< 2 Samueli 23 >
1 Nawa mawu otsiriza a Davide: “Mawu a Davide mwana wa Yese, mawu a munthu amene wakwezedwa ndi Wammwambamwamba, munthu wodzozedwa ndi Mulungu wa Yakobo, woyimba nyimbo za Israeli:
Mais voici les dernières paroles de David. David, fils d’Isaï, a parlé; l’homme institué le christ du Dieu de Jacob, l’excellent psalmiste d’Israël, a dit:
2 “Mzimu wa Yehova unayankhula kudzera mwa ine; mawu ake anali pakamwa panga.
L’Esprit du Seigneur s’est fait entendre par moi, et sa parole par ma langue.
3 Mulungu wa Israeli anayankhula, Thanthwe la Israeli linati kwa ine: ‘Pamene munthu alamulira anthu mwachilungamo, pamene alamulira moopa Mulungu,
Le Dieu d’Israël m’a dit: le Fort d’Israël a parlé: le dominateur des hommes, le juste dominateur dans la crainte de Dieu sera
4 amakhala ngati kuwala kwa mmamawa, mmawa wopanda mitambo, monga kuwala pamene mvula yaleka kugwa imene imameretsa udzu mʼnthaka.’
Comme la lumière de l’aurore, qui, au soleil levant, le matin, brille sans nuages, et comme l’herbe qui germe de la terre par les pluies.
5 “Kodi banja langa silolungama pamaso pa Mulungu? Kodi Iye sanachite pangano losatha ndi ine, lokonzedwa ndi lotetezedwa mbali zonse? Kodi sadzakwaniritsa chipulumutso changa, ndi kundipatsa chokhumba changa chilichonse?
Et ma maison n’était pas si grande devant Dieu, pour qu’il fit avec moi un pacte éternel, ferme en toutes choses et assuré; car ce pacte est tout mon salut et toute ma volonté; et rien n’en provient qui ne porte ses fruits.
6 Koma anthu oyipa ndiwo ayenera kutayidwa kunja ngati minga, imene sitengedwa ndi manja.
Mais les prévaricateurs seront extirpés tous comme des épines que l’on n’arrache pas avec les mains.
7 Aliyense amene wayikhudza mingayo amayidula pogwiritsa ntchito chigwandali kapena ndodo ya mkondo; nayitentha pa moto.”
Et si quelqu’un veut les toucher, il s’arme de fer, et d’un bois de lance, et brûlées par le feu, elles sont consumées jusqu’à néant.
8 Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yosebu-Basebeti wa ku Takemoni mkulu wa atsogoleri a ankhondo atatu. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 800 nthawi imodzi.
Voici le nom des braves de David. Celui qui était assis dans la chaire, le plus sage, le premier entre les trois; c’est lui qui, comme le petit ver le plus tendre du bois, tua huit cents hommes en une seule fois.
9 Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi. Monga mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu a Davide, iye anali ndi Davide pamene anazunza Afilisti amene anasonkhana ku Pasi-Damimu kuchita nkhondo. Kenaka ankhondo a Israeli anabwerera mʼmbuyo.
Après lui, Éléazar, Ahohite, fils de son oncle paternel, était entre les trois braves qui étaient avec David, lorsqu’ils insultèrent les Philistins, et qu’ils s’assemblèrent en ce lieu pour le combat.
10 Koma iye anayima osasuntha ndipo anakantha Afilisti mpaka mkono wake unatopa ndipo unakanirira ku lupanga lake. Yehova anapereka chigonjetso chachikulu pa tsiku limenelo. Asilikali anabwerera kwa Eliezara, kukatenga katundu wa anthu ophedwa.
Et lorsque les hommes d’Israël eurent monté, lui se présenta, et battit les Philistins, jusqu’à ce que sa main se lassât et demeurât attachée à son glaive; et le Seigneur donna une grande victoire à Israël en ce jour-là, et le peuple, qui avait fui, retourna pour enlever les dépouilles des morts.
11 Wotsatana naye anali Sama mwana wa Age Mharari. Pamene Afilisti anasonkhana pamalo pamene panali munda wa mphodza, ankhondo a Israeli anathawa Afilistiwo.
Et après lui venait Semma, fils d’Agé, d’Arari. Et les Philistins s’assemblèrent au poste; car il y avait là un champ plein de lentilles. Et lorsque le peuple se fut enfui devant les Philistins,
12 Koma Sama anayima pakati pa mundawo. Iye anawuteteza nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
Semma se tint au milieu du champ, le défendit et battit les Philistins; et le Seigneur accorda une grande victoire.
13 Pa nthawi yokolola, atatu mwa atsogoleri makumi atatu anabwera kwa Davide ku phanga la Adulamu, pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
Et déjà auparavant étaient descendus les trois qui étaient les premiers entre les trente, et ils étaient venus au temps de la moisson vers David, dans la caverne d’Odollam; mais le camp des Philistins était placé dans la Vallée des Géants.
