< 2 Samueli 3 >

1 Nkhondo ya pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide inachitika nthawi yayitali. Mphamvu za Davide zinkakulirakulirabe, pamene banja la Sauli mphamvu zake zimapita zicheperachepera.
Krigen imellem Sauls og Davids Huse trak i Langdrag; men David blev stærkere og stærkere, Sauls Hus svagere og svagere.
2 Ana aamuna a Davide amene anabadwira ku Hebroni anali awa: Woyamba anali Amnoni, amayi ake anali Ahinoamu wa ku Yezireeli.
I Hebron fødtes der David Sønner; hans førstefødte var Amnon, Søn af Ahinoam fra Jizre'el,
3 Mwana wachiwiri anali Kileabu, amayi ake anali Abigayeli mkazi wamasiye wa Nabala wa ku Karimeli. Wachitatu anali Abisalomu, amayi ake anali Maaka mwana wa Talimai mfumu ya Gesuri;
den næstældste Kil'ab, Søn af Abigajil, Karmeliten Nabals Hustru, den tredje Absalom, en Søn af Kong Talmaj af Gesjurs Datter Ma'aka,
4 wachinayi anali Adoniya, amayi ake anali Hagiti; wachisanu, Sefatiya amayi ake anali Abitali;
den fjerde Adonija, en Søn af Haggit, den femte Sjefatja, en Søn af Abital,
5 ndipo wachisanu ndi chimodzi anali Itireamu, amayi ake anali Egila, mkazi wa Davide. Ana awa a Davide anabadwira ku Hebroni.
og den sjette Jitream, Søn af Davids Hustru Egla. Disse fødtes David i Hebron.
6 Pamene kunali nkhondo pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide, Abineri anayamba kudzipatsa yekha mphamvu pakati pa banja la Sauli.
Under Krigen mellem Sauls og Davids Huse ydede Abner Sauls Hus kraftig Støtte.
7 Sauli anali ndi mzikazi dzina lake Rizipa mwana wa Ayiwa. Ndipo Isiboseti anati kwa Abineri, “Nʼchifukwa chiyani unagona ndi mzikazi wa abambo anga?”
Nu havde Saul haft en Medhustru ved Navn Rizpa, Ajjas Datter. Og Isjbosjet sagde til Abner: »Hvorfor gik du ind til min Faders Medhustru?«
8 Abineri anakwiya kwambiri chifukwa cha zimene Isi-Boseti ananena ndipo anamuyankha kuti “Kodi ukuyesa ndine mutu wagalu umene ali mbali ya Ayuda? Lero lino ndine wokhulupirika ku nyumba ya abambo ako, Sauli ndi banja lake ndi anzake. Ine sindinakupereke kwa Davide, koma tsopano ukundinena pa cholakwa chimene ndachita pa mkazi uyu!
Abner blev opbragt over Isjbosjets Ord og sagde: »Er jeg nu blevet et Hundehoved fra Juda? Nu har jeg Gang paa Gang vist Godhed mod din Fader Sauls Hus, hans Brødre og Venner og ikke ladet dig falde i Davids Haand, og saa gaar du nu i Rette med mig for en Kvindes Skyld!
9 Mulungu andilange ine Abineri, andilange kwambiri, ngati sindichitira Davide zimene Yehova anamulonjeza iye mwa lumbiro.
Gud ramme Abner baade med det ene og det andet: Hvad HERREN tilsvor David, skal jeg nu sørge for bliver opfyldt paa ham;
10 Ndidzachotsa ufumu ku nyumba ya Sauli ndi kukhazikitsa ufumu wa Davide pa Aisraeli onse ndi Yuda kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba.”
jeg skal sørge for, at Sauls Hus mister Kongedømmet og Davids Trone bliver rejst over Israel og Juda fra Dan til Be'ersjeba!«
11 Isiboseti sanayerekezenso kunena mawu ena kwa Abineri, chifukwa ankamuopa.
Og af Frygt for Abner kunde Isjbosjet ikke svare et Ord.
12 Kenaka Abineri anatuma amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Kodi dzikoli ndi la yani? Uchite mgwirizano ndi ine ndipo ndidzakuthandiza kuti Aisraeli onse azikutsatira.”
Saa sendte Abner Sendebud til David i Hebron og lod sige: »Slut Pagt med mig! Se, jeg vil hjælpe dig og bringe hele Israel over paa din Side!«
13 Davide anati, “Chabwino. Ine ndichita mgwirizano ndi iwe. Koma ndikukupempha chinthu chimodzi: Usabwere pamaso panga pokhapokha utabweretsa Mikala mwana wamkazi wa Sauli, ukamabwera kudzandiona.”
Han svarede: »Vel, jeg vil slutte Pagt med dig; men een Ting kræver jeg af dig: Du bliver ikke stedet for mit Aasyn, med mindre du har Sauls Datter Mikal med, naar du kommer!«
14 Ndipo Davide anatuma amithenga kwa Isi-Boseti mwana wa Sauli, kumulamula kuti, “Patse mkazi wanga Mikala, amene ndinamukwatira ndi makungu 100 a msonga za mavalo a Afilisti.”
