< 2 Samueli 22 >

1 Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
Or, David dit au Seigneur les paroles de ce cantique, au jour où le Seigneur le délivra de la main de tous ses ennemis et de la main de Saül.
2 Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
Et il dit: Le Seigneur est mon rocher, et ma force, et mon sauveur.
3 Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
Dieu est mon fort, j’espérerai en lui; il est mon bouclier, l’appui de mon salut; c’est lui qui m’élève, et qui est mon refuge; mon Sauveur, vous me délivrerez de l’iniquité.
4 “Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
J’invoquerai le Seigneur, digne de louanges, et je serai délivré de mes ennemis.
5 “Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
Parce que les brisements de la mort m’ont environné, les torrents de Bélial m’ont épouvanté.
6 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
Les liens de l’enfer m’ont environné, les lacs de la mort m’ont enveloppé. (Sheol h7585)
7 “Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
Dans ma tribulation, j’invoquerai le Seigneur, et c’est vers mon Dieu que je crierai, et il exaucera ma voix de son temple, et mon cri viendra jusqu’à ses oreilles.
8 “Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
La terre s’est émue et a tremblé; les fondements des montagnes ont été agités et ébranlés, parce que le Seigneur s’est irrité contre elles.
9 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
Une fumée est montée de ses narines, et un feu sorti de sa bouche dévorera; des charbons en ont été allumés.
10 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
Il a incliné les cieux, et il est descendu, et un nuage obscur était sous ses pieds.
11 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
Il a monté sur des chérubins, et il a pris son vol, et il s’est élancé sur des ailes de vent.
12 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
Il a mis des ténèbres autour de lui pour se cacher; il a fait distiller des eaux des nuées des cieux.
13 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
À la lumière qui éclate en sa présence, des charbons de feu se sont allumés.
14 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
Le Seigneur tonnera du ciel, et le Très-Haut élèvera sa voix.
15 Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
Il a lancé des flèches, et il les a dissipés; la foudre, et il les a consumés.
16 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
Alors ont paru les abîmes de la mer, les fondements du monde ont été mis à nu, à la menace du Seigneur, au souffle du vent de sa colère.
17 “Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
Il a envoyé d’en haut, et il m’a pris, et il m’a retiré d’un gouffre d’eaux.
18 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
Il m’a délivré de mon ennemi très puissant, et de ceux qui me haïssaient, parce qu’ils étaient plus forts que moi.
19 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
Il m’a prévenu au jour de mon affliction, et le Seigneur s’est fait mon appui.
20 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
Et il m’a mis au large; il m’a délivré, parce que je lui ai plu.
21 “Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
Le Seigneur me rétribuera selon ma justice, et il me rendra selon la pureté de mes mains,
22 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
Parce que j’ai gardé les voies du Seigneur, et que je n’ai pas agi avec impiété en m’éloignant de mon Dieu.
23 Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
Tous ses jugements sont devant mes yeux, et je n’ai point éloigné ses préceptes de moi.
24 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
Et je serai parfait avec lui, et je me garderai de mon iniquité.
25 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
Et le Seigneur me rendra selon ma justice, et selon la pureté de mes mains devant ses yeux.
26 “Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
Avec un saint vous serez saint, et avec un fort, parfait.
27 Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
Avec un homme excellent, vous serez excellent, et avec un pervers, vous agirez selon sa perversité.
28 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
Vous sauverez un peuple pauvre, et par vos yeux vous humilierez les superbes.
29 Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
Parce que c’est vous, Seigneur, qui êtes ma lampe; vous, qui illuminez mes ténèbres.
30 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
Car avec vous je courrai tout prêt au combat; avec mon Dieu, je franchirai un mur.
31 “Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
Dieu, sa voie est sans tache, la parole du Seigneur est éprouvée par le feu; il est le bouclier de tous ceux qui espèrent en lui.
32 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
Qui est Dieu, excepté le Seigneur? et qui est le fort, excepté notre Dieu?
33 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
Le Dieu qui m’a revêtu de force, et qui m’a aplani ma voie parfaite;
34 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
Egalant mes pieds aux cerfs, et m’établissant sur mes lieux élevés;
35 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
Instruisant mes mains au combat, et rendant mes bras comme un arc d’airain.
36 Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
Vous m avez donné le bouclier de votre salut, et votre bonté ma multiplié.
37 Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
Vous agrandirez mes pas sous moi, et mes talons ne chancelleront point.
38 “Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
Je poursuivrai mes ennemis, et je les briserai; et je ne reviendrai point jusqu’à ce que je les détruise.
39 Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
Je les détruirai et les briserai, de manière qu’ils ne se relèvent point; ils tomberont sous mes pieds.
40 Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
Vous m’avez revêtu de force pour le combat, vous avez fait plier sous moi ceux qui me résistaient.
41 Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
Vous m’avez livré mes ennemis par derrière; ceux qui me haïssaient, et je les exterminerai.
42 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
Ils crieront, et il n’y aura personne qui les sauve; ils crieront vers le Seigneur, et il ne les exaucera pas.
43 Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
Je les dissiperai comme de la poussière de la terre, et je les broierai comme de la boue de rues et les briserai.
44 “Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
Vous me sauverez des contradictions de mon peuple; vous me garderez pour chef de nations; un peuple que j’ignore me servira.
45 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
Des fils d’étranger me résisteront; en écoutant de leurs oreilles, ils m’obéiront.
46 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
Des fils d’étranger se sont dispersés, et ils seront resserrés dans leurs défilés.
47 “Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
Le Seigneur vit, et béni mon Dieu! et le Dieu fort de mon salut sera exalté;
48 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
Vous, le Dieu qui me donnez des vengeances, et qui abattez des peuples sous moi;
49 amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
Qui m’arrachez à mes ennemis et qui m’élevez au-dessus de ceux qui me résistent: vous me délivrerez de l’homme inique.
50 Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
À cause de cela, je vous confesserai. Seigneur, parmi les nations, et je chanterai votre nom,
51 “Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”
Qui exalte les victoires de son roi, et qui fait miséricorde à son christ, David, et à sa postérité pour toujours.

< 2 Samueli 22 >