< 2 Samueli 22 >

1 Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
וידבר דוד ליהוה את דברי השירה הזאת ביום הציל יהוה אתו מכף כל איביו ומכף שאול
2 Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
ויאמר יהוה סלעי ומצדתי ומפלטי לי
3 Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
אלהי צורי אחסה בו מגני וקרן ישעי משגבי ומנוסי משעי מחמס תשעני
4 “Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
מהלל אקרא יהוה ומאיבי אושע
5 “Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
כי אפפני משברי מות נחלי בליעל יבעתני
6 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
חבלי שאול סבני קדמני מקשי מות (Sheol h7585)
7 “Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
בצר לי אקרא יהוה ואל אלהי אקרא וישמע מהיכלו קולי ושועתי באזניו
8 “Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
ותגעש (ויתגעש) ותרעש הארץ מוסדות השמים ירגזו ויתגעשו כי חרה לו
9 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
עלה עשן באפו ואש מפיו תאכל גחלים בערו ממנו
10 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
ויט שמים וירד וערפל תחת רגליו
11 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
וירכב על כרוב ויעף וירא על כנפי רוח
12 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
וישת חשך סביבתיו סכות חשרת מים עבי שחקים
13 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
מנגה נגדו בערו גחלי אש
14 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
ירעם מן שמים יהוה ועליון יתן קולו
15 Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
וישלח חצים ויפיצם ברק ויהמם (ויהם)
16 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
ויראו אפקי ים יגלו מסדות תבל בגערת יהוה מנשמת רוח אפו
17 “Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
ישלח ממרום יקחני ימשני ממים רבים
18 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
יצילני מאיבי עז משנאי כי אמצו ממני
19 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
יקדמני ביום אידי ויהי יהוה משען לי
20 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
ויצא למרחב אתי יחלצני כי חפץ בי
21 “Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
יגמלני יהוה כצדקתי כבר ידי ישיב לי
22 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
כי שמרתי דרכי יהוה ולא רשעתי מאלהי
23 Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
כי כל משפטו לנגדי וחקתיו לא אסור ממנה
24 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
ואהיה תמים לו ואשתמרה מעוני
25 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
וישב יהוה לי כצדקתי כברי לנגד עיניו
26 “Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
עם חסיד תתחסד עם גבור תמים תתמם
27 Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
עם נבר תתבר ועם עקש תתפל
28 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
ואת עם עני תושיע ועיניך על רמים תשפיל
29 Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
כי אתה נירי יהוה ויהוה יגיה חשכי
30 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
כי בכה ארוץ גדוד באלהי אדלג שור
31 “Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
האל תמים דרכו אמרת יהוה צרופה-- מגן הוא לכל החסים בו
32 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
כי מי אל מבלעדי יהוה ומי צור מבלעדי אלהינו
33 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
האל מעוזי חיל ויתר תמים דרכו (דרכי)
34 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
משוה רגליו (רגלי) כאילות ועל במתי יעמדני
35 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
מלמד ידי למלחמה ונחת קשת נחושה זרעתי
36 Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
ותתן לי מגן ישעך וענתך תרבני
37 Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
תרחיב צעדי תחתני ולא מעדו קרסלי
38 “Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
ארדפה איבי ואשמידם ולא אשוב עד כלותם
39 Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
ואכלם ואמחצם ולא יקומון ויפלו תחת רגלי
40 Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
ותזרני חיל למלחמה תכריע קמי תחתני
41 Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
ואיבי תתה לי ערף משנאי ואצמיתם
42 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
ישעו ואין משיע אל יהוה ולא ענם
43 Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
ואשחקם כעפר ארץ כטיט חוצות אדקם ארקעם
44 “Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
ותפלטני מריבי עמי תשמרני לראש גוים עם לא ידעתי יעבדני
45 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
בני נכר יתכחשו לי לשמוע אזן ישמעו לי
46 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
בני נכר יבלו ויחגרו ממסגרותם
47 “Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
חי יהוה וברוך צורי וירם אלהי צור ישעי
48 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
האל הנתן נקמת לי ומריד עמים תחתני
49 amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
ומוציאי מאיבי ומקמי תרוממני מאיש חמסים תצילני
50 Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
על כן אודך יהוה בגוים ולשמך אזמר
51 “Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”
מגדיל (מגדול) ישועות מלכו ועשה חסד למשיחו לדוד ולזרעו עד עולם

< 2 Samueli 22 >