David sendte derpaa Bud til Isjbosjet, Sauls Søn, og lod sige: »Giv mig min Hustru Mikal, som jeg blev trolovet med for 100 Filisterforhuder!«
15 Kotero Isi-Boseti analamulira ndipo anakamutenga kwa mwamuna wake Palitieli mwana wa Laisi.
Da sendte Isjbosjet Bud og lod hende hente hos hendes Mand Paltiel, Lajisj's Søn.
16 Koma mwamuna wake anapita naye akulira pambuyo pake njira yonse mpaka ku Bahurimu. Kenaka Abineri anati kwa iye, “Bwerera kwanu!” Ndipo anabwerera kwawo.
Hendes Mand fulgte hende grædende lige til Bahurim; her sagde Abner til ham: »Gaa nu hjem!« Saa vendte han hjem.
17 Abineri anakambirana ndi akuluakulu a Israeli ndipo anati, “Kwa kanthawi mwakhala mukufuna kulonga Davide kuti akhale mfumu yanu.
Men Abner havde forhandlet med Israels Ældste og sagt: »Allerede tidligere ønskede I David til Konge;
18 Tsopano chitani zimenezo! Pakuti Yehova analonjeza Davide kuti, ‘Kudzera mwa mtumiki wanga Davide ndidzapulumutsa anthu anga Aisraeli mʼdzanja la Afilisti ndi kuwachotsa mʼmanja mwa adani awo.’”
saa gør nu Alvor af det! Thi HERREN har sagt om David: Ved min Tjener Davids Haand vil jeg frelse mit Folk Israel fra Filisternes og alle dets Fjenders Haand!«
19 Abineri anayankhulanso nawo yekha anthu a fuko la Benjamini. Kenaka anapita ku Hebroni kukamuwuza Davide zonse zimene Aisraeli ndi fuko lonse la Benjamini amafuna kuchita.
Abner talte ogsaa til Benjamin derom. Endelig gik Abner ogsaa til Hebron for at meddele David alt, hvad Israel og hele Benjamins Hus havde vedtaget.
20 Abineri, amene anali ndi anthu makumi awiri, atafika kwa Davide ku Hebroni, Davide anamukonzera phwando pamodzi ndi anthu ake.
Da Abner, fulgt af tyve Mænd, kom til David i Hebron, gjorde David Gæstebud for Abner og Mændene, som var med ham.
21 Ndipo Abineri anawuza Davide kuti, “Loleni kuti ndipite msanga kukasonkhanitsa Aisraeli onse kuti abwere kwa inu kuno, mbuye wanga mfumu, kuti adzachite nanu pangano, ndipo kuti muzilamulira kulikonse kumene mtima wanu ufuna.” Kotero Davide analola Abineri kuti apite, ndipo anapita mwamtendere.
Derpaa sagde Abner til David: »Lad mig bryde op og drage hen og samle hele Israel om min Herre Kongen, for at de kan slutte Pagt med dig, at du kan blive Konge over alt, hvad din Hu staar til!« Da lod David Abner rejse, og han drog bort i Fred.
22 Nthawi yomweyo ankhondo a Davide ndi Yowabu anafika kuchokera kumene anakathira nkhondo ndipo anabweretsa katundu wambiri wolanda ku nkhondo. Koma Abineri sanalinso ndi Davide ku Hebroni, chifukwa Davide anamulola kuti apite, ndipo anapita mu mtendere.
Just da kom Davids Folk og Joab hjem fra et Strejftog og medførte et rigt Bytte; Abner var da ikke mere hos David i Hebron, thi David havde ladet ham rejse, og han var draget bort i Fred.
23 Yowabu ndi asilikali onse amene anali naye atafika, anawuzidwa kuti Abineri mwana wa Neri anabwera kwa mfumu ndipo kuti mfumu yamulola kuti apite ndi kuti wapita ndi mtendere.
Da nu Joab var vendt hjem med hele sin Hær, fik han at vide at Abner, Ners Søn, havde været hos Kongen, og at denne havde ladet ham rejse, saa han var draget bort i Fred.
24 Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Mwachita chiyani? Taonani, Abineri anabwera kwa inu. Nʼchifukwa chiyani mwamulola kuti apite? Tsopanotu wapitadi!
Da gik Joab til Kongen og sagde: »Hvad har du gjort? Abner har jo været hos dig! Hvorfor lod du ham rejse, saa han frit kunde drage bort?
25 Inu mukumudziwa bwino Abineri mwana wa Neri. Iye anabwera kudzakunamizani ndi kudzaona mayendedwe anu ndiponso kudzaona zonse zimene mukuchita.”
Indser du ikke, at Abner, Ners Søn, kun kom for at bedrage dig, udspejde din Færd og faa at vide, hvad du har for!«
26 Kenaka Yowabu anachoka pamaso pa Davide ndipo anatumiza amithenga kutsatira Abineri, ndipo anabwera naye kuchokera ku chitsime cha Sira. Koma Davide sanadziwe zimenezi.
Saa gik Joab bort fra David og sendte uden Davids Vidende Sendebud efter Abner og de hentede ham tilbage fra Bor-Sira.
