi mwakhala mukufuna kulonga Davide kuti akhale mfumu yanu.
Abner eut des pourparlers avec les anciens d’Israël, et leur dit: « Vous désiriez depuis longtemps déjà avoir David pour roi;
18 Tsopano chitani zimenezo! Pakuti Yehova analonjeza Davide kuti, ‘Kudzera mwa mtumiki wanga Davide ndidzapulumutsa anthu anga Aisraeli mʼdzanja la Afilisti ndi kuwachotsa mʼmanja mwa adani awo.’”
agissez donc maintenant, car Yahweh a dit à David: C’est par la main de David, mon serviteur, que je délivrerai mon peuple d’Israël de la main des Philistins et de la main de tous ses ennemis. »
19 Abineri anayankhulanso nawo yekha anthu a fuko la Benjamini. Kenaka anapita ku Hebroni kukamuwuza Davide zonse zimene Aisraeli ndi fuko lonse la Benjamini amafuna kuchita.
Abner parla aussi aux oreilles de Benjamin, et Abner alla reporter aux oreilles de David, à Hébron, ce qui paraissait bon aux yeux d’Israël et aux yeux de toute la maison de Benjamin.
20 Abineri, amene anali ndi anthu makumi awiri, atafika kwa Davide ku Hebroni, Davide anamukonzera phwando pamodzi ndi anthu ake.
Abner vint près de David, à Hébron, accompagné de vingt hommes; et David fit un festin à Abner et aux hommes qui l’accompagnaient.
21 Ndipo Abineri anawuza Davide kuti, “Loleni kuti ndipite msanga kukasonkhanitsa Aisraeli onse kuti abwere kwa inu kuno, mbuye wanga mfumu, kuti adzachite nanu pangano, ndipo kuti muzilamulira kulikonse kumene mtima wanu ufuna.” Kotero Davide analola Abineri kuti apite, ndipo anapita mwamtendere.
Et Abner dit à David: « Je vais me lever et partir pour rassembler tout Israël vers mon seigneur le roi; ils feront alliance avec toi et tu régneras sur tout ce que ton âme désire. » Et David congédia Abner, qui s’en alla en paix.
22 Nthawi yomweyo ankhondo a Davide ndi Yowabu anafika kuchokera kumene anakathira nkhondo ndipo anabweretsa katundu wambiri wolanda ku nkhondo. Koma Abineri sanalinso ndi Davide ku Hebroni, chifukwa Davide anamulola kuti apite, ndipo anapita mu mtendere.
Mais voici que les serviteurs de David et Joab revenaient d’une excursion, ramenant avec eux un grand butin. — Abner n’était plus auprès de David à Hébron, car David l’avait congédié et il s’en était allé en paix. —
23 Yowabu ndi asilikali onse amene anali naye atafika, anawuzidwa kuti Abineri mwana wa Neri anabwera kwa mfumu ndipo kuti mfumu yamulola kuti apite ndi kuti wapita ndi mtendere.
Joab et toute la troupe qui était avec lui arrivèrent, et on fit ce rapport à Joab: « Abner, fils de Ner, est venu auprès du roi, qui l’a congédié, et il s’en est allé en paix. »
24 Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Mwachita chiyani? Taonani, Abineri anabwera kwa inu. Nʼchifukwa chiyani mwamulola kuti apite? Tsopanotu wapitadi!
Joab se rendit chez le roi et dit: « Qu’as-tu fait? Voilà qu’Abner est venu vers toi: pourquoi l’as-tu congédié et laissé partir?
25 Inu mukumudziwa bwino Abineri mwana wa Neri. Iye anabwera kudzakunamizani ndi kudzaona mayendedwe anu ndiponso kudzaona zonse zimene mukuchita.”
Tu connais Abner, fils de Ner: c’est pour te tromper qu’il est venu, pour épier ta conduite, et savoir tout ce que tu fais. »
26 Kenaka Yowabu anachoka pamaso pa Davide ndipo anatumiza amithenga kutsatira Abineri, ndipo anabwera naye kuchokera ku chitsime cha Sira. Koma Davide sanadziwe zimenezi.
Joab, ayant quitté David, envoya sur les traces d’Abner des messagers qui le ramenèrent depuis la citerne de Sira, sans que David en sût rien.
27 Tsono Abineri atabwerera ku Hebroni, Yowabu anamutengera pambali ku chipata, kukhala ngati akufuna kuyankhula naye mwamseri. Ndipo kumeneko pobwezera imfa ya mʼbale wake Asaheli, Yowabu analasa iyeyo mʼmimba, ndipo anafa.
Quand Abner fut de retour à Hébron, Joab le tira à l’écart, dans l’intérieur de la porte, comme pour lui parler tranquillement, et là il le frappa au ventre; il mourut, à cause du sang d’Asaël, frère de Joab.
