< 2 Samueli 22 >
1 Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
I izgovori David Gospodu rijeèi ove pjesme, kad ga izbavi Gospod iz ruku svijeh neprijatelja njegovijeh i iz ruke Saulove;
2 Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
I reèe: Gospod je moja stijena i grad moj i izbavitelj moj.
3 Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
Bog je stijena moja, u njega æu se uzdati, štit moj i rog spasenja mojega, zaklon moj i utoèište moje, spasitelj moj, koji me izbavlja od sile.
4 “Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
Prizivljem Gospoda, kojega valja hvaliti, i opraštam se neprijatelja svojih.
5 “Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
Jer obuzeše me smrtni bolovi, potoci nevaljalijeh ljudi uplašiše me.
6 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol )
Bolovi grobni opkoliše me, stegoše me zamke smrtne. (Sheol )
7 “Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
U tjeskobi svojoj prizvah Gospoda, i k Bogu svojemu povikah, on èu iz dvora svojega glas moj, i vika moja doðe mu do ušiju.
8 “Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
Zatrese se i pokoleba se zemlja, temelji nebesima zadrmaše se i pomjeriše se, jer se on razgnjevi.
9 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
Podiže se dim iz nozdara njegovijeh i iz usta njegovijeh oganj koji proždire, živo ugljevlje otskakaše od njega.
10 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
Savi nebesa i siðe; a mrak bijaše pod nogama njegovijem.
11 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
I sjede na heruvima i poletje, i pokaza se na krilima vjetrnijem.
12 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
Od mraka naèini oko sebe šator, od mraènijeh voda, oblaka vazdušnijeh.
13 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
Od sijevanja pred njim goraše živo ugljevlje.
14 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
Zagrmje s nebesa Gospod, i višnji pusti glas svoj.
15 Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
Pusti strijele svoje, i razmetnu ih; munje, i razasu ih.
16 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
Pokazaše se dubine morske, i otkriše se temelji vasiljenoj od prijetnje Gospodnje, od dihanja duha iz nozdara njegovijeh.
17 “Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
Tada pruži s visine ruku i uhvati me, izvuèe me iz vode velike.
18 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
Izbavi me od neprijatelja mojega silnoga i od mojih nenavidnika, kad bijahu jaèi od mene.
19 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
Ustaše na me u dan nevolje moje, ali mi Gospod bi potpora.
20 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
I izvede me na prostrano mjesto, izbavi me, jer sam mu mio.
21 “Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
Dade mi Gospod po pravdi mojoj, po èistoti ruku mojih dariva me.
22 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
Jer se držah putova Gospodnjih, i ne odmetnuh se Boga svojega.
23 Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
Nego su svi zakoni njegovi preda mnom, i zapovijesti njegovijeh ne uklanjam od sebe.
24 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
I bih mu vjeran, i èuvah se od bezakonja svojega.
25 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
Dade mi Gospod po pravdi mojoj, po èistoti mojoj pred oèima njegovima.
26 “Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
Sa svetima postupaš sveto, s èovjekom vjernijem vjerno;
27 Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
S èistijem èisto postupaš, a s nevaljalijem nasuprot njemu.
28 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
Jer pomažeš narodu nevoljnom, a na ponosite spuštaš oèi svoje i ponižavaš ih.
29 Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
Ti si vidjelo moje, Gospode, i Gospod prosvjetljuje tamu moju.
30 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
S tobom razbijam vojsku, s Bogom svojim skaèem preko zida.
31 “Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
Put je Božji vjeran, rijeè Gospodnja èista. On je štit svjema koji se uzdaju u nj.
32 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
Jer ko je Bog osim Gospoda? i ko je stijena osim Boga našega?
33 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
Bog je krjepost moja i sila moja, i èini da mi je put bez mane.
34 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
Daje mi noge kao u jelena, i na visine moje stavlja me.
35 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
Uèi ruke moje boju, te lome luk mjedeni mišice moje.
36 Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
Ti mi daješ štit spasenja svojega, i milost tvoja èini me velika.
37 Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
Širiš korake moje poda mnom, te se ne omièu gležnji moji.
38 “Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
Tjeram neprijatelje svoje, i potirem ih, i ne vraæam se dokle ih ne istrijebim.
39 Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
I istrebljujem ih, i obaram ih da ne mogu ustati, nego padaju pod noge moje.
40 Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
Jer me ti opasuješ snagom za boj: koji ustanu na me, obaraš ih poda me.
41 Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
Neprijatelja mojih pleæi ti mi obraæaš, i potirem nenavidnike svoje.
42 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
Obziru se, ali nema pomagaèa: vièu ka Gospodu, ali ih ne sluša.
43 Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
Satirem ih kao prah zemaljski, kao blato po ulicama gazim ih i razmeæem.
44 “Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
Ti me izbavljaš od bune naroda mojega, èuvaš me da sam glava narodima; narod kojega ne poznavah služi mi.
45 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
Tuðini laskaju mi, èujuæi pokoravaju mi se.
46 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
Tuðini blijede, dršæu u gradovima svojim.
47 “Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
Živ je Gospod, i da je blagoslovena stijena moja. Da se uzvisi Bog, stijena spasenja mojega.
48 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
Bog, koji mi daje osvetu, i pokorava mi narode,
49 amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
Koji me izvodi iz neprijatelja mojih, i podiže me nad one koji ustaju na me, i od èovjeka žestoka izbavlja me.
50 Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
Toga radi hvalim te, Gospode, po narodima, i pojem imenu tvojemu,
51 “Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”
Koji slavno izbavljaš cara svojega, i èiniš milost pomazaniku svojemu Davidu i sjemenu njegovu dovijeka.