< 2 Samueli 23 >

1 Nawa mawu otsiriza a Davide: “Mawu a Davide mwana wa Yese, mawu a munthu amene wakwezedwa ndi Wammwambamwamba, munthu wodzozedwa ndi Mulungu wa Yakobo, woyimba nyimbo za Israeli:
Now these be the last words of David. David the son of Jesse saith, and the man who was raised on high saith, the anointed of the God of Jacob, and the sweet psalmist of Israel:
2 “Mzimu wa Yehova unayankhula kudzera mwa ine; mawu ake anali pakamwa panga.
The spirit of the LORD spake by me, and his word was upon my tongue.
3 Mulungu wa Israeli anayankhula, Thanthwe la Israeli linati kwa ine: ‘Pamene munthu alamulira anthu mwachilungamo, pamene alamulira moopa Mulungu,
The God of Israel said, the Rock of Israel spake to me: One that ruleth over men righteously, that ruleth in the fear of God,
4 amakhala ngati kuwala kwa mmamawa, mmawa wopanda mitambo, monga kuwala pamene mvula yaleka kugwa imene imameretsa udzu mʼnthaka.’
[He shall be] as the light of the morning, when the sun riseth, a morning without clouds; [when] the tender grass [springeth] out of the earth, through clear shining after rain.
5 “Kodi banja langa silolungama pamaso pa Mulungu? Kodi Iye sanachite pangano losatha ndi ine, lokonzedwa ndi lotetezedwa mbali zonse? Kodi sadzakwaniritsa chipulumutso changa, ndi kundipatsa chokhumba changa chilichonse?
Verily my house is not so with God; yet he hath made with me an everlasting covenant, ordered in all things, and sure: for it is all my salvation, and all [my] desire, although he maketh it not to grow.
6 Koma anthu oyipa ndiwo ayenera kutayidwa kunja ngati minga, imene sitengedwa ndi manja.
But the ungodly shall be all of them as thorns to be thrust away, for they cannot be taken with the hand:
7 Aliyense amene wayikhudza mingayo amayidula pogwiritsa ntchito chigwandali kapena ndodo ya mkondo; nayitentha pa moto.”
But the man that toucheth them must be armed with iron and the staff of a spear; and they shall be utterly burned with fire in [their] place.
8 Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yosebu-Basebeti wa ku Takemoni mkulu wa atsogoleri a ankhondo atatu. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 800 nthawi imodzi.
These be the names of the mighty men whom David had: Josheb-basshebeth a Tahchemonite, chief of the captains; the same was Adino the Eznite, against eight hundred slain at one time.
9 Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi. Monga mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu a Davide, iye anali ndi Davide pamene anazunza Afilisti amene anasonkhana ku Pasi-Damimu kuchita nkhondo. Kenaka ankhondo a Israeli anabwerera mʼmbuyo.
And after him was Eleazar the son of Dodai the son of an Ahohite, one of the three mighty men with David, when they defied the Philistines that were there gathered together to battle, and the men of Israel were gone away:
10 Koma iye anayima osasuntha ndipo anakantha Afilisti mpaka mkono wake unatopa ndipo unakanirira ku lupanga lake. Yehova anapereka chigonjetso chachikulu pa tsiku limenelo. Asilikali anabwerera kwa Eliezara, kukatenga katundu wa anthu ophedwa.
He arose, and smote the Philistines until his hand was weary, and his hand clave unto the sword: and the LORD wrought a great victory that day; and the people returned after him only to spoil.
11 Wotsatana naye anali Sama mwana wa Age Mharari. Pamene Afilisti anasonkhana pamalo pamene panali munda wa mphodza, ankhondo a Israeli anathawa Afilistiwo.
And after him was Shammah the son of Agce a Hararite. And the Philistines were gathered together into a troop, where was a plot of ground full of lentils; and the people fled from the Philistines.
12 Koma Sama anayima pakati pa mundawo. Iye anawuteteza nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
But he stood in the midst of the plot, and defended it, and slew the Philistines: and the LORD wrought a great victory.
13 Pa nthawi yokolola, atatu mwa atsogoleri makumi atatu anabwera kwa Davide ku phanga la Adulamu, pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
And three of the thirty chief went down, and came to David in the harvest time unto the cave of Adullam; and the troop of the Philistines were encamped in the valley of Rephaim.