28 Patapita nthawi, Davide atamva zimenezi anati, “Ine ndi ufumu wanga tidzakhala osalakwa pamaso pa Yehova pa imfa ya Abineri mwana wa Neri.
David l’apprit ensuite, et il dit: « Je suis à jamais, moi et mon royaume, innocent, devant Yahweh, du sang d’Abner, fils de Ner.
29 Mlandu umenewu ukhala pa Yowabu ndi banja lonse la abambo ake! Mʼbanja la Yowabu musadzasowe munthu wodwala matenda a chizonono kapena khate, kapena wolumala woyendera ndodo kapena wophedwa ndi lupanga, kapena wosowa chakudya.”
Que ce sang retombe sur la tête de Joab et sur toute la maison de son père! Qu’il y ait toujours dans la maison de Joab un homme qui souffre d’un flux ou de la lèpre, ou qui tienne le fuseau, ou qui tombe par l’épée, ou qui manque de pain. »
30 (Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anapha Abineri chifukwa iye anapha mʼbale wawo Asaheli ku nkhondo ku Gibiyoni).
C’est ainsi que Joab et Abisaï, son frère, tuèrent Abner, parce qu’il avait donné la mort à leur frère Asaël, à Gabaon, dans la bataille.
31 Ndipo Davide anati kwa Yowabu ndi anthu onse amene anali nawo, “Ngʼambani zovala zanu ndipo muvale ziguduli, muyende mukulira patsogolo pa Abineri.” Mfumu Davide mwini anayenda motsatira chitandacho.
David dit à Joab et à tout le peuple qui était avec lui: « Déchirez-vos vêtements, ceignez-vous de sacs et faites le deuil devant Abner. » Et le roi David marchait derrière la litière.
32 Iwo anamuyika Abineri mʼmanda ku Hebroni ndipo mfumu inalira mokweza pa manda a Abineri. Ndipo anthu onse analiranso.
On enterra Abner à Hébron. Le roi pleura à haute voix sur le tombeau d’Abner et tout le peuple pleura.
33 Mfumu inayimba nyimbo iyi ya maliro a Abineri: “Abineri nʼkufa motere monga mmene chimafera chitsiru.
Le roi chanta un chant funèbre sur Abner, et dit: Abner devait-il mourir comme meurt un insensé?
34 Manja ako anali osamanga, mapazi ako anali osakulungidwa. Iwe wafa monga mmene amafera anthu pamaso pa anthu oyipa.” Ndipo anthu onse analiranso kulirira Abineri.
Tes mains ne furent pas liées et tes pieds ne furent pas jetés dans les chaînes! Tu es tombé comme on tombe devant des scélérats. Tout le peuple continua de se lamenter sur Abner;
35 Kenaka onse anabwera kwa Davide kumuwumiriza kuti adye kusanade. Koma Davide analumbira kuti, “Mulungu andilange ine, andilange kwambiri, ngati ndilawe buledi kapena chilichonse dzuwa lisanalowe!”
et tout le peuple s’approcha de David pour lui faire prendre de la nourriture lorsqu’il était encore jour. Mais David fit ce serment: « Que Yahweh me traite dans toute sa rigueur, si je goûte du pain ou quoi que ce soit avant le coucher du soleil! »
36 Anthu onse anadziwa zimenezi ndipo zinawakondweretsa ndithu. Zonse zimene mfumu inachita zinawakondweretsa.
Tout le peuple le remarqua et le trouva bon, comme il trouvait bon tout ce que faisait le roi.
37 Kotero tsiku limeneli anthu onse ndi Aisraeli onse anadziwa kuti sikunali kufuna kwa mfumu kuti Abineri mwana wa Neri aphedwe.
Tout le peuple et tout Israël comprirent en ce jour que ce n’était pas de par le roi qu’on avait fait mourir Abner, fils de Ner.
38 Ndipo mfumu inati kwa ankhondo ake, “Kodi inu simukudziwa kuti lero mu Israeli mwagwa kalonga ndi munthu wamkulu?
Le roi dit à ses serviteurs: « Ne savez-vous pas qu’un chef, qu’un grand homme est tombé aujourd’hui en Israël?
39 Ndipo lero, ngakhale ine ndine mfumu yodzozedwa, ndilibe mphamvu ndipo ana awa a Zeruya ndi amphamvu kwa ine. Yehova abwezere woyipa molingana ndi zoyipa zake!”
Pour moi, je suis doux, quoiqu’ayant reçu l’onction royale; et ces hommes, les fils de Sarvia, sont plus durs que moi. Que Yahweh rende à qui fait le mal selon le mal qu’il fait! »