< 2 Samueli 22 >

1 Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
And David spoke to Jehovah the words of this song in the day that Jehovah delivered him out of the hand of all his enemies, and out of the hand of Saul:
2 Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
And he said, Jehovah is my rock, and my fortress, and my deliverer, even mine.
3 Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
God, my rock, in him I will take refuge, my shield, and the horn of my salvation, my high tower, and my refuge, my savior. Thou save me from violence.
4 “Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
I will call upon Jehovah, who is worthy to be praised. So I shall be saved from my enemies.
5 “Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
For the waves of death encompassed me. The floods of ungodliness made me afraid.
6 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
The cords of Sheol were round about me. The snares of death came upon me. (Sheol h7585)
7 “Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
In my distress I called upon Jehovah. Yea, I called to my God. And he heard my voice out of his temple, and my cry came into his ears.
8 “Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
Then the earth shook and trembled, the foundations of heaven quaked and were shaken, because he was angry.
9 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
There went up a smoke out of his nostrils, and fire out of his mouth devoured. Coals were kindled by it.
10 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
He bowed the heavens also, and came down, and thick darkness was under his feet.
11 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
And he rode upon a cherub, and flew. Yea, he was seen upon the wings of the wind.
12 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
And he made darkness pavilions round about him, gathering of waters, thick clouds of the skies.
13 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
At the brightness before him coals of fire were kindled.
14 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
Jehovah thundered from heaven, and the Most High uttered his voice.
15 Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
And he sent out arrows, and scattered them, lightning, and discomfited them.
16 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
Then the channels of the sea appeared. The foundations of the world were laid bare by the rebuke of Jehovah, at the blast of the breath of his nostrils.
17 “Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
He sent from on high, he took me. He drew me out of many waters.
18 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
He delivered me from my strong enemy, from those who hated me, for they were too mighty for me.
19 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
They came upon me in the day of my calamity, but Jehovah was my support.
20 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
He brought me forth also into a large place. He delivered me, because he delighted in me.
21 “Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
Jehovah rewarded me according to my righteousness. According to the cleanness of my hands he has rewarded me.
22 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
For I have kept the ways of Jehovah, and have not wickedly departed from my God.
23 Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
For all his ordinances were before me. And as for his statutes, I did not depart from them.
24 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
I was also perfect toward him, and I kept myself from my iniquity.
25 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
Therefore Jehovah has recompensed me according to my righteousness, according to my cleanness in his eyesight.
26 “Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
With the merciful thou will show thyself merciful. With the perfect man thou will show thyself perfect.
27 Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
With the pure thou will show thyself pure. And with the perverse thou will show thyself contrary.
28 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
And the afflicted people thou will save, but thine eyes are upon the haughty, that thou may bring them down.
29 Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
For thou are my lamp, O Jehovah. And Jehovah will lighten my darkness.
30 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
For by thee I run upon a troop. By my God do I leap over a wall.
31 “Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
As for God, his way is perfect. The word of Jehovah is tried. He is a shield to all those who take refuge in him.
32 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
For who is God, except Jehovah? And who is a rock, except our God?
33 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
God is my strong fortress, and he guides the perfect in his way.
34 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
He makes his feet like hinds' feet, and sets me upon my high places.
35 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
He teaches my hands to war, so that my arms bend a bow of brass.
36 Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
Thou have also given me the shield of thy salvation, and thy gentleness has made me great.
37 Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
Thou have enlarged my steps under me, and my feet have not slipped.
38 “Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
I have pursued my enemies, and destroyed them, neither did I turn again till they were consumed.
39 Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
And I have consumed them, and smitten them through, so that they cannot arise. Yea, they are fallen under my feet.
40 Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
For thou have girded me with strength to the battle. Thou have subdued under me those who rose up against me.
41 Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
Thou have also made my enemies turn their backs to me, that I might cut off those who hate me.
42 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
They looked, but there was none to save; even to Jehovah, but he did not answer them.
43 Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
Then I beat them small as the dust of the earth. I crushed them as the mire of the streets, and spread them abroad.
44 “Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
Thou have also delivered me from the strivings of my people. Thou have kept me to be the head of the nations. A people whom I have not known shall serve me.
45 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
The foreigners shall submit themselves to me. As soon as they hear of me, they shall obey me.
46 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
The foreigners shall fade away, and shall come trembling out of their hiding places.
47 “Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
Jehovah lives. And blessed be my rock. And exalted be God, the rock of my salvation,
48 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
Even the God who executes vengeance for me, and who brings down peoples under me,
49 amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
and who brings me forth from my enemies. Yea, thou lift me up above those who rise up against me. Thou deliver me from the violent man.
50 Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
Therefore I will give thanks to thee, O Jehovah, among gentiles, and will sing praises to thy name.
51 “Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”
He gives great deliverance to his king, and shows loving kindness to his anointed, to David and to his seed, for evermore.

< 2 Samueli 22 >