< 2 Samueli 23 >

1 Nawa mawu otsiriza a Davide: “Mawu a Davide mwana wa Yese, mawu a munthu amene wakwezedwa ndi Wammwambamwamba, munthu wodzozedwa ndi Mulungu wa Yakobo, woyimba nyimbo za Israeli:
Now these are the last words of David. David the son of Jesse said, and the man who was raised on high, the anointed of the God of Jacob, and the sweet psalmist of Israel, said,
2 “Mzimu wa Yehova unayankhula kudzera mwa ine; mawu ake anali pakamwa panga.
The Spirit of the LORD spoke by me, and his word was on my tongue.
3 Mulungu wa Israeli anayankhula, Thanthwe la Israeli linati kwa ine: ‘Pamene munthu alamulira anthu mwachilungamo, pamene alamulira moopa Mulungu,
The God of Israel said, the Rock of Israel spoke to me, He that ruleth over men must be just, ruling in the fear of God.
4 amakhala ngati kuwala kwa mmamawa, mmawa wopanda mitambo, monga kuwala pamene mvula yaleka kugwa imene imameretsa udzu mʼnthaka.’
And he shall be as the light of the morning, when the sun riseth, even a morning without clouds; as the tender grass springing out of the earth by clear shining after rain.
5 “Kodi banja langa silolungama pamaso pa Mulungu? Kodi Iye sanachite pangano losatha ndi ine, lokonzedwa ndi lotetezedwa mbali zonse? Kodi sadzakwaniritsa chipulumutso changa, ndi kundipatsa chokhumba changa chilichonse?
Although my house is not so with God; yet he hath made with me an everlasting covenant, ordered in all things, and sure: for this is all my salvation, and all my desire, although he maketh it not to grow.
6 Koma anthu oyipa ndiwo ayenera kutayidwa kunja ngati minga, imene sitengedwa ndi manja.
But the worthless, all of them shall be as thorns thrust away, because they cannot be taken with hands:
7 Aliyense amene wayikhudza mingayo amayidula pogwiritsa ntchito chigwandali kapena ndodo ya mkondo; nayitentha pa moto.”
But the man that shall touch them must be armed with iron and the staff of a spear; and they shall be utterly burned with fire in the same place.
8 Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yosebu-Basebeti wa ku Takemoni mkulu wa atsogoleri a ankhondo atatu. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 800 nthawi imodzi.
These are the names of the mighty men whom David had: The Tachmonite that sat in the seat, chief among the captains; the same was Adino the Eznite: he lifted up his spear against eight hundred, whom he slew at one time.
9 Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi. Monga mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu a Davide, iye anali ndi Davide pamene anazunza Afilisti amene anasonkhana ku Pasi-Damimu kuchita nkhondo. Kenaka ankhondo a Israeli anabwerera mʼmbuyo.
And after him was Eleazar the son of Dodo the Ahohite, one of the three mighty men with David, when they defied the Philistines that were there gathered together to battle, and the men of Israel had gone away:
10 Koma iye anayima osasuntha ndipo anakantha Afilisti mpaka mkono wake unatopa ndipo unakanirira ku lupanga lake. Yehova anapereka chigonjetso chachikulu pa tsiku limenelo. Asilikali anabwerera kwa Eliezara, kukatenga katundu wa anthu ophedwa.
He arose, and smote the Philistines until his hand was weary, and his hand clung to the sword: and the LORD wrought a great victory that day; and the people returned after him only to strip the slain.
11 Wotsatana naye anali Sama mwana wa Age Mharari. Pamene Afilisti anasonkhana pamalo pamene panali munda wa mphodza, ankhondo a Israeli anathawa Afilistiwo.
And after him was Shammah the son of Agee the Hararite. And the Philistines were gathered together into a troop, where was a piece of ground full of lentiles: and the people fled from the Philistines.
12 Koma Sama anayima pakati pa mundawo. Iye anawuteteza nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
But he stood in the midst of the ground, and defended it, and slew the Philistines: and the LORD wrought a great victory.
13 Pa nthawi yokolola, atatu mwa atsogoleri makumi atatu anabwera kwa Davide ku phanga la Adulamu, pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
And three of the thirty leaders went down, and came to David in the harvest time to the cave of Adullam: and the troop of the Philistines encamped in the valley of Rephaim.