14 Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
And David was then in the hold, and the garrison of the Philistines was then in Beth-lehem.
15 Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
And David longed and said, Oh that one would give me water to drink of the well of Beth-lehem which is by the gate!
16 Choncho anthu amphamvu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
And the three mighty men brake through the host of the Philistines, and drew water out of the well of Beth-lehem, that was by the gate, and took it, and brought it to David: but he would not drink thereof, but poured it out unto the LORD.
17 Iye anati, “Inu Yehova, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi awa si magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Ndipo Davide sanamwe madziwo. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
And he said, Be it far from me, O LORD, that I should do this: [shall I drink] the blood of the men that went in jeopardy of their lives? therefore he would not drink it. These things did the three mighty men.
18 Abisai mʼbale wa Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300, choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
And Abishai, the brother of Joab, the son of Zeruiah, was chief of the three. And he lifted up his spear against three hundred and slew them, and had a name among the three.
19 Kodi iyeyo sanali wolemekezeka koposa? Iye anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
Was he not most honourable of the three? therefore he was made their captain: howbeit he attained not unto the [first] three.
20 Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
And Benaiah the son of Jehoiada, the son of a valiant man of Kabzeel, who had done mighty deeds, he slew the two [sons of] Ariel of Moab: he went down also and slew a lion in the midst of a pit in time of snow:
21 Ndipo iye anakanthanso Mwigupto wamkulu msinkhu. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
And he slew an Egyptian, a goodly man: and the Egyptian had a spear in his hand; but he went down to him with a staff, and plucked the spear out of the Egyptian’s hand, and slew him with his own spear.
22 Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
These things did Benaiah the son of Jehoiada, and had a name among the three mighty men.
23 Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu aja, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
He was more honourable than the thirty, but he attained not to the [first] three. And David set him over his guard.
24 Mʼgulu la anthu makumi atatu aja munalinso awa: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
Asahel the brother of Joab was one of the thirty; Elhanan the son of Dodo of Beth-lehem;
25 Sama Mharodi, Elika Mherodi,
Shammah the Harodite, Elika the Harodite;
26 Helezi Mpaliti, Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa,
Helez the Paltite, Ira the son of Ikkesh the Tekoite;
27 Abiezeri wa ku Anatoti, Sibekai Mhusati,
Abiezer the Anathothite, Mebunnai the Hushathite;
28 Zalimoni Mwahohi, Maharai Mnetofa,
Zalmon the Ahohite, Maharai the Netophathite;
29 Heledi mwana wa Baana Mnetofa, Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini,
Heleb the son of Baanah the Netophathite, Ittai the son of Ribai of Gibeah of the children of Benjamin;
30 Benaya Mpiratoni, Hidayi wa ku zigwa za Gaasi.
Benaiah a Pirathonite, Hiddai of the brooks of Gaash;
31 Abi-Aliboni Mwaribati, Azimaveti Mbarihumi,
Abi-albon the Arbathite, Azmaveth the Barhumite;
32 Eliyahiba Msaaliboni, ana a Yaseni, Yonatani,
Eliahba the Shaalbonite, the sons of Jashen, Jonathan;
33 mwana wa Sama Mharari, Ahiamu mwana wa Sarari Mharari,
Shammah the Hararite, Ahiam the son of Sharar the Ararite;
34 Elifeleti mwana wa Ahasibai Mmaakati, Eliamu mwana wa Ahitofele Mgiloni,
Eliphelet the son of Ahasbai, the son of the Maacathite, Eliam the son of Ahithophel the Gilonite;
35 Heziro wa ku Karimeli, Paarai Mwaribi,
Hezro the Carmelite, Paarai the Arbite;
36 Igala mwana wa Natani wa ku Zoba, mwana wa Hagiri,
Igal the son of Nathan of Zobah, Bani the Gadite;
37 Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya,
Zelek the Ammonite, Naharai the Beerothite, armourbearers to Joab the son of Zeruiah;
38 Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
Ira the Ithrite, Gareb the Ithrite;
39 ndi Uriya Mhiti. Onse pamodzi analipo 37.
Uriah the Hittite: thirty and seven in all.

< 2 Samueli 23 >