27 Tsono Abineri atabwerera ku Hebroni, Yowabu anamutengera pambali ku chipata, kukhala ngati akufuna kuyankhula naye mwamseri. Ndipo kumeneko pobwezera imfa ya mʼbale wake Asaheli, Yowabu analasa iyeyo mʼmimba, ndipo anafa.
Og da Abner kom tilbage til Hebron, tog Joab ham til Side midt i Porten for at tale uhindret med ham; og der dræbte han ham ved et Stik i Underlivet for at hævne sin Broder Asa'els Blod.
28 Patapita nthawi, Davide atamva zimenezi anati, “Ine ndi ufumu wanga tidzakhala osalakwa pamaso pa Yehova pa imfa ya Abineri mwana wa Neri.
Da det siden kom David for Øre, sagde han: »Jeg og mit Rige er til evig Tid uden Skyld for HERREN i Abners, Ners Søns, Blod!
29 Mlandu umenewu ukhala pa Yowabu ndi banja lonse la abambo ake! Mʼbanja la Yowabu musadzasowe munthu wodwala matenda a chizonono kapena khate, kapena wolumala woyendera ndodo kapena wophedwa ndi lupanga, kapena wosowa chakudya.”
Det komme over Joabs Hoved og over hele hans Fædrenehus; og Joabs Hus være aldrig frit for Folk, som lider af Flaad eller Spedalsk hed, gaar med Krykke eller falder for Sværdet eller mangler Brød!«
30 (Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anapha Abineri chifukwa iye anapha mʼbale wawo Asaheli ku nkhondo ku Gibiyoni).
Men Joab og hans Broder Abisjaj havde slaaet Abner ihjel, fordi han havde fældet deres Broder Asa'el i Kampen ved Gibeon.
31 Ndipo Davide anati kwa Yowabu ndi anthu onse amene anali nawo, “Ngʼambani zovala zanu ndipo muvale ziguduli, muyende mukulira patsogolo pa Abineri.” Mfumu Davide mwini anayenda motsatira chitandacho.
Derpaa sagde David til Joab og alle Folkene, som fulgte ham: »Sønderriv eders Klæder, tag Sæk om eder og hold Klage over Abner!« Og Kong David gik selv bag efter Baaren.
32 Iwo anamuyika Abineri mʼmanda ku Hebroni ndipo mfumu inalira mokweza pa manda a Abineri. Ndipo anthu onse analiranso.
Og da man jordede Abner i Hebron, græd Kongen højt ved Abners Grav, og alt Folket græd med,
33 Mfumu inayimba nyimbo iyi ya maliro a Abineri: “Abineri nʼkufa motere monga mmene chimafera chitsiru.
Da sang Kongen denne Klagesang over Abner: Skulde Abner dø en Daares Død?
34 Manja ako anali osamanga, mapazi ako anali osakulungidwa. Iwe wafa monga mmene amafera anthu pamaso pa anthu oyipa.” Ndipo anthu onse analiranso kulirira Abineri.
Dine Hænder var ikke bundne, dine Fødder ikke lagt i Lænker, du faldt, som man falder for Misdædere! Da græd hele Folket end mere over ham,
35 Kenaka onse anabwera kwa Davide kumuwumiriza kuti adye kusanade. Koma Davide analumbira kuti, “Mulungu andilange ine, andilange kwambiri, ngati ndilawe buledi kapena chilichonse dzuwa lisanalowe!”
og da hele Folket kom for at faa David til at spise, medens det endnu var Dag, svor David: »Gud ramme mig baade med det ene og det andet, om jeg smager Brød eller noget andet, før Sol gaar ned!«
36 Anthu onse anadziwa zimenezi ndipo zinawakondweretsa ndithu. Zonse zimene mfumu inachita zinawakondweretsa.
Hele Folket lagde Mærke dertil, og det gjorde et godt Indtryk paa dem; alt, hvad Kongen foretog sig, gjorde et godt Indtryk paa alt Folket;
37 Kotero tsiku limeneli anthu onse ndi Aisraeli onse anadziwa kuti sikunali kufuna kwa mfumu kuti Abineri mwana wa Neri aphedwe.
og hele Folket og hele Israel skønnede den Dag, at Kongen ikke var Ophavsmand til Drabet paa Abner, Ners Søn.
38 Ndipo mfumu inati kwa ankhondo ake, “Kodi inu simukudziwa kuti lero mu Israeli mwagwa kalonga ndi munthu wamkulu?
Og Kongen sagde til sine Folk: »Ved I ikke, af der i Dag er faldet en Øverste og Stormand i Israel?
39 Ndipo lero, ngakhale ine ndine mfumu yodzozedwa, ndilibe mphamvu ndipo ana awa a Zeruya ndi amphamvu kwa ine. Yehova abwezere woyipa molingana ndi zoyipa zake!”
Men jeg er endnu for svag, skønt jeg er salvet til Konge, og disse Mænd, Zerujasønnerne, er mig for stærke. HERREN gengælde Udaadsmanden hans Skændselsdaad!«

< 2 Samueli 3 >