14 Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
And David was then in a strong hold, and the garrison of the Philistines was then in Bethlehem.
15 Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
And David longed, and said, O that one would give me drink of the water of the well of Bethlehem, which is by the gate!
16 Choncho anthu amphamvu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
And the three mighty men broke through the host of the Philistines, and drew water out of the well of Bethlehem, that was by the gate, and took it, and brought it to David: nevertheless he would not drink of it, but poured it out to the LORD.
17 Iye anati, “Inu Yehova, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi awa si magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Ndipo Davide sanamwe madziwo. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
And he said, Be it far from me, O LORD, that I should do this: is not this the blood of the men that went in jeopardy of their lives? therefore he would not drink it. These things did these three mighty men.
18 Abisai mʼbale wa Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300, choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
And Abishai, the brother of Joab, the son of Zeruiah, was chief among three. And he lifted up his spear against three hundred, and slew them, and had the name among three.
19 Kodi iyeyo sanali wolemekezeka koposa? Iye anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
Was he not most honourable of three? therefore he was their captain: yet he attained not to the first three.
20 Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
And Benaiah the son of Jehoiada, the son of a valiant man, of Kabzeel, who had done many deeds, he slew two lionlike men of Moab: he went down also and slew a lion in the midst of a pit in time of snow:
21 Ndipo iye anakanthanso Mwigupto wamkulu msinkhu. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
And he slew an Egyptian, a handsome man: and the Egyptian had a spear in his hand; but he went down to him with a staff, and plucked the spear out of the Egyptian’s hand, and slew him with his own spear.
22 Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
These things did Benaiah the son of Jehoiada, and had a name among three mighty men.
23 Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu aja, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
He was more honourable than the thirty, but he attained not to the first three. And David set him over his guard.
24 Mʼgulu la anthu makumi atatu aja munalinso awa: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
Asahel the brother of Joab was one of the thirty; Elhanan the son of Dodo of Bethlehem,
25 Sama Mharodi, Elika Mherodi,
Shammah the Harodite, Elika the Harodite,
26 Helezi Mpaliti, Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa,
Helez the Paltite, Ira the son of Ikkesh the Tekoite,
27 Abiezeri wa ku Anatoti, Sibekai Mhusati,
Abiezer the Anethothite, Mebunnai the Hushathite,
28 Zalimoni Mwahohi, Maharai Mnetofa,
Zalmon the Ahohite, Maharai the Netophathite,
29 Heledi mwana wa Baana Mnetofa, Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini,
Heleb the son of Baanah, a Netophathite, Ittai the son of Ribai out of Gibeah of the children of Benjamin,
30 Benaya Mpiratoni, Hidayi wa ku zigwa za Gaasi.
Benaiah the Pirathonite, Hiddai of the brooks of Gaash,
31 Abi-Aliboni Mwaribati, Azimaveti Mbarihumi,
Abialbon the Arbathite, Azmaveth the Barhumite,
32 Eliyahiba Msaaliboni, ana a Yaseni, Yonatani,
Eliahba the Shaalbonite, of the sons of Jashen, Jonathan,
33 mwana wa Sama Mharari, Ahiamu mwana wa Sarari Mharari,
Shammah the Hararite, Ahiam the son of Sharar the Hararite,
34 Elifeleti mwana wa Ahasibai Mmaakati, Eliamu mwana wa Ahitofele Mgiloni,
Eliphelet the son of Ahasbai, the son of the Maachathite, Eliam the son of Ahithophel the Gilonite,
35 Heziro wa ku Karimeli, Paarai Mwaribi,
Hezrai the Carmelite, Paarai the Arbite,
36 Igala mwana wa Natani wa ku Zoba, mwana wa Hagiri,
Igal the son of Nathan of Zobah, Bani the Gadite,
37 Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya,
Zelek the Ammonite, Naharai the Beerothite, armourbearer to Joab the son of Zeruiah,
38 Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
Ira an Ithrite, Gareb an Ithrite,
39 ndi Uriya Mhiti. Onse pamodzi analipo 37.
Uriah the Hittite: thirty and seven in all.

< 2 Samueli 23 >