< 2 Samueli 22 >

1 Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
當上主救達味脫離了仇敵和撒烏耳的毒手時,達味向上主唱了詩歌說:
2 Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
「上主,我的盤石,我的保障,我的避難所;
3 Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
天主是我所倚靠的盤石,是我的盾牌,我的大救主,我的堡壘,我的藏身處。我的救主,是你救我脫離了強暴。
4 “Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
我一呼求應受頌揚的上主,我便獲救,脫離了我的仇敵。
5 “Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
死亡的波濤圍繞我,凶險的急流驚嚇我,
6 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
陰府的繩索纏住中我,死亡的羅網絆住我; (Sheol h7585)
7 “Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
在急難中我呼求上主,向我的天主呼號,衪由殿中聽了我的聲音,我的呼聲達入衪耳中。
8 “Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
因衪盛大作,大地震動戢慄,上主的基礎動盪搖撼,
9 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
由衪的鼻孔湧出濃煙,由衪的口中噴出烈火,由衪的身上射出火炭,
10 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
使天低垂親自降下,在衪的腳下濃雲密佈。
11 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
衪乘坐革魯賓飛騰,藉著風的翼羽翱翔。
12 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
衪四周以黑暗做帷幔,以豪雨濃雲為帳幕。
13 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
閃電在衪前閃爍,紅炭發出了火光。
14 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
上主由高天興雷,至高者發出了呼聲。
15 Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
衪射出羽箭,使敵人四散,發閃電,使敵人驚擾。
16 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
上主的呵斥一發,鼻孔的怒氣一出,蒼海的海低即出現,大地的地基也外露。
17 “Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
衪由高處伸手將我拉住,由大水中將我提出。
18 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
救我脫離了我的勁敵,擺脫了強於我的仇人。
19 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
他們在我困厄之日,襲擊了我,然而上主卻作了我的後盾;
20 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
衪引我步坦途,因喜愛我而救了我。
21 “Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
上主照我的正義酬報了我,按我雙手的清白報答了我;
22 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
因我遵行了上主的正道,沒有作惡離棄我的天主。
23 Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
衪的一切法令在我前,我未曾違過衪的誡命;
24 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
我衪前常保成全,自知提防各種不義。
25 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
因此,上主照我的正義,我在衪的純潔,賞報了我。
26 “Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
仁慈的人,你待他仁慈;正直的人,你待他正直;
27 Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
純的人,你待他純樸;乖戾的人,你待他乖戾。
28 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
卑微的人,你必拯救;傲慢的人,你必睥視。
29 Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
上主,你是我的火炬,我的天主,照明我的黑暗。
30 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
仗著你,我衝入了敵營;靠著我的天主,我跳過了牆垣。
31 “Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
天主的道路是完善的;上主的言語是純淨的;凡投衪的人,衪怍他們的後盾。
32 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
上主以外,還有誰是天主﹖除我的的天主外,還有誰的盤石﹖
33 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
是天主賜我毅力,使我一路順利,
34 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
使我的腳快如鹿蹄,使我屹立高地,
35 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
教導我手作戰,使臂膊能開銅弓。
36 Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
你你的救生盾賜了我,你的長甲作了我的掩護。
37 Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
你為我的腳步拓寬了路,我的腳從未顛簸。
38 “Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
我追趕仇敵,消滅他們;不滅絕他們,決不返回。
39 Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
我將他們打得一蹶不振,盡都倒斃在我腳下
40 Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
你賜我毅力勇作戰,把我的對手屈伏我下,
41 Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
使我的敵人在 前轉背而逃,使我殲滅了一切仇恨我的人。
42 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
他們呼號,卻無人施救;呼號上主,也不獲應允。
43 Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
我搗碎他們地上的灰塵,踐踏他們像道上的泥土。
44 “Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
你由百姓的叛亂中救拔了我,立我做了列國的首領;我不知道的人民竟給我服役;
45 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
外邦的子民諂媚奉承我,一聽到是我,即服從我;
46 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
外的子民驚惶失色,戰戰兢兢走的堡壘。
47 “Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
上主萬歲! 願我的盤石受讚美,願救我的的天主受頌揚!
48 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
天主是你為我報了仇,使萬民屈伏於我,
49 amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
是你救我脫離了我的仇敵,提拔我凌駕我的對手之上,救我脫免了強暴的人。
50 Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
為此,上主! 我要在異民中稱謝你,歌頌你的聖名。
51 “Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”
因為衪使自己的君大獲勝利,對自己的受傅者達味和他的子孫,廣施仁慈,直到永遠」。

< 2 Samueli 22 >