14 Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
Et David était dans la forteresse; mais l’armée des Philistins était alors à Bethléhem.
15 Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
David donc fit un souhait, et dit: Oh! si quelqu’un me donnait à boire de l’eau de la citerne qui est à Bethléhem, près de la porte:
16 Choncho anthu amphamvu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
Les trois braves passèrent donc à travers le camp des Philistins, et puisèrent de l’eau dans la citerne de Bethléhem qui était près de la porte, et l’apportèrent à David; et David n’en voulut pas boire, mais il l’offrit en libations au Seigneur,
17 Iye anati, “Inu Yehova, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi awa si magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Ndipo Davide sanamwe madziwo. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
Disant: Que le Seigneur me soit propice, pour que je ne fasse pas cela: boirai-je le sang de ces hommes qui sont allés la chercher, et le péril de leurs âmes? Il ne voulut donc pas boire. Voilà ce que firent ces trois hommes très vigoureux.
18 Abisai mʼbale wa Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300, choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
Abisaï aussi, frère de Joab, fils de Sarvia, était le premier de trois autres: c’est lui qui leva sa lance contre trois cents, qu’il tua: il était renommé parmi ces trois,
19 Kodi iyeyo sanali wolemekezeka koposa? Iye anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
Et le plus noble d’entre ces trois, et leur chef; mais il n’atteignait pas les premiers.
20 Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
Ensuite Banaïas de Cabséel, fils de Joïada, homme très vaillant, et aux grands exploits; c’est lui qui tua les deux lions de Moab, et lui qui descendit et tua le lion au milieu de la citerne, dans les jours de la neige.
21 Ndipo iye anakanthanso Mwigupto wamkulu msinkhu. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
C’est lui qui tua l’Egyptien: homme digne d’être en spectacle et ayant en main une lance; c’est pourquoi, lorsqu’il fut descendu vers lui avec sa verge, il arracha de force la lance de la main de l’Egyptien, et le tua de sa lance.
22 Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
Voilà ce que fit Banaïas, fils de Joïada.
23 Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu aja, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
Et il était renommé entre les trois vaillants les plus nobles entre les trente; cependant il n’atteignait pas les trois premiers; et David le fit son conseiller intime.
24 Mʼgulu la anthu makumi atatu aja munalinso awa: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
Asaël, frère de Joab, était entre les trente; Eléhanan de Bethléhem, fils de l’oncle paternel d’Asaël;
25 Sama Mharodi, Elika Mherodi,
Semma de Harodi, Elica de Harodi,
26 Helezi Mpaliti, Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa,
Hélès de Phalti, Hira, fils d’Accès de Thécua;
27 Abiezeri wa ku Anatoti, Sibekai Mhusati,
Abiézer d’Anathoth, Mobonnaï de Husati,
28 Zalimoni Mwahohi, Maharai Mnetofa,
Selmon, l’Ahohite, Maharaï, le Nétophathite;
29 Heledi mwana wa Baana Mnetofa, Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini,
Héled, fils de Baana, lui aussi Nétophatite, Ithaï, fils de Ribaï de Gabaath des enfants de Benjamin;
30 Benaya Mpiratoni, Hidayi wa ku zigwa za Gaasi.
Banaï, le Pharathonite, Heddaï du torrent de Gaas,
31 Abi-Aliboni Mwaribati, Azimaveti Mbarihumi,
Abialbon, l’Arbathite, Azmaveth de Béromi,
32 Eliyahiba Msaaliboni, ana a Yaseni, Yonatani,
Eliaba de Salaboni. Les fils de Jassen, Jonathan,
33 mwana wa Sama Mharari, Ahiamu mwana wa Sarari Mharari,
Semma d’Orori; Ahiam, fils de Sarar, l’Arorite;
34 Elifeleti mwana wa Ahasibai Mmaakati, Eliamu mwana wa Ahitofele Mgiloni,
Eliphélet, fils d’Aasbaï, fils de Machati; Eliam, fils d’Achitophel, le Gélonite,
35 Heziro wa ku Karimeli, Paarai Mwaribi,
Hesraï du Carmel, Pharaï d’Arbi,
36 Igala mwana wa Natani wa ku Zoba, mwana wa Hagiri,
Igaal, fils de Nathan de Soba, Bonni de Gadi,
37 Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya,
Sélec d’Ammoni, Naharaï, le Bérothite, écuyer de Joab, fils de Sarvia,
38 Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
Ira, le Jéthrite, Gareb, lui aussi Jéthrite,
39 ndi Uriya Mhiti. Onse pamodzi analipo 37.
Urie, l’Héthéen. En tout trente-sept.