< 2 Samueli 21 >

1 Pa nthawi ya ulamuliro wa Davide kunali njala kwa zaka zitatu zotsatana. Kotero Davide anapemphera kwa Yehova. Yehova anati, “Izi zachitika chifukwa chakuti Sauli ndi banja lake akanali ndi mlandu wakupha Agibiyoni.”
Also hungur was maad in the lond of Israel in the daies of Dauid, bi thre yeer contynueli. And Dauid counselide the answere of the Lord; and the Lord seide, For Saul, and his hows, and blood, for he killide men of Gabaon.
2 Mfumu inayitanitsa Agibiyoni ndipo inayankhula nawo. (Tsono Agibiyoni sanali Aisraeli, koma otsala mwa Aamori. Aisraeli analumbira kuwasiya ndi moyo, koma Sauli chifukwa cha chikondi cha pa Israeli ndi Yuda, anafuna kuwawonongeratu).
Therfor whanne Gabaonytis weren clepid, the kyng seide to hem; sotheli Gabaonytis ben not of the sones of Israel, but thei ben the relikys of Ammorreis; and the sones of Israel hadden swore to hem, `that is, that thei schulden not `be slayn, and Saul wolde smyte hem for feruent loue, as for the sones of Israel and of Juda;
3 Davide anafunsa Agibiyoni kuti, “Kodi ine ndikuchitireni chiyani? Ndipepese bwanji kuti inu mudalitse cholowa cha Yehova?”
therfor Dauid seide to Gabaonytis, What schal Y do to you, and what schal be youre amendis, that ye blesse the eritage of the Lord?
4 Agibiyoni anamuyankha kuti, “Ife tilibe ufulu woti nʼkulamula Sauli ndi banja lake kuti atipatse siliva kapena golide, tilibenso ufulu woti nʼkupha wina aliyense mu Israeli.” Davide anafunsa, “Mukufuna ine ndikuchitireni chiyani?”
And Gabaonytis seiden to hym, No questioun is to vs on gold and siluer, but ayens Saul, and ayens his hows; nether we wolen, that a man of Israel be slayn. To whiche the kyng seide, What therfor wolen ye, that Y do to you?
5 Iwo anayankha mfumu kuti, “Tsono za munthu amene anatiwononga ndi kukonza chiwembu choti titheretu ndi kukhala wopanda malo mu Israeli,
Whiche seiden to the king, We owen to do awei so the man, that `al to brak ethir defoulide vs, and oppresside wickidli, that not oon sotheli be residue of his generacioun in alle the coostis of Israel.
6 mutipatse adzukulu ake aamuna asanu ndi awiri kuti tiwaphe ndi kuwapereka pamaso pa Yehova ku Gibeya wa Sauli, wosankhidwa wa Yehova.” Choncho mfumu inati, “Ine ndidzakupatsani.”
Seuene men of hise sones be youun to vs, that we `crucifie hem to the Lord in Gabaa of Saul, sum tyme the chosun man of the Lord. And the kyng seide, Y schal yyue.
7 Koma mfumu inasunga Mefiboseti mwana wa Yonatani, mwana wa Sauli, chifukwa cha kulumbira kumene mfumu Davide ndi Yonatani mwana wa Sauli anachita pamaso pa Yehova.
And the kyng sparide Myphibosech, sone of Jonathas, sone of Saul, for the ooth of the Lord, that was bitwixe Dauid and bitwixe Jonathas, sone of Saul.
8 Ndipo mfumu inatenga Arimoni ndi Mefiboseti, ana aamuna awiri a Rizipa, mwana wamkazi wa Ayiwa, amene anaberekera Sauli pamodzi ndi ana asanu a Merabi mwana wamkazi wa Sauli, amene anabereka Adirieli mwana wa Barizilai Mmeholati.
Therfor the kyng took twei sones of Respha, douyter of Ahira, whiche sche childide to Saul, Armony, and Mysphibosech; and he took fyue sones of Mychol, douyter of Saul, whiche sche gendride to Adriel, sone of Berzellai, that was of Molaty.
9 Iye anawapereka kwa anthu a ku Gibiyoni, amene anawapha nawayika pa phiri la Yehova. Onse asanu ndi awiri anafera limodzi. Iwo anaphedwa masiku oyamba kukolola barele.
And he yaf hem in to the hondis of Gabaonytis, whiche crucifieden tho sones in the hil bifor the Lord; and these seuene felden slayn togidere in the daies of the firste rep, whanne the repyng of barli bigan.
10 Rizipa mwana wamkazi wa Ayiwa anatenga chiguduli ndi kudziyalira pa mwala (pamene panali mitemboyo). Kuyambira nthawi yoyamba kukolola mpaka pamene mvula inayambanso kugwa, iye sanalole kuti mbalame zikhudze mitemboyo masana kapena nyama zakuthengo usiku.
Forsothe Respha, douytir of Ahia, took an heire, and `araiede to hir silf a place aboue the stoon, fro the bigynnyng of heruest til watir droppide `on hem fro heuene; and sche suffride not briddis to tere hem bi dai, nether beestis bi nyyt.
11 Davide atawuzidwa zimene Rizipa mwana wamkazi wa Ayiwa, mzikazi wa Sauli anachita,
And tho thingis whiche Respha, secoundarie wijf of Saul, douytir of Ahia, hadde do, weren teld to Dauid.
12 anapita kukatenga mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani kwa anthu a ku Yabesi Giliyadi (iwo anawatenga mwamseri kuchoka pabwalo la ku Beti-Sani, kumene Afilisti anawapachika atapha Sauli ku Gilibowa).
And Dauid yede, and took the boonys of Saul, and the boonys of Jonathas, his sone, of the men of Jabes of Galaad; that hadden stole tho boonys fro the street of Bethsan, in which street the Filisteis hadden hangid hem, whanne thei hadden slayn Saul in Gelboe.
13 Davide anakatenga mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani kumeneko ndiponso mafupa otayidwa a amene anaphedwa nawasonkhanitsa pamodzi.
And Dauid bar out fro thennus the boonys of Saul, and the boonys of Jonathas, his sone; and thei gaderiden the boonys of hem that weren crucified, and birieden tho with the boonys of Saul and of Jonathas, his sone, in the lond of Beniamyn, in the side of the sepulcre of Cys, fadir of Saul.
14 Iwo anayika mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani mʼmanda a Kisi abambo ake a Sauli ku Zera mʼdziko la Benjamini, ndipo anachita zonse zimene mfumu inalamula. Atachita zimenezi, Mulungu anayankha pemphero lopempherera dzikolo.
And thei diden al thingis, what euer thingis the kyng comaundide; and the Lord dide mercy to the lond aftir these thingis.
15 Nthawi inanso panali nkhondo pakati pa Afilisti ndi Aisraeli, Davide anapita ndi ankhondo ake kukamenyana ndi Afilisti ndipo iye anatopa kwambiri.
Forsothe batel of Filisteis was maad eft ayens Israel; and Dauid yede doun, and hise seruauntis with hym, and fouyten ayen Filisteis.
16 Ndipo Isibi-Benobi, mmodzi mwa zidzukulu za Rafa, amene mkondo wake unkalemera makilogalamu atatu ndi theka ndipo analinso ndi lupanga latsopano, anati adzapha Davide.
Sotheli whanne Dauid failide, Jesbydenob, that was of the kyn of Arapha, that is, of giauntis, and the yrun of his spere peiside thre hundrid ouncis, and he was gird with a newe swerd, enforside to smyte Dauid.
17 Koma Abisai mwana wa Zeruya anabwera kudzapulumutsa Davide. Iye anamukantha Mfilisitiyo ndi kumupha. Pamenepo asilikali a Davide analumbira kwa iye kuti, “Inu simudzapita nafenso ku nkhondo, kuti nyale ya Israeli isadzazimitsidwe.”
And Abisai, sone of Saruye, was in help to Dauid; and he smoot and killide the Filistei. Than the men of Dauid sworen, and seiden, Now thou schalt not go out with vs in to batel, lest thou quenche the lanterne of Israel.
18 Patapita nthawi, panali nkhondo ina ndi Afilisti ku Gobu. Pa nthawi imeneyo Sibekai Mhusati anapha Safu, mmodzi mwa zidzukulu za Arefai.
Also the secounde batel was in Gob ayens Filisteis; thanne Sobothai of Osothai smoot Zephi, of the generacioun of Arapha, of the kyn of giauntis.
19 Pa nkhondo inanso ndi Afilisti ku Gobu, Elihanani mwana wa Yaare-Oregimu wa ku Betelehemu anapha Goliati Mgiti, amene anali ndi mkondo ngati ndodo yowombera nsalu.
Also the thridde batel was in Gob ayens Filisteis; in which batel a man youun of God, the sone of forest, a broiderer, a man of Bethleem, smoot Golyath of Geth, whos `schaft of spere was as a beem of webbis.
20 Pa nkhondo inanso imene inachitika ku Gati panali munthu wina wamtali kwambiri wa zala zisanu ndi chimodzi mʼmanja ndi mʼmapazi ndipo zonse pamodzi zinalipo 24. Iyenso anali chidzukulu cha Rafa.
The fourthe batel was in Geth; where ynne was an hiy man, that hadde sixe fyngris in the hondis and feet, that is, foure and twenti; and he was of the kyn of Arapha;
21 Pamene iye ankanyoza Aisraeli, Yonatani mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anamupha.
and he blasfemyde Israel; sotheli Jonathan, sone of Samaa, brother of Dauid, killide hym.
22 Anthu anayi amenewa anali zidzukulu za Rafa ku Gati, ndipo onse anaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.
These foure weren borun of Arapha in Geth, and thei felden doun in the hond of Dauid, and of hise seruauntis.

< 2 Samueli 21 >